< Matthew 24 >

1 Jesus went out from the temple, and was going on his way. His disciples came to him to show him the buildings of the temple.
Yesu anatuluka mʼNyumba ya Mulungu ndipo akuchoka ophunzira ake anadza kwa Iye ndi kumuonetsa mamangidwe a Nyumbayo.
2 But he answered them, “You see all of these things, don’t you? Most certainly I tell you, there will not be left here one stone on another, that will not be thrown down.”
Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukuona zinthu zonsezi? Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti palibe mwala pano umene udzasiyidwe pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”
3 As he sat on the Mount of Olives, the disciples came to him privately, saying, “Tell us, when will these things be? What is the sign of your coming, and of the end of the age?” (aiōn g165)
Pamene Yesu anakhala pansi pa phiri la Olivi, ophunzira ake anabwera kwa Iye mwamseri nati, “Tiwuzeni, kodi izi zidzachitika liti, ndipo chizindikiro cha kubwera kwanu ndi zizindikiro za kutha kwa dziko zidzakhala chiyani?” (aiōn g165)
4 Jesus answered them, “Be careful that no one leads you astray.
Yesu anayankha kuti, “Onetsetsani kuti wina asakunyengeni.
5 For many will come in my name, saying, ‘I am the Christ,’ and will lead many astray.
Pakuti ambiri adzabwera mʼdzina langa nadzati, ‘Ndine Khristu,’ ndipo adzanyenga ambiri.
6 You will hear of wars and rumors of wars. See that you aren’t troubled, for all this must happen, but the end is not yet.
Mudzamva za nkhondo ndi mbiri za nkhondo, koma onetsetsani kuti musadzidzimuke nazo. Zotere ziyenera kuchitika, koma chimaliziro sichinafike.
7 For nation will rise against nation, and kingdom against kingdom; and there will be famines, plagues, and earthquakes in various places.
Mtundu ndi mtundu udzawukirana, ndipo ufumu ndi ufumu udzawukirana. Kudzakhala njala ndi zivomerezi mʼmalo osiyanasiyana.
8 But all these things are the beginning of birth pains.
Zonsezi ndi chiyambi chabe cha zowawa.
9 “Then they will deliver you up to oppression and will kill you. You will be hated by all of the nations for my name’s sake.
“Pamenepo adzakuperekani kuti mukazunzidwe ndi kuphedwa, ndipo mitundu yonse idzakudani chifukwa cha Ine.
10 Then many will stumble, and will deliver up one another, and will hate one another.
Pa nthawi imeneyo ambiri adzasiya chikhulupiriro ndipo adzadana ndi kuperekana wina ndi mnzake,
11 Many false prophets will arise and will lead many astray.
ndipo aneneri onama ambiri adzaoneka ndi kunyenga anthu ambiri.
12 Because iniquity will be multiplied, the love of many will grow cold.
Chifukwa cha kuchuluka kwa zoyipa, chikondi cha ambiri chidzazirala,
13 But he who endures to the end will be saved.
koma wopirira kufikira chimaliziro adzapulumuka.
14 This Good News of the Kingdom will be preached in the whole world for a testimony to all the nations, and then the end will come.
Ndipo uthenga wa ufumu udzalalikidwa ku dziko lonse lapansi ngati umboni kwa mitundu yonse, ndipo pomwepo chimaliziro chidzafika.”
15 “When, therefore, you see the abomination of desolation, which was spoken of through Daniel the prophet, standing in the holy place (let the reader understand),
“Tsono mukadzaona chinthu chonyansa chosakaza chitayima pamalo oyera chimene anayankhula mneneri Danieli, owerengayo azindikire.
16 then let those who are in Judea flee to the mountains.
Pamenepo amene ali ku Yudeya athawire ku mapiri.
17 Let him who is on the housetop not go down to take out the things that are in his house.
Yemwe ali pa denga la nyumba yake asatsike kukatulutsa chinthu chilichonse mʼnyumba.
18 Let him who is in the field not return back to get his clothes.
Yemwe ali ku munda asapite kukatenga mkanjo wake.
19 But woe to those who are with child and to nursing mothers in those days!
Kudzakhala koopsa kwambiri masiku amenewo kwa amayi oyembekezera ndi kwa oyamwitsa!
20 Pray that your flight will not be in the winter nor on a Sabbath,
Pempherani kuti kuthawa kwanu kusadzachitike nthawi yozizira kapena pa Sabata.
21 for then there will be great suffering, such as has not been from the beginning of the world until now, no, nor ever will be.
Popeza kudzakhala masautso aakulu, omwe safanana ndi ena ali onse chiyambireni cha dziko lapansi mpaka lero lino ndipo sadzafanananso ndi ena.
22 Unless those days had been shortened, no flesh would have been saved. But for the sake of the chosen ones, those days will be shortened.
Ngati masiku amenewo sakanafupikitsidwa, palibe mmodzi akanapulumuka, koma chifukwa cha osankhidwawo masiku amenewo adzafupikitsidwa.
23 “Then if any man tells you, ‘Behold, here is the Christ!’ or, ‘There!’ don’t believe it.
Pa nthawi imeneyo ngati wina adzati kwa inu, ‘Onani, Khristu ali pano!’ Kapena, ‘Uyo ali ukoyo!’ Musakhulupirire.
24 For false christs and false prophets will arise, and they will show great signs and wonders, so as to lead astray, if possible, even the chosen ones.
Chifukwa akhristu onama ndi aneneri onama adzaoneka ndipo adzachita zizindikiro zazikulu ndi zodabwitsa kuti akanyenge ngakhale osankhidwawo ngati kukanakhala kotheka kutero.
25 “Behold, I have told you beforehand.
Onani, ndakuwuzani izi nthawi isanafike.
26 “If therefore they tell you, ‘Behold, he is in the wilderness,’ don’t go out; or ‘Behold, he is in the inner rooms,’ don’t believe it.
“Ndiye ngati wina akuwuzani inu kuti, ‘Uyo ali ku chipululu,’ inu musapiteko; kapena akati, ‘Uyu ali kuno mʼchipinda chamʼkati,’ musakhulupirire.
27 For as the lightning flashes from the east, and is seen even to the west, so will the coming of the Son of Man be.
Monga momwe mphenzi ingʼanima kuchokera kummawa kupita kumadzulo, momwemonso kudzakhala kubwera kwa Mwana wa Munthu.
28 For wherever the carcass is, that is where the vultures gather together.
Kulikonse kuli chinthu cha kufa, makwangwala adzasonkhanako.
29 “But immediately after the suffering of those days, the sun will be darkened, the moon will not give its light, the stars will fall from the sky, and the powers of the heavens will be shaken;
“Akadzangotha mavuto a masiku amenewo, “‘dzuwa lidzadetsedwa, ndipo mwezi sudzawala; nyenyezi zidzagwa kuchokera kumwamba, ndipo mphamvu za mmwamba zidzagwedezeka.’
30 and then the sign of the Son of Man will appear in the sky. Then all the tribes of the earth will mourn, and they will see the Son of Man coming on the clouds of the sky with power and great glory.
“Pa nthawi imeneyo chizindikiro cha Mwana wa Munthu chidzaoneka mlengalenga, ndipo mitundu yonse ya pa dziko lapansi idzalira. Idzaona Mwana wa Munthu akubwera ndi mitambo, mphamvu ndi ulemerero waukulu.
31 He will send out his angels with a great sound of a trumpet, and they will gather together his chosen ones from the four winds, from one end of the sky to the other.
Ndipo adzatuma angelo ake, ndi kulira kwa lipenga kwakukulu, nadzasonkhanitsa osankhidwa ake kuchokera ku mphepo zinayi, ndi kuchokera kumathero a thambo kufika mbali ina.
32 “Now from the fig tree learn this parable: When its branch has now become tender and produces its leaves, you know that the summer is near.
“Tsopano kuchokera ku mtengo wamkuyu phunzirani ichi: Pamene uyamba kuphukira, masamba ake akatuluka, mumadziwa kuti dzinja layandikira.
33 Even so you also, when you see all these things, know that he is near, even at the doors.
Momwemonso, pamene mudzaona zinthu zonsezi mudzadziwe kuti ali pafupi pa khomo penipeni.
34 Most certainly I tell you, this generation will not pass away until all these things are accomplished.
Zoonadi, ndikuwuzani kuti mʼbado uwu sudzatha mpaka zinthu zonse zitachitika.
35 Heaven and earth will pass away, but my words will not pass away.
Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”
36 “But no one knows of that day and hour, not even the angels of heaven, but my Father only.
“Palibe amene adziwa za tsikulo kapena nthawi, angakhale angelo akumwamba, angakhale Mwana, koma Atate okha.
37 As the days of Noah were, so will the coming of the Son of Man be.
Monga momwe zinalili nthawi ya Nowa, momwemonso zidzatero pobwera kwa Mwana wa Munthu.
38 For as in those days which were before the flood they were eating and drinking, marrying and giving in marriage, until the day that Noah entered into the ship,
Pakuti masiku amenewo chisanafike chigumula, anthu amadya ndi kumwa, kukwatira ndi kukwatiwa, mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchombo;
39 and they didn’t know until the flood came and took them all away, so will the coming of the Son of Man be.
ndipo sanadziwe za chimene chikanachitika mpaka pamene chigumula chinafika ndi kuwamiza onse. Umu ndi mmene zidzakhalira pobwera kwa Mwana wa Munthu.
40 Then two men will be in the field: one will be taken and one will be left.
Amuna awiri adzakhala mʼmunda; wina adzatengedwa ndi wina adzatsala.
41 Two women will be grinding at the mill: one will be taken and one will be left.
Amayi awiri adzakhala akusinja pa mtondo; wina adzatengedwa ndi wina adzatsala.
42 Watch therefore, for you don’t know in what hour your Lord comes.
“Chifukwa chake yangʼanirani, popeza simudziwa tsiku lanji limene Ambuye anu adzabwera.
43 But know this, that if the master of the house had known in what watch of the night the thief was coming, he would have watched, and would not have allowed his house to be broken into.
Koma zindikirani ichi: Ngati mwini nyumba akanadziwa nthawi yanji ya usiku imene mbala imabwera, sakanagona ndipo sakanalola kuti nyumba yake ithyoledwe.
44 Therefore also be ready, for in an hour that you don’t expect, the Son of Man will come.
Inunso tsono muyenera kukhala okonzeka, chifukwa Mwana wa Munthu adzabwera pa nthawi imene inu simukumuyembekezera.
45 “Who then is the faithful and wise servant, whom his lord has set over his household, to give them their food in due season?
“Kodi wantchito wokhulupirika ndi wanzeru amene ambuye ake anamuyika kukhala woyangʼanira antchito a mʼnyumba kuti awapatse chakudya chawo pa nthawi yake ndani?
46 Blessed is that servant whom his lord finds doing so when he comes.
Chidzakhala chabwino kwa wantchitoyo ngati mbuye wake pofika adzamupeza akuchita zimenezi.
47 Most certainly I tell you that he will set him over all that he has.
Zoonadi, ndikuwuzani kuti adzamuyika kukhala woyangʼanira katundu wake yense.
48 But if that evil servant should say in his heart, ‘My lord is delaying his coming,’
Koma tiyerekeze kuti wantchitoyo ndi woyipa, nati kwa iye yekha, ‘Mbuye wanga akuchedwa kubwera,’
49 and begins to beat his fellow servants, and eat and drink with the drunkards,
nayamba kumenya antchito anzake, nadya ndi kumwa ndi zidakwa.
50 the lord of that servant will come in a day when he doesn’t expect it and in an hour when he doesn’t know it,
Mbuye wa wantchitoyo adzabwera pa tsiku limene iye samamuyembekezera ndi pa nthawi imene iye sakuyidziwa.
51 and will cut him in pieces and appoint his portion with the hypocrites. That is where the weeping and grinding of teeth will be.
Adzamulanga koopsa ndipo adzamuyika kokhala anthu achiphamaso, kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.”

< Matthew 24 >