< Nombres 31 >

1 Yahvé parla à Moïse, et dit:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 « Venge les enfants d'Israël sur les Madianites. Ensuite, vous serez rassemblés auprès de votre peuple. »
“Uwabwezere zoyipa Amidiyani chifukwa cha zimene anachitira Aisraeli. Ukatha kuchita zimenezi, iwe udzamwalira.”
3 Moïse parla au peuple, et dit: « Armez des hommes parmi vous pour la guerre, afin qu'ils aillent contre Madian, pour exécuter la vengeance de Yahvé sur Madian.
Ndipo Mose anati kwa Aisraeli, “Perekani zida kwa ena mwa anthu anu kuti akamenyane ndi Amidiyani ndi kuwabwezera choyipa mʼmalo mwa Yehova.
4 Vous enverrez mille hommes de chaque tribu, de toutes les tribus d'Israël, à la guerre. »
Mutumize ku nkhondoko amuna 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.”
5 On livra donc, parmi les milliers d'Israël, mille hommes de chaque tribu, soit douze mille hommes armés pour la guerre.
Choncho amuna okwana 12,000 anatenga zida kukonzekera nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.
6 Moïse les envoya, mille de chaque tribu, à la guerre, avec Phinées, fils du prêtre Éléazar, à la guerre, les ustensiles du sanctuaire et les trompettes d'alarme dans sa main.
Mose anawatumiza ku nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse pamodzi ndi Finehasi mwana wa Eliezara wansembe amene ananyamula zipangizo zochokera ku malo wopatulika ndi malipenga okaliza.
7 Ils combattirent contre Madian, comme Yahvé l'avait ordonné à Moïse. Ils tuèrent tous les mâles.
Iwo anamenyana ndi Amidiyani monga momwe Yehova analamulira Mose ndipo anapha mwamuna aliyense.
8 Ils tuèrent les rois de Madian avec le reste de leurs morts: Evi, Rékem, Tsur, Hur et Réba, les cinq rois de Madian. Ils tuèrent aussi par l'épée Balaam, fils de Beor.
Mwa anthu ophedwawo munali Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu asanu a Amidiyani. Ndipo anaphanso ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori.
9 Les enfants d'Israël emmenèrent captives les femmes de Madian et leurs petits enfants, et ils pillèrent tout leur bétail, tous leurs troupeaux et tous leurs biens.
Aisraeli anagwira ukapolo amayi a Chimidiyani ndi ana awo ndipo analandanso ngʼombe, ziweto zawo zina zonse ndi katundu wawo yense.
10 Ils brûlèrent au feu toutes leurs villes, dans les lieux qu'ils habitaient, et tous leurs campements.
Anawotcha mizinda yonse imene Amidiyani ankakhalamo pamodzi ndi misasa yawo yonse.
11 Ils prirent tous les captifs et tout le butin, tant des hommes que des animaux.
Anatenga zonse zimene analanda ku nkhondoko, anthu ndi zoweta zomwe.
12 Ils amenèrent les captifs, avec le butin et le pillage, à Moïse, au sacrificateur Éléazar et à l'assemblée des enfants d'Israël, au camp des plaines de Moab, qui sont près du Jourdain, à Jéricho.
Ndipo anabwera nawo akapolowo ndi zolanda ku nkhondozo kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa gulu lonse la Aisraeli ku misasa yawo ku chigwa cha Mowabu, mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko.
13 Moïse et le sacrificateur Éléazar, avec tous les chefs de l'assemblée, sortirent à leur rencontre hors du camp.
Mose, wansembe Eliezara ndi atsogoleri onse a gululo anapita kukakumana nawo kunja kwa misasa.
14 Moïse se mit en colère contre les officiers de l'armée, les chefs de milliers et les chefs de centaines, qui venaient du service de la guerre.
Mose anakwiya nawo akuluakulu a magulu a ankhondowo: olamulira 1,000 ndi olamulira 100, amene ankachokera ku nkhondo.
15 Moïse leur dit: « Avez-vous sauvé toutes les femmes en vie?
Iye anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mwawaleka amoyo amayi onsewa?”
16 Voici qu'elles ont poussé les enfants d'Israël, par le conseil de Balaam, à commettre une infidélité à l'égard de l'Éternel dans l'affaire de Péor, et c'est ainsi que la plaie a frappé la congrégation de l'Éternel.
Paja iwo ndi amene ankatsatira uphungu wa Balaamu ndiponso ndi amene anachititsa Aisraeli kuti asiye Yehova pa zimene zinachitika ku Peori, kotero mliri unagwera anthu a Yehova.
17 Maintenant, tuez tout mâle parmi les petits enfants, et tuez toute femme qui a connu un homme en couchant avec lui.
Tsopano iphani munthu wamwamuna aliyense. Ndiponso iphani mayi aliyense amene anagonapo ndi mwamuna,
18 Mais toutes les filles qui n'ont pas connu d'homme en couchant avec lui, gardez-les vivantes pour vous.
koma sungani mtsikana aliyense amene sanagonepo ndi mwamuna.
19 « Campez hors du camp pendant sept jours. Celui qui a tué quelqu'un et celui qui a touché un mort, purifiez-vous le troisième jour et le septième jour, vous et vos captifs.
“Inu nonse amene mwaphapo wina wake, kapena kukhudza aliyense amene anaphedwa mukhale kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachitatu mudziyeretse nokha pamodzi ndi akapolo anu.
20 Vous purifierez tout vêtement, tout ce qui est fait en peau, tout ce qui est fait en poil de chèvre et tout ce qui est fait en bois. »
Muyeretsenso zovala zanu ndi china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, ubweya wa mbuzi kapenanso ndi mtengo.”
21 Le sacrificateur Éléazar dit aux hommes de guerre qui allaient au combat: « Voici le règlement de la loi que l'Éternel a prescrite à Moïse.
Tsono wansembe Eliezara anati kwa asilikali amene anapita ku nkhondo aja, “Lamulo limene Yehova anapereka kwa Mose ndi ili:
22 Cependant, l'or, l'argent, l'airain, le fer, l'étain et le plomb,
Golide, siliva, mkuwa, chitsulo, chiwaya, mtovu
23 tout ce qui peut résister au feu, vous le ferez passer par le feu, et il sera pur; néanmoins, il sera purifié avec l'eau pour être impur. Tout ce qui ne résistera pas au feu, vous le ferez passer dans l'eau.
ndi china chilichonse chimene sichingapse ndi moto muchidutsitse pa moto, ndipo chidzayeretsedwa. Komanso chiyeretsedwe ndi madzi oyeretsa. Ndipo chilichonse chimene chingapse ndi moto muchidutsitse mʼmadzimo.
24 Tu laveras tes vêtements le septième jour, et tu seras pur. Ensuite, tu entreras dans le camp. »
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muchape zovala zanu ndipo mudzayera. Mukatero mutha kulowa mu msasa.”
25 L'Éternel parla à Moïse, et dit:
Yehova anawuza Mose kuti,
26 Comptez le butin qui a été fait, tant pour les hommes que pour les animaux, vous, le prêtre Éléazar et les chefs de famille de l'assemblée,
“Iwe ndi wansembe Eliezara ndiponso akuluakulu a mabanja a anthuwa, muwerenge anthu onse ndi ziweto zomwe zinagwidwa ku nkhondo.
27 et partagez le butin en deux parties: entre les hommes de guerre qui sont allés au combat et toute l'assemblée.
Mugawe zolanda ku nkhondozo magawo awiri, lina la ankhondo amene anapita ku nkhondo, lina la anthu onse.
28 Prélève un tribut à l'Éternel sur les hommes de guerre qui sont allés au combat: une âme sur cinq cents, sur les personnes, sur le bétail, sur les ânes et sur les troupeaux.
Pa gawo la ankhondowo, mutengeko gawo la Yehova, pa zofunkha 500 zilizonse mutengeko chimodzi, pa akapolo, ngʼombe, bulu ndi nkhosa.
29 Prenez-en la moitié et donnez-la au prêtre Éléazar, pour l'offrande de l'Éternel.
Utenge zimenezo pa theka la gawo la ankhondowo ndipo upereke kwa wansembe Eliezara kuti zikhale zopereka zanu kwa Yehova.
30 Sur la moitié des enfants d'Israël, tu prendras une personne tirée sur cinquante, du bétail, des ânes et des troupeaux, de tout le bétail, et tu la donneras aux Lévites, qui font le service de la tente de Yahvé. »
Kuchokera pa theka la gawo la Aisraeli, utengeko cholanda chimodzi pa makumi asanu aliwonse, pa anthu, ngʼombe, abulu, nkhosa, mbuzi kapena zoweta zina. Uzipereke kwa Alevi amene ntchito yawo ndi yosamalira tenti ya Yehova.”
31 Moïse et le prêtre Éléazar firent ce que l'Éternel avait ordonné à Moïse.
Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara anachita monga Yehova analamulira Mose.
32 Or le butin, en sus du butin que les hommes de guerre avaient pris, fut de six cent soixante-quinze mille brebis,
Zotsala pa zolanda ku nkhondo zimene ankhondowo anatenga zinali nkhosa 675,000,
33 soixante-douze mille têtes de bétail,
Ngʼombe 72,000,
34 soixante et un mille ânes,
abulu 61,000,
35 et trente-deux mille personnes en tout, des femmes qui n'avaient pas connu d'homme en couchant avec lui.
ndi atsikana omwe sanagonepo ndi mwamuna 32,000.
36 La moitié, qui était la part de ceux qui partaient pour la guerre, était en nombre de trois cent trente-sept mille cinq cents moutons;
Gawo la ankhondo amene anapita ku nkhondo linali: nkhosa 337,500,
37 et le tribut de l'Éternel sur les moutons était de six cent soixante-quinze.
mwa zimenezi gawo la Yehova linali 675;
38 Les bovins étaient au nombre de trente-six mille, et le tribut de l'Éternel était de soixante-douze.
ngʼombe zinalipo 36,000 ndipo gawo la Yehova linali 72;
39 Les ânes étaient au nombre de trente mille cinq cents; le tribut de l'Éternel était de soixante et un.
abulu analipo 30,500 ndipo gawo la Yehova linali 61;
40 Les personnes étaient au nombre de seize mille; le tribut de l'Éternel était de trente-deux personnes.
anthu analipo 16,000 ndipo gawo la Yehova linali 32.
41 Moïse remit au sacrificateur Éléazar le tribut, qui était l'ondoiement de l'Éternel, comme l'Éternel l'avait ordonné à Moïse.
Mose anapereka kwa wansembe Eliezara gawo limene linali loyenera kupereka kwa Yehova monga momwe Yehova analamulira Mose.
42 Sur la moitié des enfants d'Israël, que Moïse sépara des hommes qui avaient combattu
Pa gawo la Aisraeli, Mose anapatula theka limodzi kuchotsa pa zolanda ku nkhondo zonse zimene zinabwera ndi ankhondo aja.
43 (la moitié de l'assemblée était de trois cent trente-sept mille cinq cents moutons,
Tsono gawo la Aisraeli linali ili: nkhosa 337,500,
44 trente-six mille têtes de bétail,
ngʼombe 36,000,
45 trente mille cinq cents ânes
abulu 30,500,
46 et seize mille personnes),
anthu 16,000.
47 sur la moitié des enfants d'Israël, Moïse prit un homme et un animal sur cinquante, et les donna aux Lévites, qui faisaient le service du tabernacle de Yahvé, comme Yahvé l'avait ordonné à Moïse.
Kuchoka pa gawo la Aisraelilo, Mose anatengapo chimodzi pa zolanda ku nkhondo makumi asanu aliwonse, anthu ndi nyama, ndipo anazipereka kwa Alevi amene ankayangʼanira tenti ya Yehova monga Yehova analamulira Mose.
48 Les officiers qui commandaient les milliers de l'armée, les chefs de milliers et les chefs de centaines, s'approchèrent de Moïse.
Pamenepo omwe ankayangʼanira magulu a ankhondo olamulira 1,000 ndi olamulira 100 anabwera kwa Mose,
49 Ils dirent à Moïse: « Tes serviteurs ont fait le compte des hommes de guerre qui sont sous nos ordres, et il ne manque pas un seul homme parmi nous.
iwo anati kwa iye, “Ife anthu anu tawerenga ankhondo amene timawalamulira. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe amene wasowa.
50 Nous avons apporté l'offrande de l'Éternel, ce que chacun a trouvé: des ornements en or, des bracelets, des bagues, des anneaux, des boucles d'oreilles et des colliers, pour faire l'expiation de nos âmes devant l'Éternel. »
Ndipo tabweretsa zopereka kwa Yehova zimene munthu aliyense anapeza: ziwiya zagolide, zibangiri, zigwinjiri, mphete zosindikizira, ndolo ndi mikanda kuti tichitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.”
51 Moïse et le sacrificateur Éléazar prirent leur or, tous les bijoux travaillés.
Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara analandira kuchokera kwa atsogoleriwo golide pamodzi ndi zipangizo zonse zosula.
52 Tout l'or de l'ondoiement qu'ils offrirent à l'Éternel, des chefs de milliers et des chefs de centaines, fut de seize mille sept cent cinquante sicles.
Golide yense wochokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 zomwe Mose ndi Eliezara anapereka ngati mphatso kwa Yehova zinali zolemera makilogalamu 200.
53 Les hommes de guerre avaient fait du butin, chacun pour soi.
Wankhondo aliyense anatenga zomwe analanda yekha ku nkhondo.
54 Moïse et le prêtre Éléazar prirent l'or des chefs de milliers et des chefs de centaines, et l'apportèrent dans la tente d'assignation, comme souvenir pour les enfants d'Israël devant l'Éternel.
Mose ndi Eliezara wansembe analandira golide kuchokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 ndi kukamuyika mu tenti ya msonkhano ngati chikumbutso cha Aisraeli pamaso pa Yehova.

< Nombres 31 >