< Job 38 >

1 Darauf antwortete der Herr dem Job nach dem Gewitter also:
Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
2 "Wer ist denn dieser, der mit einsichtslosen Worten so dunkel findet meine Pläne?
“Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
3 Auf, gürte deine Lenden wie ein Mann! Ich will dich fragen; du belehre mich!
Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
4 Wo warst du denn, als ich die Erde gründete? Vermelde es, wenn Einsicht dir bekannt.
“Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
5 Wer nur bestimmte ihre Maße? Du weißt es ja. Wer hat die Meßschnur über sie gespannt?
Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
6 Worauf sind ihre Pfeiler eingesenkt? Wer hat für sie den Schlußstein eingesetzt?
Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
7 Wo warst du, als die Morgensterne jubelten, als alle Gottessöhne jauchzten?
pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
8 Wer schloß das Meer mit Toren ein, als dies hervorbrach wie aus einem Mutterschoß,
“Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
9 als ich Gewölk zu seinem Kleide machte und dichte Finsternis zu seinen Windeln?
pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
10 Ich gab ihm mein Gesetz, versah mit Riegeln seine Tore
pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
11 und sprach: 'Bis hierher und nicht weiter! Hier soll sich brechen deiner Wogen Überschwang!'
Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
12 Hast du in deinem Leben je dem Morgenrot geboten, dem Frührot seine Stätte angewiesen,
“Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
13 der Erde Säume zu umfassen, damit die Frevler von ihr schwänden?
kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
14 Sie wandelt sich gleich Siegelton; sie färbt sich gleichwie ein Gewand.
Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
15 Den Frevlern wird ihr Licht entzogen; zerschmettert wird der schon erhobene Arm.
Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
16 Gelangtest du bis zu des Meeres Strudeln? Bist du gewandelt auf der Tiefe Grund?
“Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
17 Und öffneten sich dir des Todes Tore, und schautest du des tiefen Dunkels Hüter?
Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
18 Hast du der Erde Breiten überschaut? Vermelde, wenn du dies alles weißt:
Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
19 Wo ist der Weg zur Wohnstätte des Lichtes,
“Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
20 wo ist der Ort der Finsternis, auf daß du jenes zum Gebiete dieser führen und ihrer Wohnung Wege zeigen kannst?
Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
21 Du weißt es ja; denn damals wurdest du geboren, und deiner Tage Zahl ist groß.
Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
22 Bist du gekommen zu des Schnees Kammern? Hast du erblickt des Hagels Speicher,
“Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
23 den für die Drangsalzeit ich aufgespart, für Kampf- und Fehdetage?
zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
24 Wo ist der Weg dahin, wo sich der Sturm zerteilt, von wo der Ostwind auf die Erde sich verbreitet?
Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
25 Wer hat Kanäle für den Regen hergestellt und einen Weg dem Wetterstrahl,
Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
26 um Regen menschenleerem Land zu geben, der Wüste, in der keine Leute wohnen,
kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
27 um öde Wildnis zu ersättigen, damit sie Pflanzen sprossen lasse?
kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
28 Hat denn der Regen einen Vater? Wer hat die Tautropfen erzeugt?
Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
29 Aus wessen Schoße kommt das Eis? Wer hat des Himmels Reif geboren?
Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
30 Gleich dem Kristall verdichtet sich das Wasser; der Wasserfluten Fläche hält dann fest zusammen.
pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
31 Verknüpfest du die Bande der Plejaden, oder lösest du die Fesseln des Orion?
“Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
32 Führst du den Tierkreis aus zu seiner Zeit, und leitest den Bären du samt seinen Jungen?
Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
33 Erkennst du die Gesetze der Himmelshöhn? Bestimmst du ihre Herrschaft für die Erde?
Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
34 Erhebst du zu der Wolke deine Stimme? Bedeckt dich dann ein Wasserschwall?
“Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
35 Entsendest du die Blitze, daß sie gehen und zu dir sagen: 'Hier sind wir'?
Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
36 Wer legte in die Wolken Weisheit? Oder wer verlieh der Wolkenmasse Klugheit?
Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
37 Wer treibt die Wolken weise fort? Wer legt des Himmels Krüge um,
Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
38 auf daß zu Gußwerk fließt der Staub zusammen und fest die Schollen aneinanderkleben?
pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
39 Erjagst du für die Löwin Beute? Und stillest du die Gier der jungen Leuen,
“Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
40 wenn in den Lagerstätten sie sich ducken, im Dickicht auf der Lauer liegen?
pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
41 Wer gibt dem Raben seine Atzung, wenn seine Jungen schrein zu Gott und ohne Nahrung flattern?"
Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?

< Job 38 >