< Psalm 118 >

1 Dem Herrn sagt Dank! Denn er ist gut. In Ewigkeit währt sein Erbarmen.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
2 So spreche Israel: "In Ewigkeit währt seine Huld!"
Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
3 So spreche Aarons Haus: "In Ewigkeit währt seine Huld!"
Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
4 So mögen, die den Herren fürchten, sprechen: "In Ewigkeit währt seine Huld!" -
Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
5 Aus tiefer Not ruf ich zum Herrn, und mich erhört der Herr aus weiter Ferne.
Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
6 Ist schon der Herr für mich, dann fürcht ich nichts. Was könnten mir die Menschen tun?
Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
7 Und ist der Herr mein Beistand, dann schau ich meine Lust an meinen Hassern.
Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
8 Viel besser ist es, auf den Herrn zu bauen, als Menschen zu vertrauen.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
9 Viel besser ist es, auf den Herrn zu bauen, als Fürsten zu vertrauen. -
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
10 Umringen mich die Heiden all, ich wehre sie doch in des Herren Namen ab.
Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
11 Umringen sie mich auch, wie sie nur können, ich wehre sie doch in des Herren Namen ab.
Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
12 Umschwärmen sie mich auch wie ausgestoßene Bienen und wie das Feuer Dorngestrüpp einhüllt, ich wehre sie doch in des Herren Namen ab.
Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
13 Und stößt man mich zum Sturz, dann steht der Herr mir bei.
Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
14 Mein Siegen ist des Herren Lob, verhilft er mir zur Rettung. -
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
15 Dann tönen Jubellaut und Siegesruf bei den Gezelten der Gerechten: Gar Großes tut des Herren Rechte.
Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
16 Ganz überlegen ist des Herren Rechte; gar Großes tut des Herren Rechte."
Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
17 Ich sterbe nicht; ich bleibe noch am Leben, verkündige des Herren Taten.
Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
18 Und züchtigt mich der Herr auch hart, er gibt mich nicht dem Tode preis.
Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
19 So öffnet mir die Siegespforten! Ich ziehe ein, dem Herrn zu danken.
Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
20 Dies ist des Herren Pforte; die Frommen ziehen durch sie ein. -
Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
21 "Ich danke Dir, daß Du mich hast erhört und mir zur Rettung bist geworden." -
Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
22 Der Stein, verworfen von den Bauleuten, ist jetzt der Eckstein.
Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
23 Dies ist vom Herrn geschehn, ganz wunderbar in unsern Augen.
Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
24 Dies ist der Tag, vom Herrn gewährt. Geweiht sei er dem Jubel und der Freude! -
Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
25 "Wohlan, Herr, spende Heil! Wohlan, Herr, spende Glück!"
Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
26 Gesegnet in des Herren Namen sei, wer eintritt! Wir segnen euch vom Haus des Herrn:
Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
27 "Der Herr ist Gott; er leuchte uns!" Beginnt den Reigen mit den Zweigen bis zu den Hörnern des Altars! -
Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
28 "Du bist mein Gott; ich danke Dir. Mein Gott, ich preise Dich." In Ewigkeit währt seine Huld.
Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
29 Dem Herrn sagt Dank! Denn er ist gut.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.

< Psalm 118 >