< 1 Corinthians 3 >

1 And I, my brethren, could not speak to you, as to spiritual persons, but as to carnal ones, even as to babes in Christ.
Ndipo abale sindikanakuyankhulani ngati auzimu koma adziko lapansi, makanda chabe mwa Khristu.
2 I have fed you with milk, and not with meat; for ye were not hitherto able to bear it, nor yet are ye even now able.
Ndinakupatsani mkaka osati chakudya cholimba pakuti munali musanakonzeke kuchilandira. Zoonadi, simunakonzekebe.
3 Because ye are still carnal: for while there is among you envy and strife and divisions, are ye not carnal, and do ye not walk as men?
Mukanali adziko lapansi. Pakuti pakati panu pali kaduka ndi kukangana, kodi si inu a dziko lapansi? Kodi simukuchita ngati anthu wamba?
4 For when one saith, I am of Paul; and another, I am of Apollos, are ye not carnal?
Pamene wina anena kuti, “Ine ndimatsatira Paulo,” ndipo wina akuti, “Ine ndimatsatira Apolo,” Kodi si inu akunja?
5 Who then is Paul, and who is Apollos, but ministers by whose means ye embraced the faith, even as the Lord gave success to each of them?
Ndiponso kodi Apolo ndi ndani? Nanga Paulo ndi ndani? Otumikira chabe, omwe kudzera mwa iwo inu munakhulupirira monga Ambuye anawagawira aliyense ntchito yake.
6 I have planted, Apollos watered: but God gave the increase.
Ine ndinadzala mbewu, Apolo anayithirira, koma Mulungu ndiye anayikulitsa.
7 So that neither he that planteth is any thing, nor he that watereth, but God that giveth the increase.
Choncho kuphatikiza iye wodzala ndi iye wothirira, onse sali kanthu, koma Mulungu yekha amene amakulitsa zinthu.
8 And he that planteth, and he that watereth, are as one: but each shall receive his own reward according to his own labor.
Munthu wodzala ndi munthu wothirira ali ndi cholinga chimodzi, ndipo aliyense adzapatsidwa mphotho molingana ndi ntchito yake.
9 For we are fellow-laborers, the servants of God: and ye are the husbandry of God, ye are the building of God.
Pakuti ife ndife antchito anzake a Mulungu; inu ndinu munda wa Mulungu, Nyumba ya Mulungu.
10 According to the grace of God given to me, as a wise architect I have laid the foundation, and another buildeth thereon: but let every one see to it how he buildeth thereon.
Mwachisomo chimene Mulungu wandipatsa, ine ndinayika maziko monga mmisiri waluntha, ndipo ena akumangapo. Koma aliyense ayenera kuchenjera mmene akumangira.
11 For no one can lay any other foundation, but that which is laid, which is Jesus Christ: and if any build upon this foundation gold,
Pakuti wina sangayikenso maziko ena oposera amene anakhazikitsidwa kale, amene ndi Yesu Khristu.
12 silver, precious stones, or wood, hay, stubble;
Ngati munthu aliyense amanga pa maziko awa pogwiritsa ntchito golide, siliva, miyala yamtengowapatali, milimo yamitengo, tsekera kapena udzu,
13 every man's work shall be made manifest. For the great day will shew it; because it will be discovered by fire, and the fire will prove every man's work of what sort it is.
ntchito yake idzaonekera pamene Tsiku la chiweruzo lidzazionetsa poyera. Tsikulo lidzafika ndi moto, ndipo motowo ndi umene udzayesa ntchito ya munthu aliyense.
14 If any man's work abide, which he hath built upon it, he shall receive a reward:
Ngati zimene zamangidwazo sizidzagwa, adzalandira mphotho yake.
15 but if any man's work be burnt, he will be damaged; though he himself shall be saved, but, as it were out of fire.
Ndipo ngati zidzanyeke ndi moto, sadzalandira mphotho koma iye mwini adzapulumukabe, koma monga ngati munthu amene wapulumuka mʼmoto.
16 Do ye not know that ye are the temple of God, and the Spirit of God dwelleth in you?
Kodi inu simukudziwa kuti ndinu Nyumba ya Mulungu ndipo kuti Mzimu wa Mulungu amakhala mwa inu?
17 If any one destroy the temple of God, him will God destroy: for the temple of God is holy, and this temple are ye.
Ngati wina aliyense awononga Nyumba ya Mulunguyo, Mulungu nayenso adzamuwononga ameneyo; popeza Nyumba ya Mulungu ndi yopatulika ndipo Nyumbayo ndi inu amene.
18 Let no one deceive himself: if any among you seem to be wise in this world, let him become a fool, that he may be truly wise. (aiōn g165)
Choncho musadzinyenge. Ngati wina wa inu akuganiza kuti ndi wanzeru pa mulingo wa mʼbado uno, ayenera kukhala “wopusa” kuti athe kukhala wanzeru. (aiōn g165)
19 For the wisdom of this world is foolishness with God; for it is written, "He taketh the wise in their own craftiness:"
Pakuti nzeru ya dziko lapansi ndi yopusa pamaso pa Mulungu. Monga kwalembedwera kuti, “Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,”
20 and again, "The Lord knoweth the thoughts of the wise, that they are vain."
ndiponso, “Ambuye amadziwa kuti maganizo a wanzeru ndi opandapake.”
21 Therefore let no one glory in men: for all things are yours;
Choncho, wina asanyadire anthu chabe! Zonse ndi zanu,
22 whether Paul, or Apollos, or Cephas, or the world, or life, or death, or things present, or future, all are yours;
kaya Paulo kapena Apolo kapena Kefa kapena dziko lapansi, kapena moyo, kapena imfa, kapena tsopano, kapena mʼtsogolo, zonse ndi zanu,
23 and ye are Christ's; and Christ is God's.
ndipo inu ndinu a Khristu, ndipo Khristu ndi wa Mulungu.

< 1 Corinthians 3 >