< 1 Chronik 2 >

1 Dies sind Israels Söhne: Ruben, Simeon, Levi und Juda, Issakar und Zabulon,
Ana a Israeli anali awa: Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Zebuloni,
2 Dan, Joseph und Benjamin, Naphtali, Gad und Asser.
Dani, Yosefe, Benjamini, Nafutali, Gadi ndi Aseri.
3 Judas Söhne sind: Er, Onan und Sela, drei, die ihm von Suas Tochter, der Kanaaniterin, geboren sind. Judas Erstgeborener machte sich dem Herrn mißfällig, und dieser ließ ihn sterben.
Ana a Yuda anali awa: Eri, Onani ndi Sela. Ana atatu awa anabereka ndi mkazi wa Chikanaani, Batisuwa. Eri, mwana woyamba wa Yuda anali woyipa kwambiri pamaso pa Yehova, kotero Yehova anamupha.
4 Seine Schwiegertochter Tamar aber gebar ihm Peres und Zerach. Aller Söhne Judas sind es fünf.
Mpongozi wake Tamara anamuberekera Perezi ndi Zera. Ana onse a Yuda analipo asanu.
5 Des Peres Söhne sind Chesron und Chamul.
Ana a Perezi anali awa: Hezironi ndi Hamuli.
6 Des Zerach Söhne sind Zimri, Etan, Heman, Kalkol und Dara, zusammen fünf.
Ana a Zera anali awa: Zimuri, Etani, Hemani, Kalikoli ndi Dara. Onse analipo asanu.
7 Des Karmi Söhne sind: Akar, der Israel ins Unglück stürzte, da er sich am Geweihten pflichtvergessen vergriff.
Mwana wa Karimi anali Akani, amene anabweretsa mavuto pakati pa Israeli pamene anatenga zinthu zoyenera kuwonongedwa.
8 Etans Söhne sind: Azarja.
Mwana wa Etani anali Azariya.
9 Chesrons Söhne, die ihm geboren worden, sind Jerachmeel, Ram und Kelubai.
Ana amene anabadwa kwa Hezironi anali: Yerahimeeli, Ramu ndi Kelubai.
10 Ram zeugte Aminadab und Aminadab den Nachson, den Judäerfürsten.
Ramu anabereka Aminadabu ndipo Aminadabu anali abambo ake a Naasoni, mtsogoleri wa fuko la Yuda.
11 Nachson zeugte Salma und Salma den Boaz.
Naasoni anabereka Salima, Salima anabereka Bowazi,
12 Boaz zeugte Obed und Obed den Isai.
Bowazi anabereka Obedi ndipo Obedi anabereka Yese.
13 Und Isai zeugte als seinen Erstgeborenen Eliab, als zweiten Abinadab, als dritten Sima,
Yese anabereka Eliabu mwana wake woyamba, wachiwiri Abinadabu, wachitatu Simea,
14 als vierten Natanael, als fünften Raddai,
wachinayi Netaneli, wachisanu Radai,
15 als sechsten Osem und als siebten David.
wachisanu ndi chimodzi Ozemu ndi wachisanu ndi chiwiri Davide.
16 Ihre Schwestern sind Seruja und Abigail. Der Seruja Söhne sind Absai, Joab und Asael, drei.
Alongo awo anali Zeruya ndi Abigayeli. Ana atatu a Zeruya anali Abisai Yowabu ndi Asaheli.
17 Abigail gebar Amasa. Des Amasa Vater ist der Ismaeliter Jeter.
Abigayeli anali amayi ake a Amasa amene abambo ake anali Yeteri wa fuko la Ismaeli.
18 Chesrons Sohn Kaleb hat Azuba geheiratet. Dies sind ihre Söhne: Jeser, Sobab und Ardon.
Kalebe mwana wa Hezironi anabereka ana mwa Azuba mkazi wake (ndi mwa Yerioti). Ana a mkaziyo anali awa: Yeseri, Sobabu ndi Aridoni.
19 Als Azuba starb, nahm sich Kaleb die Ephrat. Sie gebar ihm den Chur.
Azuba atamwalira, Kalebe anakwatira Efurata, amene anamuberekera Huri.
20 Chur aber zeugte Uri und Uri den Besalel.
Huri anabereka Uri ndipo Uri anabereka Bezaleli.
21 Hernach ist Chesron zur Tochter Makirs, des Vaters von Gilead, gegangen und hat sie geheiratet, als er sechzig Jahre alt war, und sie gebar ihm den Segub.
Patapita nthawi, Hezironi anagona ndi mwana wamkazi wa Makiri abambo ake a Giliyadi (iye anamukwatira ali ndi zaka 60) ndipo anamuberekera Segubu.
22 Segub aber zeugte Jair. Dieser besaß dreiundzwanzig Städte im Lande Gilead.
Segubu anabereka Yairi, amene anali ndi mizinda 23 ku Giliyadi.
23 Aber die Gesuriter und die Aramäer nahmen ihnen Jairs Zeltdörfer weg, Kenat mit seinen Tochterstädten, sechzig Städte. Alle diese waren die Söhne des Gileadvaters Makir.
(Koma Gesuri ndi Aramu analanda Havoti Yairi komanso Kenati ndi madera ake onse ozungulira, mizinda makumi asanu ndi umodzi). Onsewa anali adzukulu, a Makiri abambo ake a Giliyadi.
24 Nach Chesrons Tod ging Kaleb nach Ephrat. Chesrons Weib aber war Abia, und sie gebar ihm Aschur, Tekoas Vater.
Atamwalira Hezironi ku Kalebe Efurata, Abiya mkazi wa Hezironi anamuberekera Asihuri abambo a Tekowa.
25 Jerachmeels, des Erstgeborenen des Chesron, Söhne waren der Erstgeborene Ram, dann Buna, Oren, Osem und Achia.
Ana a Yerahimeeli, mwana woyamba wa Hezironi anali: Ramu, mwana wake woyamba, Buna, Oreni, Ozemu ndi Ahiya.
26 Jerachmeel hatte noch ein anderes Weib mit Namen Atara. Sie war Onams Mutter.
Yerahimeeli anali ndi mkazi wina amene dzina lake linali Atara, amene anali amayi a Onamu.
27 Rams, des Erstgeborenen von Jerachmeel, Söhne sind Maan, Jamin und Eker.
Ana a Ramu, mwana woyamba wa Yerahimeeli, anali awa: Maazi, Yamini ndi Ekeri.
28 Onams Söhne sind Sammai und Jada. Sammais Söhne sind Nadab und Abisur.
Ana a Onamu anali awa: Shamai ndi Yada. Ana a Shamai anali awa: Nadabu ndi Abisuri.
29 Abisurs Weib hieß Abichail. Sie gebar ihm Achban und Molid.
Mkazi wa Abisuri anali Abihaili, amene anamuberekera Ahibani ndi Molidi.
30 Nadabs Söhne sind Seled und Appaim. Seled starb kinderlos.
Ana a Nadabu anali awa: Seledi ndi Apaimu. Koma Seledi anamwalira wopanda ana.
31 Appaims Söhne sind Isi, Isis Söhne sind: Sesan, Sesans Söhne sind Achlai.
Ana a Apaimu anali awa: Isi, amene anabereka Sesani. Sesani anabereka Ahilai.
32 Jadas, Sammais Bruders, Söhne sind Jeter und Jonatan. Jeter aber starb kinderlos.
Ana a Yada, mʼbale wa Samai, anali awa: Yereri ndi Yonatani. Koma Yeteri anamwalira wopanda ana.
33 Jonatans Söhne sind Pelet und Zaza. Dies sind Jerachmeels Söhne.
Ana a Yonatani anali awa: Peleti ndi Zaza. Amenewa anali adzukulu a Yerahimeeli.
34 Sesan hatte keine Söhne gehabt, sondern nur Töchter. Dagegen besaß Sesan einen ägyptischen Sklaven namens Jarcha.
Sesani sanabereke ana aamuna koma aakazi okhaokha. Iye anali ndi wantchito wa ku Igupto, dzina lake Yariha.
35 Seinem Sklaven Jarcha aber gab Sesan seine Tochter zum Weibe, und sie gebar ihm den Attai.
Sesani anapereka mwana wake wamkazi kwa Yariha wantchito wake kuti amukwatire ndipo anamuberekera Atayi.
36 Attai zeugte Natan und Natan den Zabad.
Atayi anali abambo ake a Natani, Natani anali abambo ake a Zabadi,
37 Zabad zeugte Ephlal und Ephlal den Obed.
Zabadi anali abambo a Efilali, Efilali anali abambo a Obedi,
38 Obed zeugte Jehu und Jehu den Azarja.
Obedi anali abambo a Yehu, Yehu anali abambo a Azariya,
39 Azarja hat Cheles gezeugt und Cheles den Elasa.
Azariya anali abambo a Helezi, Helezi anali abambo a Eleasa,
40 Elasa zeugte Sismai und Sismai den Sallum.
Eleasa anali abambo ake a Sisimai, Sisimai anali abambo a Salumu,
41 Sallum zeugte Jekamja und Jekamja den Elisama.
Salumu anali abambo a Yekamiya, Yekamiya anali abambo a Elisama.
42 Kalebs, Jerachmeels Bruders, Söhne sind sein Erstgeborener Mesa, das ist Ziphs Vater, und die Söhne Maresas, des Vaters von Chebron.
Ana a Kalebe mʼbale wa Yerahimeeli anali awa: Mesa mwana wachisamba, anali abambo a Zifi, ndipo mwana wake Maresa anali abambo a Hebroni.
43 Chebrons Söhne sind Korach, Tappuach, Rekem und Sema.
Ana a Hebroni anali awa: Kora, Tapuwa, Rekemu ndi Sema.
44 Sema zeugte Jorkams Vater Racham, und Rekem zeugte Sammai.
Sema anali abambo ake Rahamu ndipo Rahamu anali abambo a Yorikeamu. Rekemu anali abambo a Samai.
45 Sammais Sohn ist Maon, und Maon ist der Vater von Bet Sur.
Mwana wa Samai anali Maoni, ndipo Maoni anali abambo a Beti Zuri.
46 Kalebs Nebenweib Epha gebar Charan, Mosa und Gazez. Charan zeugte Gazez.
Efai, mzikazi wa Kalebe, anali amayi a Harani, Moza ndi Gazezi. Harani anali abambo a Gazezi.
47 Jahdais Söhne sind Regem, Jotam, Gesan, Pelet, Epha und Saaph.
Ana a Yahidai anali awa: Regemu, Yotamu, Gesani, Peleti, Efai ndi Saafi.
48 Kalebs Nebenweib Maaka gebar Seber und Tirchana.
Maaka mzikazi wa Kalebe anali mayi Seberi ndi Tirihana.
49 Sie gebar auch Saaph, den Vater von Madmanna, Seva, den Vater von Makbenna, und den Vater von Giba. Kalebs Tochter war Aksa.
Iye anaberekanso Saafi abambo a Madimena ndi Seva abambo a Makibena ndi Gibeya. Mwana wamkazi wa Kalebe anali Akisa.
50 Dies sind Kalebs Söhne: Churs, des Erstgeborenen des Ephrat, Söhne sind Sobal, der Vater von Kirjat Jearim,
Izi zinali zidzukulu za Kalebe. Ana a Huri mwana wachisamba wa Efurata anali awa: Sobala abambo a Kiriati Yearimu,
51 Salma, der Vater von Bethlehem, und Chareph, der Vater von Bet Gader.
Salima abambo a Betelehemu ndi Harefu abambo ake a Beti-Gadera.
52 Sobal, Kirjat Jearims Vater, hatte zu Söhnen Haroeh, die Hälfte der Menuchot
Zidzukulu za Sobala abambo a Kiriati Yearimu zinali izi: Harowe, theka la banja la Manahati,
53 und die Sippen Kirjat Jearims, die Itriter, Putiter, Sumatiter und Misraiter. Von diesen stammen die Saratiter und die Estauliter.
ndipo mabanja a Kiriati-Yeyarimu anali awa: Aitiri, Aputi, Asumati ndi Amisirai. Azorati ndi Aesitaoli anachokera kwa amenewa.
54 Salmas Söhne sind Bethlehem und die Netophatiter, Aterot, Bet Joab und die Hälfte der Manachtiter und der Sariter
Zidzukulu za Salima zinali izi: Betelehemu, Anetofati, Atiroti-Beti-Yowabu, theka la banja la Manahati, Azori,
55 und die Sippen der Sopherim, die in Jabes wohnen, die Tiratiter, Simatiter und Sukatiter. Dies sind die Kiniter, die von Chamot, Bet Rekabs Vater, stammen.
ndiponso mabanja a alembi amene amakhala ku Yabesi: Atiroti, Asimeati ndiponso Asukati. Awa ndi Akeni amene anachokera kwa Hamati, kholo la Arekabu.

< 1 Chronik 2 >