< Job 16 >

1 Job reprit la parole et dit:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 De tels discours, j’en ai entendu beaucoup: vous êtes tous de pauvres consolateurs.
“Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
3 Y aura-t-il une fin à ces paroles qui sonnent creux? Qu’est-ce donc qui te contraint de répliquer?
Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
4 Moi aussi, je pourrais parler comme vous, si seulement vous étiez à ma place; je pourrais aligner des paroles contre vous et hocher la tête à votre sujet.
Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
5 Je vous donnerais du réconfort avec ma bouche, et le mouvement de mes lèvres serait votre soulagement.
Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
6 Maintenant; si je parle, ma douleur n’en sera pas adoucie; si je m’abstiens, me lâchera-t-elle pour cela?
“Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
7 Oui, à l’heure présente Dieu m’a exténué; tu as jeté le trouble dans tout mon entourage.
Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
8 Tu m’as couvert de rides qui sont autant de témoins à charge; ma maigreur elle-même me trahit et dépose contre moi.
Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
9 Sa fureur me déchire, me traite en ennemi; il grince des dents contre moi: mon adversaire darde sur moi ses regards.
Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
10 Ils ouvrent contre moi une bouche béante, ils me frappent ignominieusement sur les joues: en bande ils s’attroupent autour de moi.
Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
11 Le Tout-Puissant me livre à des écervelés; il me jette en proie aux mains des méchants.
Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
12 Je vivais paisible, et il m’a broyé; il m’a saisi par la nuque et mis en pièces; il m’a dressé comme une cible à ses coups.
Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
13 Ses archers me cernent de toutes parts; sans pitié il me perce les reins, répand à terre mon fiel.
anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
14 Il ouvre en moi brèche sur brèche, il court sur moi comme un guerrier puissant.
Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
15 J’Ai cousu un cilice sur ma peau desséchée et traîné mon front dans la poussière.
“Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
16 J’Ai le visage tout bouffi par les pleurs; une nuit noire s’étend sur mes paupières.
Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
17 Et aucune injustice ne souille mes mains! Et ma prière a toujours été pure!
komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
18 O terre, ne recouvre pas mon sang! Qu’aucun obstacle n’arrête mes cris!
“Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
19 Dès maintenant j’ai un témoin pour moi dans les cieux, un répondant dans les régions supérieures.
Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
20 Mes amis se raillent de moi: c’est vers Dieu que s’élèvent mes yeux baignés de larmes,
Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
21 pour qu’il soit lui-même arbitre entre l’homme et Dieu, entre le fils de l’homme et son semblable.
iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
22 Car ce peu d’années vont s’écouler, et je prendrai un chemin par où je ne repasserai point.
“Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”

< Job 16 >