< 1 Abhakorintho 3 >

1 Nanye, bhamula bhasu na bhayala bhasu, nitalomele nemwe kuti lwa bhanu bhechinyamwoyo, nawe lwa bhanu bhechinyamubhili. Na lwa bhana bhalela mu Kristo.
Ndipo abale sindikanakuyankhulani ngati auzimu koma adziko lapansi, makanda chabe mwa Khristu.
2 Nabhanywesishe amata na jitali nyama, kulwokubha aliga mutemaliliye okulya jinyama. Na woli muchali kwimalilila.
Ndinakupatsani mkaka osati chakudya cholimba pakuti munali musanakonzeke kuchilandira. Zoonadi, simunakonzekebe.
3 Kulwokubha emwe muchali bhachinyamubhili. Kulwokubha lifubha no kwikuya okubhonekana agati yemwe. Angu, mutakwikala okulubhana no mubhili, na angu, mutakulibhata lwakutyo jibheile abhana bhanu?
Mukanali adziko lapansi. Pakuti pakati panu pali kaduka ndi kukangana, kodi si inu a dziko lapansi? Kodi simukuchita ngati anthu wamba?
4 Kulwokubha oumwi kaikati, “Enimulubha Paulo” Oundi kaikati “Enimulubha Apolo,” mutakwikala lwa bhana bhanu?
Pamene wina anena kuti, “Ine ndimatsatira Paulo,” ndipo wina akuti, “Ine ndimatsatira Apolo,” Kodi si inu akunja?
5 Apolo niga? na Paulo niga? Abhakosi bha unu mwikilisishe, bhuli unu Latabhugenyi ayanile okukola.
Ndiponso kodi Apolo ndi ndani? Nanga Paulo ndi ndani? Otumikira chabe, omwe kudzera mwa iwo inu munakhulupirira monga Ambuye anawagawira aliyense ntchito yake.
6 Anye nayambile, Apolo natako amanji, nawe Nyamuanga nakusha.
Ine ndinadzala mbewu, Apolo anayithirira, koma Mulungu ndiye anayikulitsa.
7 Kulwejo, atalyati unu ayambile nolo unu ateeko amanji atana chona chona. Nawe ni Nyamuanga unu kakusha.
Choncho kuphatikiza iye wodzala ndi iye wothirira, onse sali kanthu, koma Mulungu yekha amene amakulitsa zinthu.
8 Woli unu kayamba na unu katako amanji bhona ni sawa, na bhuli umwi kalamila omuyelo okulubhana ne milimu jae.
Munthu wodzala ndi munthu wothirira ali ndi cholinga chimodzi, ndipo aliyense adzapatsidwa mphotho molingana ndi ntchito yake.
9 Kulwokubha eswe chili bhakosi bha Nyamuanga, emwe ni migunda ja Nyamuanga, inyumba ya Nyamuanga.
Pakuti ife ndife antchito anzake a Mulungu; inu ndinu munda wa Mulungu, Nyumba ya Mulungu.
10 Okusokana ne chigongo cha Nyamuanga chinu nayanibhwe kuti mumbaki mukulu, nateewo omusingi, no oundi nombaka ingulu yagwo. Nawe omunu nabhwe mulengelesi kutyo kombakako ingulu yae.
Mwachisomo chimene Mulungu wandipatsa, ine ndinayika maziko monga mmisiri waluntha, ndipo ena akumangapo. Koma aliyense ayenera kuchenjera mmene akumangira.
11 Kulwokubha atalio undi unu katula okumbaka omusingi ogundi okukila gunu gumbakilwe, gunu guli Yesu Kristo.
Pakuti wina sangayikenso maziko ena oposera amene anakhazikitsidwa kale, amene ndi Yesu Khristu.
12 Woli, labha oumwi mwimwe kombaka ingulu yae kwa jijaabhu, Jiela, amabhui go bhugusi bhunene, amati, obhunyasi, nolo amabhabhi,
Ngati munthu aliyense amanga pa maziko awa pogwiritsa ntchito golide, siliva, miyala yamtengowapatali, milimo yamitengo, tsekera kapena udzu,
13 omulimu gwae gulisululwa, kwo bhwelu bhwa mumwisi bhuliisulula. Kulwokubha ilisululwa no mulilo. Omulilo gulilegeja obhwekisi bhwo mulimu gwa bhuli munu kutyo akolele.
ntchito yake idzaonekera pamene Tsiku la chiweruzo lidzazionetsa poyera. Tsikulo lidzafika ndi moto, ndipo motowo ndi umene udzayesa ntchito ya munthu aliyense.
14 Labha chona chona chinu omunu chinu ombakile chikasigala, omwene alibhona omuyelo.
Ngati zimene zamangidwazo sizidzagwa, adzalandira mphotho yake.
15 Nawe labha omulimu gwo munu gukalungula kwo mulilo, atalibhona muyelo. Nawe omwene alichungulwa, lwakutyo kasoka mumulilo.
Ndipo ngati zidzanyeke ndi moto, sadzalandira mphotho koma iye mwini adzapulumukabe, koma monga ngati munthu amene wapulumuka mʼmoto.
16 Mutakumenya ati emwe muli eyekalu lya Nyamuanga na ati Omwoyo gwa Nyamuanga gwikaye munda yemwe?
Kodi inu simukudziwa kuti ndinu Nyumba ya Mulungu ndipo kuti Mzimu wa Mulungu amakhala mwa inu?
17 Labha omunu akalinyamula liyekalu lya Nyamuanga, Nyamuanga kamunyamula omunu uliya. Kulwokubha liyekalu lya Nyamuanga ni lyelu, na kutyo nemwe.
Ngati wina aliyense awononga Nyumba ya Mulunguyo, Mulungu nayenso adzamuwononga ameneyo; popeza Nyumba ya Mulungu ndi yopatulika ndipo Nyumbayo ndi inu amene.
18 Omunu atajakwijiga omwene, labha wona wona mwimwe ketogelati ali no bhwengeso ku mwanya gunu, nabhe lwo “mumumu” niwo kabha mwengeso. (aiōn g165)
Choncho musadzinyenge. Ngati wina wa inu akuganiza kuti ndi wanzeru pa mulingo wa mʼbado uno, ayenera kukhala “wopusa” kuti athe kukhala wanzeru. (aiōn g165)
19 Kulwokubha obhwengeso bhwa kuchalo chinu ni bhumumu imbele ya Nyamuanga, Kulwokubha jandikilwe, “Kakoma abho bhwengeso kubhulige lige bhwebhwe”
Pakuti nzeru ya dziko lapansi ndi yopusa pamaso pa Mulungu. Monga kwalembedwera kuti, “Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,”
20 Na lindi “Latabhugenyi kamenya obhwiganilisha bhwa bhengeso ati ni bhutamu tamu.”
ndiponso, “Ambuye amadziwa kuti maganizo a wanzeru ndi opandapake.”
21 Kulwejo omunu ataja kwikuisha abhana bhanu! Kulwokubha ebhinu bhyona ni bhyemwe.
Choncho, wina asanyadire anthu chabe! Zonse ndi zanu,
22 Labha ni Paulo, nolo Apolo, nolo Kefa, nolo echalo, nolo obhulame, nolo lufu, nolo bhinu bhinu bhilio, nolo bhinu bhilibhao. Byona ni bhyemwe.
kaya Paulo kapena Apolo kapena Kefa kapena dziko lapansi, kapena moyo, kapena imfa, kapena tsopano, kapena mʼtsogolo, zonse ndi zanu,
23 nemwe muli bha Kristo na Kristo niwa Nyamuanga.
ndipo inu ndinu a Khristu, ndipo Khristu ndi wa Mulungu.

< 1 Abhakorintho 3 >