< Proverbs 9 >

1 Wisdom hath built her house, she hath hewn out her seven pillars:
Nzeru inamanga nyumba yake; inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.
2 She hath killed her beasts; she hath mixed her wine; she hath also furnished her table.
Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake; inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.
3 She hath sent forth her maidens: she crieth upon the highest places of the city,
Nzeruyo inatuma adzakazi ake, kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,
4 Whoever is simple, let him turn in here: as for him that lacketh understanding, she saith to him,
“Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!” Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,
5 Come, eat of my bread, and drink of the wine which I have mixed.
“Bwerani, dzadyeni chakudya changa ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.
6 Forsake the foolish, and live; and go in the way of understanding.
Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo; yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”
7 He that reproveth a scorner getteth to himself shame: and he that rebuketh a wicked man getteth himself a blot.
Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo; aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.
8 Reprove not a scorner, lest he shall hate thee: rebuke a wise man, and he will love thee.
Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe; dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.
9 Give instruction to a wise man, and he will be yet wiser: teach a just man, and he will increase in learning.
Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru; ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.
10 The fear of the LORD is the beginning of wisdom: and the knowledge of the Holy One is understanding.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru; kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.
11 For by me thy days shall be multiplied, and the years of thy life shall be increased.
Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka, ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.
12 If thou art wise, thou shalt be wise for thyself: but if thou scornest, thou alone shalt bear it.
Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa; ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.
13 A foolish woman is clamorous: she is simple, and knoweth nothing.
Uchitsiru ndi mkazi waphokoso, wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.
14 For she sitteth at the door of her house, on a seat in the high places of the city,
Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake, pamalo aatali a mu mzinda,
15 To call those who pass by who go right on their ways:
kuti aziyitana anthu ongodutsa, amene akunka nayenda njira zawo.
16 Whoever is simple, let him turn in here: and as for him that lacketh understanding, she saith to him,
Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,” ndipo kwa wopanda nzeru amati,
17 Stolen waters are sweet, and bread eaten in secret is pleasant.
“Madzi akuba ndiye amatsekemera; chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”
18 But he knoweth not that the dead are there; and that her guests are in the depths of hell. (Sheol h7585)
Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko, ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya. (Sheol h7585)

< Proverbs 9 >