< Pirmā Mozus 44 >

1 Un viņš pavēlēja tam, kas bija pār viņa namu, un sacīja: pildi to vīru maisus ar labību, cik tie var nest, un liec ikviena naudu viņa maisa virsgalā.
Pambuyo pake Yosefe analamulira wantchito wa mʼnyumba mwake kuti, “Adzazire chakudya anthuwa mʼmatumba mwawo monga mmene anganyamulire, ndipo uwayikire ndalama zawo pakamwa pa matumba awowo.
2 Un manu biķeri, to sudraba biķeri, liec tam jaunākam maisa virsgalā, arī viņa labības naudu. Un tas darīja pēc Jāzepa vārda, ko viņš bija sacījis.
Tsono uyike chikho changa cha siliva chija, pakamwa pa thumba la wamngʼono kwambiriyu pamodzi ndi ndalama zake za chakudya” Ndipo iye anachita monga Yosefe ananenera.
3 Rītā, gaismai austot, tie vīri tapa atlaisti līdz ar saviem ēzeļiem.
Mmawa kutacha anthu aja analoledwa kuti apite ndi abulu awo.
4 Bet tiem no pilsētas izejot un tāli vēl neesot, Jāzeps sacīja savam nama uzraugam: celies, dzenies tiem vīriem pakaļ, un tos panācis saki tiem: kādēļ esat atmaksājuši labu ar ļaunu?
Atangotuluka mu mzinda muja, koma asanapite patali, Yosefe anati kwa wantchito wake, “Nyamuka atsatire anthu aja msanga. Ndipo ukawapeza, uwafunse kuti, ‘Bwanji mwabwezera zoyipa ndi zabwino?
5 Vai šis nav tas, no kā mans kungs dzer? Un no tā viņš mēdz padzert. Jūs esat ļaunu darījuši, to darīdami.
Mwaberanji chikho chimene mbuye wanga amamweramo ndi kugwiritsa ntchito akafuna kuwombeza? Chimene mwachitachi ndi chinthu choyipa.’”
6 Un tas viņus panāca un viņiem sacīja šos vārdus.
Wantchito uja atawapeza ananena mawu anawuzidwa aja.
7 Tad viņi uz to sacīja: kāpēc mans kungs runā tādus vārdus? Ne mūžam tavi kalpi tādu darbu nedarīs.
Koma iwo anati kwa iye, “Kodi mbuye wanga mukuneneranji zimenezi? Sizingatheke ndi pangʼono pomwe kuti antchito anufe nʼkuchita zoterozo ayi!
8 Redzi, to naudu, ko esam atraduši savu maisu virsgalā, mēs tev atkal esam atnesuši no Kanaāna zemes, - kā tad mēs zagsim no tava kunga nama sudrabu vai zeltu?
Paja ife pobwera kuchokera ku Kanaani tinatenga ndalama kubwezera zimene tinazipeza mʼmatumba mwathu. Ndiye pali chifukwa chanji kuti tikabe siliva kapena golide mʼnyumba mwa mbuye wanu?
9 Pie kura no taviem kalpiem to atradīs, tas lai mirst, un mēs arī gribam būt par vergiem savam kungam.
Ngati wantchito wanu wina pano atapezeka nacho chikhocho, ameneyo aphedwe ndipo ena tonsefe tidzakhala akapolo anu, mbuye wathu.”
10 Un viņš sacīja: lai nu arī notiek pēc jūsu vārdiem: pie kura to atradīs, tas būs mans vergs, bet jūs būsiet svabadi.
Iye anati, “Chabwino, tsono zikhale monga mwaneneramu. Komatu aliyense amene angapezeke nacho chikhocho adzakhala kapolo wanga, ndipo ena nonsenu muzipita mwaufulu.”
11 Un tie steidzās un nocēla ikviens savu maisu zemē, un ikviens atraisīja savu maisu.
Tsono onse anafulumira kutsitsa pansi aliyense thumba lake ndi kulitsekula.
12 Un viņš pārmeklēja no tā vecākā iesākdams un pie tā jaunākā beigdams, un tas biķeris tapa atrasts Benjamina maisā.
Kenaka anayamba kufufuza, kuyambira pa wamkulu mpaka pa wamngʼono. Ndipo chikhocho chinapezeka mʼthumba mwa Benjamini.
13 Tad tie saplēsa savas drēbes un apkrāva ikviens savu ēzeli un griezās atpakaļ uz pilsētu.
Apo onse anangʼamba zovala zawo ndi chisoni. Ndipo anasenzetsa abulu katundu wawo nabwerera ku mzinda konkuja.
14 Un Jūda ar saviem brāļiem nāca Jāzepa namā, jo šis tur vēl bija, un tie nometās priekš viņa vaiga pie zemes.
Pamene Yuda ndi abale ake ankafika ku nyumba kwa Yosefe nʼkuti Yosefe akanali komweko. Ndipo anadzigwetsa pansi pamaso pake.
15 Un Jāzeps uz tiem sacīja: kas tas par darbu, ko jūs esat darījuši? Vai nezinājāt, ka tāds vīrs, kā es, tiešām to paredzēs?
Yosefe anafunsa kuti, “Nʼchiyani mwachitachi? Kodi simudziwa kuti munthu ngati ine ndikhoza kuona zinthu mwakuwombeza?”
16 Tad Jūda sacīja: ko lai sakām savam kungam, ko lai runājam un kā lai taisnojamies? Dievs tavu kalpu noziegumu ir atradis, redzi, mēs esam sava kunga vergi, - tā mēs, kā arī tas, pie kā tas biķeris atrasts.
Yuda anayankha, “Kodi tinganenenji kwa mbuye wanga? Tinena chiyani? Tingadzilungamitse bwanji? Mulungu waulula kulakwa kwa antchito anu. Ndipo tsopano ndife akapolo a mbuye wanga, ife tonse pamodzi ndi amene wapezeka ndi chikhocho.”
17 Tad viņš sacīja: nemūžam es to nedarīšu; tas vīrs, pie kā tas biķeris atrasts, tam būs man būt par vergu. Bet jūs ejat ar mieru pie sava tēva.
Koma Yosefe anati, “Sindingachite choncho ayi! Yekhayo amene wapezeka ndi chikhocho ndi amene akhale kapolo wanga. Ena nonsenu, bwererani kwa abambo anu mu mtendere.”
18 Tad Jūda pie tā piegāja un sacīja: ak mans kungs! Lūdzams, lai tavs kalps runā kādu vārdu priekš sava kunga ausīm, un neapskaities par savu kalpu, jo tu esi tik augsts kā Faraons.
Ndipo Yuda anamuyandikira iye nati, “Chonde mbuye wanga mulole kapolo wanune ndinene mawu pangʼono kwa mbuye wanga. Musandipsere mtima, kapolo wanune, popeza inu muli ngati Farao yemwe.
19 Mans kungs vaicāja savus kalpus un sacīja: vai jums ir tēvs vai brālis?
Mbuye wanga munafunsa akapolo anufe kuti, ‘Kodi muli ndi abambo anu kapena mʼbale wanu?’
20 Tad mēs sacījām savam kungam: mums ir vecs tēvs un viens zēns, kas tam vecumā dzimis, tas jaunākais, un viņa brālis ir miris, un tas ir viens pats no savas mātes atlicis, un viņa tēvs viņu mīļo.
Ndipo ife tinayankha, ‘Inde mbuye wathu, ife tili ndi abambo athu wokalamba, ndipo pali mwana wamwamuna wamngʼono amene anabadwa abambo athu atakalamba kale. Mʼbale wake anafa ndipo ndi yekhayo mʼmimba mwa amayi ake amene watsala ndipo abambo ake amamukonda.’
21 Tad tu sacīji saviem kalpiem: atvediet to pie manis, lai manas acis viņu redz.
“Ndipo inu munatiwuza kuti, ‘Mubwere naye kwa ine kuti ndidzamuone ndekha.’
22 Tad mēs sacījām uz savu kungu: tas zēns savu tēvu nevar atstāt; ja tas atstās savu tēvu, tad šis mirs.
Ife tinati, ‘Mbuye wathu, mnyamatayo sangasiye abambo ake, akawasiya ndiye kuti abambo akewo adzafa.’
23 Tad tu saviem kalpiem sacīji: ja jūsu jaunākais brālis ar jums neatnāk, tad jūs manu vaigu vairs neredzēsiet.
Koma inu munatichenjeza kuti, ‘Pokhapokha mutabwera naye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri, simudzandionanso.’
24 Un kad mēs nācām pie tava kalpa, sava tēva, un viņam sacījām sava kunga vārdus,
Ndiye pamene tinafika kwa kapolo wanu, abambo athu tinawawuza zonse zimene munanena.
25 Tad mūsu tēvs sacīja: noejat atkal, pērciet mums ēdama kādu mazumu.
“Abambo athu anatiwuza kuti, ‘Pitaninso mukagule kachakudya pangʼono.’
26 Tad sacījām: mēs nevaram noiet: ja mūsu jaunākais brālis mums ir līdz, tad mēs noiesim. Jo mēs nevaram tā vīra vaigu redzēt, ja šis mūsu jaunākais brālis nav mums līdz.
Koma tinati, ‘Sitingathe kupitanso. Sitingapite pokhapokha mngʼono wathuyu apite nafe chifukwa munthu uja anati sitingaonane naye ngati mngʼono wathuyu sakhala nafe.’
27 Tad tavs kalps, mans tēvs, mums sacīja: jūs zināt, ka mana sieva man divus dēlus dzemdējusi.
“Koma kapolo wanu, abambo athu anatiwuza kuti, ‘Inu mukudziwa kuti mkazi wanga anandiberekera ana aamuna awiri.
28 Un tas viens ir no manis aizgājis, un es sacīju, tiešām tas ir saplosīts, un es to vairs neesmu redzējis.
Mmodzi wa iwo anandisiya. Ine ndimati anadyedwa ndi chirombo popeza sindinamuonenso mpaka lero.
29 Ja tad jūs arī šo paņemsiet no manām acīm un tam kāda nelaime uzies, tad jūs manus sirmos matus ar sirdēstiem novedīsiet kapā. (Sheol h7585)
Tsopano mukanditengeranso uyu, nakaphedwa mu njira ndiye kuti mudzandikankhira ku manda ndi chisoni.’ (Sheol h7585)
30 Tad nu, kad es nākšu pie tava kalpa, sava tēva, un tas zēns mums nebūs līdz, jo tā tēva dvēsele viņa dvēselei sietin piesieta,
“Tsono ngati tizibwerera kwa mtumiki wanu, abambo athu popanda mnyamatayu, amene moyo wa abambo ake uli pa iyeyu,
31 Tad notiks, kad tas redzēs, ka tā zēna nav, tad tas mirs, un tavi kalpi novedīs tava kalpa, mana tēva, sirmos matus ar sirdēstiem kapā. (Sheol h7585)
ndipo akakaona kuti mnyamatayu palibe, basi akafa. Ife tidzakhala ngati takankhira abambo athu ku manda ndi chisoni. (Sheol h7585)
32 Jo tavs kalps ir galvojis par to zēnu pie sava tēva, un sacījis: ja es viņu tev atpakaļ neatvedīšu, tad visu savu mūžu es gribu būt noziedzīgs sava tēva priekšā.
Ndiponsotu ine ndinadzipereka kwa abambo anga kukhala chikole chotsimikiza kuti mnyamatayu ndidzamuteteza, ndipo ndinati, ‘Ngati sindibwerera naye mnyamatayu kwa inu, ndiye kuti ndidzakhala wochimwira inu abambo anga moyo wanga wonse.’
33 Un nu lai jel tavs kalps tā zēna vietā paliek par sava kunga vergu, un lai tas zēns aiziet ar saviem brāļiem.
“Tsono, chonde mulole kuti ine kapolo wanu nditsalire kuno kukhala kapolo wa mbuye wathu mʼmalo mwa mnyamatayu. Koma iye apite pamodzi ndi abale akewa.
34 Jo kā es varētu iet pie sava tēva, ja tas zēns man nebūtu līdz? - Man būtu jāredz tie sirdēsti, kas manam tēvam uzies.
Ndingabwerere bwanji kwa abambo anga ngati sindingapite ndi mnyamatayu? Ayi! Sindifuna kukaona tsoka limene lingakagwere abambo anga.”

< Pirmā Mozus 44 >