< Proverbes 1 >

1 Proverbes de Salomon, fils de David, roi d’Israël:
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 Grâce à eux, on apprend à connaître la sagesse et la morale, à goûter le langage de la raison;
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 à accueillir les leçons du bon sens, la vertu, la justice et la droiture.
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 Ils donnent de la sagacité aux simples, au jeune homme de l’expérience et de la réflexion.
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 En les entendant, le sage enrichira son savoir, et l’homme avisé acquerra de l’habileté.
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6 On saisira mieux paraboles et sentences, les paroles des sages et leurs piquants aphorismes.
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 La crainte de l’Eternel est le principe de la connaissance; sagesse et morale excitent le dédain des sots.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 Ecoute, mon fils, les remontrances de ton père, ne délaisse pas les instructions de ta mère;
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 car elles forment un gracieux diadème pour ta tête et un collier pour ton cou.
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 Mon fils, si des criminels cherchent à t’entraîner, ne leur cède point;
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 s’ils disent: "Viens donc avec nous, nous allons combiner des meurtres, attenter sans motif à la vie de l’innocent;
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 comme le Cheol nous les engloutirons vivants, tout entiers comme ceux qui descendent dans la tombe. (Sheol h7585)
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
13 Nous ferons main basse sur tout objet de prix; nous remplirons nos maisons de butin.
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 Tu associeras ton sort au nôtre: nous ferons tous bourse commune,"
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 mon fils, ne fraye pas avec eux, écarte tes pas de leur sentier;
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 car leurs pieds se précipitent vers le mal, ils ont hâte de répandre le sang.
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 Certes les filets paraissent dressés sans aucun but aux yeux de la gent ailée:
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 eux aussi en veulent à leur propre sang, et c’est à eux-mêmes qu’ils dressent un piège.
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 Tel est le sort auquel court quiconque poursuit le lucre: il coûte la vie à ceux qui l’ambitionnent.
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 La sagesse prêche dans la rue; sur les voies publiques elle élève la voix.
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 Elle appelle à elle au milieu des bruyants carrefours, à l’entrée des portes. En pleine ville, elle fait entendre ses discours:
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 "Jusqu’à quand, niais, aimerez-vous la sottise, et vous, persifleurs, aurez-vous du goût pour la moquerie? Jusqu’à quand, insensés, haïrez-vous le savoir?
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Cédez à mes remontrances; voici, je veux vous ouvrir les sources de mon esprit, vous enseigner mes paroles.
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 Puisque j’ai appelé et que vous avez refusé de m’entendre; puisque j’ai tendu la main et que personne n’y a fait attention;
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 puisque vous avez repoussé tous mes conseils et que vous n’avez pas voulu de mes remontrances,
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 en retour je rirai, moi, de votre malheur, je vous raillerai quand éclatera votre épouvante;
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27 oui, quand éclatera votre épouvante, pareille à une tempête, et votre malheur, tel qu’un ouragan, quand fondront sur vous détresse et angoisse.
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 Alors on m’appellera et je ne répondrai point, on me cherchera, mais on ne me trouvera pas.
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 Aussi bien, ils ont détesté le savoir, ils n’ont eu aucun goût pour fa crainte de l’Eternel.
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 Ils n’ont pas voulu de mes conseils, n’ont eu que du dédain pour toutes mes réprimandes.
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 Qu’ils se nourrissent donc du fruit de leur conduite, qu’ils se rassasient de leurs résolutions!
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 Assurément, la rébellion des niais les perdra, et la fausse quiétude des sots causera leur ruine.
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 Mais quiconque m’écoute demeurera en sécurité, exempt de la crainte du malheur."
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”

< Proverbes 1 >