< Psalm 33 >

1 Ihr Frommen, jauchzt dem Herrn! Den Redlichen ziemt Lobgesang.
Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
2 Mit Zitherklängen dankt dem Herrn! Ihm spielt auf Harfen mit zehn Saiten!
Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
3 Ihm singt ein nie gehörtes Lied! Und schlaget kräftig in die Saiten, daß es schallt!
Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
4 Wahrhaftig ist das Wort des Herrn, und Treue ist sein ganzes Tun.
Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
5 Er liebt Gerechtigkeit und Recht; des Herrn Güte ist die Erde voll.
Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
6 Die Himmel sind geworden durch das Wort des Herrn, durch seines Mundes Hauch ihr ganzes Heer.
Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
7 Er sammelt wie in einen Schlauch ein Meer von Wasser und legt in Speicher Ozeane.
Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
8 So fürchte alle Welt sich vor dem Herrn! Vor ihm erschauere jeder Erdbewohner!
Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
9 Denn so er spricht, geschieht's, gebietet er's, so bleibt es aus.
Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
10 Zunichte macht der Herr der Heiden Plan; der Völker Absichten vereitelt er.
Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
11 Der Plan des Herrn ist unveränderlich, und seines Herzens Pläne gelten für und für.
Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
12 Heil sei dem Heidenvolke, dessen Gott der Herr, der Nation, die er zur ewig Seinen sich erkoren!
Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
13 Vom Himmel schaut der Herr herab und blickt auf alle Menschenkinder!
Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
14 Von seiner Wohnstatt schaut er nieder auf alle Erdbewohner.
kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
15 Ihm, der geschaffen ihre Herzen allzumal, dem ist bekannt ihr ganzes Tun.
Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
16 Kein König siegt durch Heeresmacht; den Riesen rettet nicht die Fülle seiner Kraft.
Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
17 Betrogen, wer vom Roß den Sieg erwartet; nicht Rettung bringt es ihm trotz großer Stärke.
Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
18 Auf denen, so ihn fürchten, ruht des Herrn Auge, auf denen, die von seiner Güte hoffen,
Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
19 daß er vor Pest ihr Leben rette und sie in Hungersnot erhalte.
kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
20 Dem Herrn gilt unserer Seele Harren; uns ist er Schutz und Schild.
Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
21 So froh wird unser Herz durch ihn; denn wir vertrauen seinem heiligen Namen.
Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
22 Herr! Deine Gnade walte über uns, so wie wir sie von Dir erhoffen!
Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.

< Psalm 33 >