< Hébreux 6 >

1 C'est pourquoi, laissant l'enseignement des premiers principes de Christ, poussons à la perfection, en posant de nouveau le fondement de la repentance des œuvres mortes, de la foi en Dieu,
Tsono tiyeni tisangoyima pa maphunziro oyambirira enieni a Khristu koma tipitirire kuti mukule msinkhu. Tisaphunzitsenso zinthu zomwe zili ngati maziko, monga za kutembenuka mtima kusiya ntchito zosapindulitsa pa moyo wosatha, za kukhulupirira Mulungu,
2 de l'enseignement des baptêmes, de l'imposition des mains, de la résurrection des morts et du jugement éternel. (aiōnios g166)
za maubatizo, za kusanjika manja, za kuuka kwa akufa ndi za chiweruzo chotsiriza. (aiōnios g166)
3 C'est ce que nous ferons, si Dieu le permet.
Ndipo Mulungu akalola, tidzaterodi.
4 En effet, pour ce qui est de ceux qui ont été autrefois éclairés, qui ont goûté au don céleste, qui ont été rendus participants du Saint-Esprit,
Nʼkosatheka kuwabwezanso anthu amene nthawi ina anawunikiridwa. Iwowa analawapo mphatso yochokera kumwamba, nʼkulandira nawo Mzimu Woyera.
5 qui ont goûté à la bonne parole de Dieu et aux puissances du siècle à venir, (aiōn g165)
Analawa kukoma kwa mawu a Mulungu ndi mphamvu za nthawi ikubwera. (aiōn g165)
6 et qui sont tombés ensuite, il est impossible de les ramener à la repentance, puisqu'ils crucifient de nouveau le Fils de Dieu pour eux-mêmes et l'exposent à l'ignominie.
Popeza anabwerera mʼmbuyo, nʼkosatheka kuti atembenukenso mtima chifukwa akupachikanso Mwana wa Mulungu ndi kumunyozetsa poyera.
7 Car la terre qui a bu la pluie qui tombe souvent sur elle et qui produit une récolte convenable pour ceux pour qui elle est aussi cultivée, reçoit la bénédiction de Dieu;
Nthaka yolandira mvula kawirikawiri nʼkubala mbewu zopindulitsa oyilima, Mulungu amayidalitsa.
8 mais si elle porte des épines et des chardons, elle est rejetée et près d'être maudite, sa fin étant d'être brûlée.
Koma nthaka yobereka minga ndi nthula ndi yopanda phindu ndipo ili pafupi kutembereredwa. Matsiriziro ake idzatenthedwa mʼmoto.
9 Mais, bien-aimés, nous sommes persuadés de choses meilleures pour vous, et de choses qui accompagnent le salut, bien que nous parlions ainsi.
Okondedwa anga, ngakhale tikuyankhula zimenezi, ife tikudziwa kuti muli nazo zinthu zabwino zomwe zimabwera pamodzi ndi chipulumutso.
10 Car Dieu n'est pas injuste, au point d'oublier votre œuvre et le travail d'amour que vous avez montré envers son nom, en ce que vous avez servi les saints, et que vous les servez encore.
Mulungu ndi wolungama, sangayiwale ntchito zanu ndi chikondi chanu chimene munamuonetsa pothandiza anthu ake monga mmene mukuchitirabe tsopano.
11 Nous désirons que chacun de vous fasse preuve du même empressement jusqu'à la fin de la plénitude de l'espérance,
Ife tikufuna kuti aliyense wa inu aonetse changu chomwechi mpaka kumapeto, kuti zichitikedi zomwe mukuyembekezera.
12 afin que vous ne soyez pas paresseux, mais imitateurs de ceux qui, par la foi et la persévérance, ont hérité des promesses.
Ife sitikufuna kuti inu mukhale aulesi, koma mutsatire anthu amene, pokhulupirira ndi kupirira, akulandira zimene zinalonjezedwa.
13 En effet, lorsque Dieu fit une promesse à Abraham, comme il ne pouvait jurer par personne de plus grand, il jura par lui-même,
Pamene Mulungu ankamulonjeza Abrahamu, popeza panalibe wamkulu womuposa, amene akanamutchula ndikulumbira mwa Iye, analumbira mwa Iye yekha kuti,
14 en disant: « Je te bénirai, et je te multiplierai. »
“Ine ndidzakudalitsa ndithu, ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.”
15 C'est ainsi qu'ayant supporté patiemment, il obtint la promesse.
Ndipo Abrahamu atayembekezera mofatsa, analandira zimene anamulonjezazo.
16 Les hommes, en effet, jurent par un plus grand, et dans toute contestation de leur part, le serment est définitif pour confirmation.
Anthu amalumbira mʼdzina la wina amene akuwaposa, ndipo lumbiro lotere limatsimikizira zomwe zayankhulidwa ndi kuthetsa mikangano yonse.
17 C'est ainsi que Dieu, voulant montrer plus abondamment aux héritiers de la promesse l'immuabilité de son conseil, s'est interposé par un serment,
Momwemonso Mulungu pofuna kutsimikizira anthu amene adzalandire lonjezo, kuti Iye sangasinthe maganizo, anatsimikiza lonjezo lakelo ndi lumbiro.
18 afin que, par deux choses immuables, dans lesquelles il est impossible que Dieu mente, nous soyons fortement encouragés, nous qui avons fui pour trouver un refuge, à saisir l'espérance qui nous est proposée.
Mulungu anachita zinthu ziwiri, lonjezo ndi lumbiro, zimene sizingathe kusintha ndipo Mulungu sangathe kunama. Choncho Mulungu akutilimbikitsa mtima ife amene tinathawira kwa Iye kuti tichigwiritsitse chiyembekezo chimene tinalandira.
19 Cette espérance, nous l'avons comme une ancre de l'âme, une espérance à la fois sûre et inébranlable, et qui pénètre dans ce qui est au delà du voile,
Chiyembekezo chimenechi tili nacho ngati nangula wa moyo wathu. Nʼchokhazikika ndi chosagwedezeka ndipo chimalowa mʼkatikati mwa malo opatulika, kuseri kwa chinsalu chotchinga.
20 où Jésus est entré pour nous comme précurseur, étant devenu souverain sacrificateur pour toujours selon l'ordre de Melchisédek. (aiōn g165)
Yesu anatitsogolera kupita kumeneko, nalowako mʼmalo mwathu. Iye anasanduka Mkulu wa ansembe onse wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki. (aiōn g165)

< Hébreux 6 >