< Psalm 99 >

1 Der Herr ist König. Beben mögen da die Völker! Der Erdball zittere, wenn er sich auf die Cherubine niederläßt.
Yehova akulamulira, mitundu ya anthu injenjemere; Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi, dziko lapansi ligwedezeke.
2 Groß ist der Herr in Sion, erhaben über alle Völker!
Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova; Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
3 Sie sollen Deinen Namen preisen, ihn, den großen, schrecklichen! - Er ist so heilig.
Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri, Iye ndi woyera.
4 Und ist so mächtig. - Der Du das Recht liebst, König, stell die rechte Ordnung her und schaffe Billigkeit und Recht in Jakob!
Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera; mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
5 Den Herrn verherrlicht, unsern Gott! Vor seiner Füße Schemel betet an! Er ist so heilig.
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mulambireni pa mapazi ake; Iye ndi woyera.
6 Ein Moses und ein Aaron unter seinen Priestern; ein Samuel ruft seinen Namen an. Sie riefen zu dem Herrn, und er erhörte sie.
Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake, Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake; iwo anayitana Yehova ndipo Iyeyo anawayankha.
7 Er spricht zu ihnen wieder in der Wolkensäule, wenn sie befolgen seine Mahnungen und das von ihm gegebene Gesetz.
Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo; iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
8 Herr, unser Gott! Erhöre sie! Sei Du für sie ein Gott, fürsorgend, rächend ihre Unbilden!
Inu Yehova Mulungu wathu, munawayankha iwo; Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka, ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
9 Den Herrn verherrlicht, unsere Gott! Werft euch vor seinem heiligen Berge nieder! Denn unser Gott, der Herr, ist heilig.
Kwezani Yehova Mulungu wathu ndipo mumulambire pa phiri lake loyera, pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.

< Psalm 99 >