< 1 Corinthians 16 >

1 Now concerning the collection for the saints: as I commanded the assemblies of Galatia, you do likewise.
Tsopano za zopereka zothandiza anthu a Ambuye a ku Yerusalemu. Muchite zomwe ndinawuza mipingo ya ku Galatiya kuti ichite.
2 On the first day of every week, let each one of you save as he may prosper, that no collections are made when I come.
Pa tsiku loyamba la sabata lililonse, aliyense wa inu azipatula ndalama molingana ndi zomwe wapezera. Asunge, kuti ndikabwera pasadzakhalenso msonkhamsonkha.
3 When I arrive, I will send whoever you approve with letters to carry your gracious gift to Jerusalem.
Pamenepo, ndikadzafika, ndidzawapatsa makalata a umboni anthu amene mudzawasankhe ndi kuwatuma kuti akapereka mphatso zanu ku Yerusalemu.
4 If it is appropriate for me to go also, they will go with me.
Ngati kutaoneka kuti nʼkoyenera kuti ndipite nawo, adzapita nane limodzi.
5 I will come to you when I have passed through Macedonia, for I am passing through Macedonia.
Ndidzafika kwanuko nditadutsa ku Makedoniya pakuti ndikuyembekezera kudzera ku Makedoniyako.
6 But with you it may be that I will stay with you, or even winter with you, that you may send me on my journey wherever I go.
Mwina ndidzakhala nanu kanthawi kochepa kapenanso nyengo yonse yozizira, kuti mudzandithandize kupitiriza ulendo wanga kulikonse kumene ndingapite.
7 For I do not wish to see you now in passing, but I hope to stay a while with you, if the Lord permits.
Sindikufuna kuti ndikuoneni tsopano mongodutsa chabe, koma ndikuyembekezera kudzakhala nanu kwa kanthawi, ngati Ambuye alola.
8 But I will stay at Ephesus until Pentecost,
Koma ndikhala ndili ku Efeso mpaka nthawi ya Pentekosite,
9 for a great and effective door has opened to me, and there are many adversaries.
pakuti mwayi waukulu wapezeka woti nʼkugwira ntchito yaphindu, koma pali ambiri amene akutsutsana nane.
10 Now if Timothy comes, see that he is with you without fear, for he does the work of the Lord, as I also do.
Ngati Timoteyo afike kwanuko, onetsetsani kuti pasakhale zina zomuchititsa mantha pamene ali pakati panu, pakuti iye akugwira ntchito ya Ambuye monga ine.
11 Therefore let no one despise him. But set him forward on his journey in peace, that he may come to me; for I expect him with the brothers.
Wina aliyense asamunyoze. Muthandizeni kupitiriza ulendo wake mwamtendere kubwereranso kuli ine. Ndikumuyembekeza pamodzi ndi abale ena.
12 Now concerning Apollos the brother, I strongly urged him to come to you with the brothers, but it was not at all his desire to come now; but he will come when he has an opportunity.
Tsono kunena za mʼbale wathu, Apolo, ndinamuwumiriza kwambiri kuti abwere kwa inu abale, ndipo iye sanafune kupita tsopano. Koma akadzapeza mpata wabwino adzabwera.
13 Watch! Stand firm in the faith! Be courageous! Be strong!
Khalani tcheru; khazikikani mʼchikhulupiriro chanu; limbani mtima; khalani amphamvu.
14 Let all that you do be done in love.
Chitani zonse mwachikondi.
15 Now I beg you, brothers—you know the house of Stephanas, that it is the first fruits of Achaia, and that they have set themselves to serve the saints—
Mukudziwa kuti a mʼbanja la Stefano ndiye anali oyamba kutembenuka mtima ku Akaya, ndipo akhala akudzipereka kutumikira oyera mtima. Choncho ndikukudandaulirani, inu abale,
16 that you also be in subjection to such, and to everyone who helps in the work and labors.
kuti muziwamvera anthu oterewa, ndiponso aliyense wogwira nawo ntchitoyi modzipereka.
17 I rejoice at the coming of Stephanas, Fortunatus, and Achaicus; for that which was lacking on your part, they supplied.
Ndikondwera kuti Stefano, Fortunato ndi Akayiko afika, chifukwa akhala akundithandiza pakuti inu simuli nane.
18 For they refreshed my spirit and yours. Therefore acknowledge those who are like that.
Pakuti anatsitsimutsa mzimu wanga ndi wanu womwe. Anthu a mtundu oterewa ngofunika kuwalemekeza.
19 The assemblies of Asia greet you. Aquila and Priscilla greet you warmly in the Lord, together with the assembly that is in their house.
Mpingo wa mʼchigawo cha ku Asiya ukupereka moni. Akula ndi Prisila akuperekanso moni wachisangalalo, mwa Ambuye, ndiponso mpingo umene umakumana mʼnyumba mwawo ukupereka moni.
20 All the brothers greet you. Greet one another with a holy kiss.
Abale onse kuno akupereka moni wawo. Patsanani moni wachikondi chenicheni.
21 This greeting is by me, Paul, with my own hand.
Ineyo Paulo, ndikulemba ndi dzanja langa mawu awa akuti moni.
22 If any man doesn’t love the Lord Jesus Christ, let him be cursed. Come, Lord!
Ngati wina sakonda Ambuye akhale wotembereredwa. Maranatha! (Ambuye athu bwerani)!
23 The grace of the Lord Jesus Christ be with you.
Chisomo cha Ambuye Yesu chikhale ndi inu.
24 My love to all of you in Christ Jesus. Amen.
Chikondi changa chikhale ndi nonsenu mwa Khristu Yesu.

< 1 Corinthians 16 >