< 1 Corinto 3 >

1 Ken siak, kakabsat a lallaki ken babbai, ket saan a makasao kadakayo a kas naespirituan a tattao, ngem ketdi kas nainlasagan a tattao, a kas maladaga kenni Cristo.
Ndipo abale sindikanakuyankhulani ngati auzimu koma adziko lapansi, makanda chabe mwa Khristu.
2 Tinaraonankayo iti gatas ken saan a karne, ta saankayo pay a nakasagana idi para iti karne. Ken uray ita ket saankayo pay a nakasagana.
Ndinakupatsani mkaka osati chakudya cholimba pakuti munali musanakonzeke kuchilandira. Zoonadi, simunakonzekebe.
3 Ta nainlasagankayo pay laeng. Ta adda kadakayo iti panagimon ken panagririri, saankayo kadi nga agbibiag segun iti lasag, ken saankayo kadi a magmagna babaen kadagiti pagannurotan ti tao?
Mukanali adziko lapansi. Pakuti pakati panu pali kaduka ndi kukangana, kodi si inu a dziko lapansi? Kodi simukuchita ngati anthu wamba?
4 Ta no kuna ti maysa, “Surotek ni Pablo,” ken ibagbaga iti sabali, “Surotek ni Apollos,” saankayo kadi nga agbibiag a kas tattao?
Pamene wina anena kuti, “Ine ndimatsatira Paulo,” ndipo wina akuti, “Ine ndimatsatira Apolo,” Kodi si inu akunja?
5 Siasino ngarud ni Apollos? Ken siasino ni Pablo? Dagiti adipen a babaen kadakuada ket namatikayo, a nangtedan ti Apo kadagiti trabaho.
Ndiponso kodi Apolo ndi ndani? Nanga Paulo ndi ndani? Otumikira chabe, omwe kudzera mwa iwo inu munakhulupirira monga Ambuye anawagawira aliyense ntchito yake.
6 Nagmulaak, sinibugan ni Apollos, ngem inted ti Dios iti panagdakkel.
Ine ndinadzala mbewu, Apolo anayithirira, koma Mulungu ndiye anayikulitsa.
7 Isu ngarud, awan aniaman no siasino ti agmula wenno ti mangsibug. Ngem ti Dios ti mangpadpadakkel.
Choncho kuphatikiza iye wodzala ndi iye wothirira, onse sali kanthu, koma Mulungu yekha amene amakulitsa zinthu.
8 Ita, ti agmula ken ti mangsibug ket maymaysa, ken awatento ti tunggal maysa ti bukodna a tangdan segun iti bukodna nga aramid.
Munthu wodzala ndi munthu wothirira ali ndi cholinga chimodzi, ndipo aliyense adzapatsidwa mphotho molingana ndi ntchito yake.
9 Ta kapadanakami a trabahador ti Dios. Dakayo ti minuyongan ti Dios, ti pasdek ti Dios.
Pakuti ife ndife antchito anzake a Mulungu; inu ndinu munda wa Mulungu, Nyumba ya Mulungu.
10 Segun iti parabur ti Dios a naited kaniak a kas nalaing nga agipatpatakder, nangilatagak/nangiplastarak iti pundasyon ken adda sabali a nagpatakder iti rabawna daytoy. Ngem agannad koma ti tunggal maysa no kasano nga agipatakder isuna iti daytoy.
Mwachisomo chimene Mulungu wandipatsa, ine ndinayika maziko monga mmisiri waluntha, ndipo ena akumangapo. Koma aliyense ayenera kuchenjera mmene akumangira.
11 Ta awanen ti makaipatakder/makaiplastar iti sabali a pundasion ngem ti maysa a naipatakderen, dayta ket ni Jesu-Cristo.
Pakuti wina sangayikenso maziko ena oposera amene anakhazikitsidwa kale, amene ndi Yesu Khristu.
12 Ita, no mangipatakder ti siasinoman iti rabaw ti pundasyon nga addaan iti balitok, pirak, napateg a batbato, kayo, garami, wenno nagirikan,
Ngati munthu aliyense amanga pa maziko awa pogwiritsa ntchito golide, siliva, miyala yamtengowapatali, milimo yamitengo, tsekera kapena udzu,
13 maipakaammonto ti trabahona, ta ipakaammonto daytoy ti lawag ti aldaw. Ta maipakaammonto daytoy babaen iti apuy. Subokento ti apuy ti kita dagiti naaramidan ti tunggal maysa.
ntchito yake idzaonekera pamene Tsiku la chiweruzo lidzazionetsa poyera. Tsikulo lidzafika ndi moto, ndipo motowo ndi umene udzayesa ntchito ya munthu aliyense.
14 No agtalinaed ti aniaman nga ipatakder ti tao, magungunaanto isuna.
Ngati zimene zamangidwazo sizidzagwa, adzalandira mphotho yake.
15 Ngem no napuuran ti trabaho ti siasinoman, agsagabanto isuna iti pannakapukaw. Ngem maisalakanto isuna, a kasla agliblibas iti apuy.
Ndipo ngati zidzanyeke ndi moto, sadzalandira mphotho koma iye mwini adzapulumukabe, koma monga ngati munthu amene wapulumuka mʼmoto.
16 Saanyo kadi nga ammo a templonakayo ti Dios ken agnanaed ti Espiritu iti Dios kadakayo?
Kodi inu simukudziwa kuti ndinu Nyumba ya Mulungu ndipo kuti Mzimu wa Mulungu amakhala mwa inu?
17 No dadaelen ti siasinoman ti templo iti Dios, dadaelento ti Dios dayta a tao. Ta nasantoan ti templo iti Dios, ken kasta kayo met.
Ngati wina aliyense awononga Nyumba ya Mulunguyo, Mulungu nayenso adzamuwononga ameneyo; popeza Nyumba ya Mulungu ndi yopatulika ndipo Nyumbayo ndi inu amene.
18 Awan koma ti mangallilaw iti bagina. No adda ti siasinoman kadakayo iti agpanunot a masirib isuna iti daytoy a panawen, bay-am isuna nga agbalin a “maag” tapno agbalin isuna a masirib. (aiōn g165)
Choncho musadzinyenge. Ngati wina wa inu akuganiza kuti ndi wanzeru pa mulingo wa mʼbado uno, ayenera kukhala “wopusa” kuti athe kukhala wanzeru. (aiōn g165)
19 Ta ti kinasirib iti daytoy a lubong ket kinamaag iti Dios. Ta naisurat, “Tiltiliwenna ti masirib kadagiti kinasikapda.”
Pakuti nzeru ya dziko lapansi ndi yopusa pamaso pa Mulungu. Monga kwalembedwera kuti, “Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,”
20 Ket manen, “Ammo ti Apo nga awan mamaayna ti panagrasrason iti masirib.”
ndiponso, “Ambuye amadziwa kuti maganizo a wanzeru ndi opandapake.”
21 Isu nga awanen ti panagpaspasindayag maipanggep kadagiti tattao! Ta kukuayo dagiti amin a banbanag,
Choncho, wina asanyadire anthu chabe! Zonse ndi zanu,
22 ni Pablo man, wenno ni Apollos, wenno ni Cephas, wenno ti lubong, wenno biag, wenno patay, wenno dagiti banbanag iti agdama, wenno dagiti banbanag a dumtengto. Kukuayo dagiti amin a banbanag,
kaya Paulo kapena Apolo kapena Kefa kapena dziko lapansi, kapena moyo, kapena imfa, kapena tsopano, kapena mʼtsogolo, zonse ndi zanu,
23 ken kukuanakayo ni Cristo, ken kukua ti Dios ni Cristo.
ndipo inu ndinu a Khristu, ndipo Khristu ndi wa Mulungu.

< 1 Corinto 3 >