< Psalm 57 >

1 Auf den Siegesspender, ein Kunstgesang, von David, ein Weihegesang, als er vor Saul in die Höhle floh. Gott! Sei mir gnädig! Sei mir gnädig! Denn meine Seele flieht zu Dir. Ich fliehe in den Schatten Deiner Flügel, bis die Gefahr vorübergeht.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo, pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo. Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu mpaka chiwonongeko chitapita.
2 Zu Gott, dem Höchsten, rufe ich, zu Gott, der mir nur Gutes tut.
Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba, kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.
3 Er sendet Hilfe mir vom Himmel, verhöhnt mich auch mein Gegner, (Sela) Gott sendet dennoch seine Huld und Treue. -
Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa, kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri. Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.
4 Ich weile unter Löwen, bei Menschenfressern, bei Leuten, deren Zähne Spieß und Pfeile und deren Zungen scharfe Dolche.
Ine ndili pakati pa mikango, ndagona pakati pa zirombo zolusa; anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi, malilime awo ndi malupanga akuthwa.
5 Erhebe Dich, o Gott, soweit der Himmel, und Deinen Ruhm, soweit die Erde reicht!
Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba; mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.
6 Sie stellen meinem Schritt ein Netz; doch ich umgehe es. Sie graben eine Grube mir und fallen selbst hinein. (Sela)
Iwo anatchera mapazi anga ukonde ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa. Anakumba dzenje mʼnjira yanga koma agweramo okha mʼmenemo.
7 Aus Herzensgrunde, Gott, aus Herzensgrunde sing ich und juble:
Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu mtima wanga ndi wokhazikika. Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.
8 "Erwache, du mein Stolz! Wach, Harfe, auf und Zither! Ich singe wach das Morgenrot."
Dzuka moyo wanga! Dzukani zeze ndi pangwe! Ndidzadzuka mʼbandakucha.
9 Ich preise, Herr, Dich bei den Völkern, und ich besinge Dich bei den Nationen,
Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu, ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.
10 daß Deine Huld bis an den Himmel reicht, bis zu den Wolken Deine Treue.
Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba; kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.
11 Erhebe Dich, o Gott, soweit der Himmel, und Deinen Ruhm, soweit die Erde reicht!
Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba, mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.

< Psalm 57 >