< Matthew 22 >

1 Then Jesus told [the Jewish leaders] other parables [in order to illustrate what will happen to the people who do not accept him as the King God promised to send]. [This is one of those parables: ]
Yesu anayankhula nawonso mʼmafanizo, nati,
2 “[God] [MTY/EUP] [is like] a king [SIM] who [told his servants that they should] make a wedding feast for his son.
“Ufumu wakumwamba uli ngati mfumu imene inakonzera phwando mwana wake wamwamuna.
3 [When] the feast [was ready], the king sent his servants to tell the people who had been {whom he had} invited that it was time for them to come to the wedding feast. [The servants did that]. But the people who had been invited did not want to come.
Anatumiza antchito ake kwa amene anayitanidwa kuphwando koma anakana kubwera.
4 So he sent other servants [to] again [tell the people whom he had invited that they should come to the feast]. He said [to those servants], ‘Say to the people whom I invited [to come to the feast], “The king says that he has prepared the food. The oxen and the fattened calves have been butchered [and cooked]. Everything is ready. It is time [now for you to] come to the wedding feast!’”’
“Kenaka anatumiza antchito ena nati, ‘Awuzeni oyitanidwa kuti phwando lakonzedwa: ndapha ngʼombe yayimuna ndi nyama zina zonenepa ndipo zonse zakonzedwa. Bwerani ku phwando laukwati.’
5 [But when the servants told them that, they] disregarded [what the servants said]. Some of them went to their own fields. Others went to their places of business.
“Koma iwo sanalabadire ndipo anachoka; wina anapita ku munda wake ndi wina ku malonda ake.
6 The rest of them seized the king’s servants, mistreated them, and killed them.
Ndipo otsalawo anagwira antchito ake, nawazunza ndi kuwapha.
7 [When the king heard what had happened], he became furious. He commanded his soldiers to go and kill those murderers and burn their cities.
Mfumu inakwiya. Inatumiza asilikali ake ndipo anawononga opha anzawowo ndi kutentha mzinda wawo.
8 [After his soldiers had done that], the king said to his other servants, ‘I have prepared the [wedding] feast, but the people who were {whom I} invited do not deserve to [come to it because they did not consider it an honor to have been invited].
“Pamenepo anati kwa antchito ake, ‘Phwando laukwati lakonzedwa, koma amene ndinawayitana sanali oyenera.
9 So, go to the intersections of the main streets. Tell whomever you find that they should come to the [wedding] feast.’
Pitani ku mphambano za misewu ndipo kayitaneni aliyense amene mukamupeze kuti abwere ku phwando.’
10 So the servants went there, and they gathered everyone they saw [who wanted to come to the feast]. They gathered [both people that were considered] to be evil and [those that were considered to be] good. They brought them into the hall where the wedding [feast took place]. The hall was filled with people.
Pamenepo antchitowo anapita ku misewu nakasonkhanitsa anthu onse amene anakawapeza, abwino ndi oyipa omwe, ndipo nyumba ya madyerero inadzaza ndi oyitanidwa.
11 But when the king went [into the hall] to see the guests who were there, he saw someone who was not wearing clothes [that had been provided for the guests to wear] at a wedding [feast].
“Koma pamene mfumu inabwera kudzaona oyitanidwawo, inaona munthu amene sanavale zovala zaukwati.
12 The king said to him, ‘Friend, (you should never have entered this hall, because you are not wearing the clothes [that guests wear] at wedding [feasts]!/how did you enter this hall, because you are not wearing the clothes [that are appropriate for guests to wear] at a wedding [feast]?) [RHQ]’ The man did not say anything, [because he did not know what to say].
Inamufunsa kuti, ‘Bwenzi walowa bwanji muno wopanda zovala zaukwati?’ Munthuyo anakhala chete.
13 Then the king said to his attendants, ‘Tie this person’s feet and hands and throw him outside where there is total darkness. People who are there cry out [because they are suffering] and they gnash their teeth [because of their severe pain].’”
“Pamenepo mfumuyo inawuza otumikira kuti, ‘Mʼmangeni manja ndi miyendo, ndipo muponyeni kunja, ku mdima kumene kudzakhale kulira ndi kukuta mano.’
14 [Then Jesus said, “The point of this story is that God] has invited many [to come to him], but only a few people are the ones whom he has chosen [to be there].”
“Popeza oyitanidwa ndi ambiri koma osankhidwa ndi ochepa.”
15 After Jesus said that, the Pharisees met together in order to plan how they could cause him to say something that would enable them to accuse him.
Kenaka Afarisi anatuluka nakakonza njira zomupezera zifukwa Yesu mʼmawu ake.
16 They sent to him some of their disciples, [who thought that the Israelites should pay only the tax that the Jewish authorities required them to pay]. They also sent some members of the party that supported Herod. [The members of that party thought that the Israelites should pay only the tax that the Roman government required them to pay]. [Those who were sent came and] said to Jesus, “Teacher, we know that you are truthful and that you teach the truth about what God wants [us to do]. We also know that you do not change what you teach because of what someone says about you, even if it is an important person who does not like what you [IDM] teach.
Anatumiza ophunzira awo kwa Iye pamodzi ndi Aherodia. Anati, “Aphunzitsi, tidziwa kuti ndinu wangwiro ndi kuti mumaphunzitsa mawu a Mulungu monga mwa choonadi. Simutekeseka ndi anthu, popeza simusamala kuti kodi ndi ndani?
17 So tell us what you think [RHQ] [about this matter]: Is it right that we pay taxes to the Roman government [MTY], or not?”
Tiwuzeni tsono maganizo anu ndi otani, kodi nʼkololedwa kupereka msonkho kwa Kaisara kapena ayi?”
18 But Jesus knew that what they really wanted to do was evil. [They were wanting him to say something that would get him in trouble with either the Jewish authorities or the Roman authorities. So he said to them], “You are (hypocrites/pretending to ask a legitimate question), but you are just wanting [RHQ] me to say something for which you can accuse me.
Koma Yesu podziwa maganizo awo oyipa anati, “Inu achiphamaso, bwanji mufuna kundipezera chifukwa?
19 Show me [one of] the coins with [which people pay] the [Roman] tax.” So they showed him [a coin called] a denarius.
Onetseni ndalama imene mumapereka msonkho.” Iwo anabweretsa dinari,
20 He said to them, “Whose picture is [on] this [coin]? And [whose] name [is on it]?”
ndipo anawafunsa kuti, “Kodi chithunzi ichi ndi malemba awa ndi za ndani?”
21 They answered, “[It has the picture and name of] Caesar, [the head of the Roman government].” Then he said to them, “Okay, give to the government what they [require], and give to God what he [requires].”
Iwo anayankha kuti, “Ndi za Kaisara.” Pamenepo anawawuza kuti, “Perekani kwa Kaisara zake za Kaisara, ndi kwa Mulungu zake za Mulungu.”
22 When those men heard Jesus say that, they marveled [that his answer did not enable anyone to accuse him]. Then they left Jesus.
Atamva izi, anadabwa, ndipo anamusiya Iye, nachoka.
23 During that same day, some Sadducees came to Jesus. [They are a Jewish sect who do not] believe that people will become alive again after they die. They [wanted to] ask [Jesus] a question.
Tsiku lomwelo Asaduki amene amati kulibe za kuukanso, anabwera kwa Iye ndi funso.
24 [In order to discredit the idea that dead people will live again], they said [to him], “Teacher, Moses wrote [in the Scriptures], ‘If a man dies who did not have any children, his brother must marry the [dead man’s] widow in order that she can have a child by him. The child [will be considered] the descendant of the man [who died], [and in that way the dead man will have descendants].’
Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatiwuza kuti munthu akamwalira wosasiya ana, mʼbale wake akuyenera kukwatira mkazi wamasiyeyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo.
25 Well, there were seven boys in a family [living] near us. The oldest one married someone. He [and his wife] did not have any children, and he died. So the second brother married the widow. [But he also died without having a child].
Tsopano panali abale asanu ndi awiri pakati pathu. Woyambayo anakwatira ndipo anamwalira, ndipo popeza analibe ana, mʼbale wake analowa chokolo.
26 The same thing [happened to] the third [brother], and also to the other four [brothers, who one by one married this same woman].
Izi zinachitikiranso mʼbale wa chiwiri ndi wachitatu mpaka wachisanu ndi chiwiri.
27 Last of all, the widow also died.
Pa mapeto pake mkaziyo anamwaliranso.
28 So, at the time when people are raised from the dead, which of the seven [brothers do you think] will be her husband? Keep in mind that they had all been married to her.”
Tsopano, kodi akadzaukitsidwa adzakhala mkazi wa ndani mwa asanu ndi awiriwa popeza aliyense anamukwatirapo?”
29 Jesus replied to them, “You are certainly wrong [in what you are thinking]. You do not know [what is written in] the Scriptures. [You] also do not know [that] God has [the] power [to make people alive again].
Yesu anayankha kuti, “Inu mukulakwitsa chifukwa simukudziwa malemba kapena mphamvu ya Mulungu.
30 The fact is that [the woman will not be the wife of any of them, because] after [God causes all dead] people [to] live again, no one will be married. Instead, [people] will be like the angels in heaven. [They do not marry].
Anthu akadzaukitsidwa, sadzakwatira kapena kukwatiwa; adzakhala ngati angelo kumwamba.
31 But as for dead people becoming alive again, God said something about that. (I’m sure you have read it./Have you not read it?) [RHQ] [Long after Abraham, Isaac, and Jacob had died, God said to Moses],
Koma za kuukitsidwa kwa akufa, kodi simunawerenge zimene Mulungu ananena kwa inu kuti,
32 ‘I am the God whom Abraham [worships] and the God whom Isaac [worships] and the God whom Jacob worships.’ It is not dead people who worship God. It is living people who worship him. [Abraham, Isaac and Jacob died long before Moses lived, but God said that they were still worshipping him, so we know their spirits were still alive]!”
‘Ine ndine Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo?’ Iyeyo si Mulungu wa akufa koma wa amoyo.”
33 When the crowds of people heard [Jesus teach] that, they were amazed.
Magulu a anthu atamva zimenezi, anazizwa ndi chiphunzitso chake.
34 But when the Pharisees heard that Jesus had answered the Sadducees in such a way that the Sadducees could not [think of anything that they might say to] respond to him, the Pharisees gathered together to [plan what they would say to him]. [Then they approached him].
Pakumva kuti Yesu anawakhalitsa chete Asaduki, Afarisi anasonkhana pamodzi.
35 One of them was a man who had studied well the laws [that God gave Moses]. He wanted to see if Jesus [could answer] his question well [or if he would say something wrong]. He asked him,
Mmodzi wa iwo, katswiri wa malamulo anamuyesa Iye ndi funso ndipo anati,
36 “Teacher, which commandment in the laws [that God gave Moses] is the most important?”
“Aphunzitsi, kodi lamulo lalikulu koposa mu malamulo ndi liti?”
37 Jesus [quoted the Scriptures as he replied], “‘You must love the Lord your God with all [IDM] your (inner being/heart). [Show that you love him] in all that you desire, in all that you feel, and in all that you think.’
Yesu anayankha kuti, “Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse ndi moyo wako wonse ndi nzeru zako zonse.
38 That is the most important commandment [in the laws that God gave Moses].
Ili ndi lamulo loyamba ndi loposa onse.
39 The next most important commandment [that everyone must surely obey] is: ‘You must love the people you come in contact with as much as [you love] yourself.’
Ndipo lachiwiri ndi lofanana nalo: ‘Konda mnansi wako monga iwe mwini.’
40 These two commandments are the basis of every law [that Moses wrote in the Scriptures] and also of all that the prophets [wrote].”
Malamulo onse ndi aneneri zakhazikika pa malamulo awiriwa.”
41 While the Pharisees were still gathered together [near] Jesus, he asked them,
Afarisi atasonkhana pamodzi, Yesu anawafunsa kuti,
42 “What do you think about the Messiah? Whose descendant is he?” They said to him, “[He is] the descendant of [King] David.”
“Kodi mukuganiza bwanji za Khristu? Ndi Mwana wa ndani?” Iwo anayankha kuti, “Mwana wa Davide.”
43 Jesus said to them, “[If the Messiah is King David’s descendant], then (David should not have called him ‘Lord’ when David was saying [what] the [Holy] Spirit [prompted him to] say./Why did David call the Messiah ‘Lord’ when David was speaking [what] the [Holy] Spirit [prompted him to] say?) [RHQ]
Iye anawawuza kuti, “Nanga zikutheka bwanji kuti Davide poyankhula mwa Mzimu Woyera amatchula Iye ‘Ambuye?’ Pakuti akuti,
44 [David wrote this in the Scriptures about the Messiah]: ‘God said to my Lord, “Sit [here beside me] on my right, [the place of greatest honor you] [MTY]. [Sit here] while I completely defeat your enemies [MTY].”’
“Ambuye anati kwa Ambuye wanga: ‘Khala pa dzanja langa lamanja mpaka ndiyike adani ako pansi pa mapazi ako.’
45 So, since [King] David called [the Messiah] ‘my Lord’, ([the Messiah] cannot be [just someone] descended from David!/how can he be [only] the descendant of [King] David?) [RHQ] [He must be much greater than David]!”
Ngati tsono Davide amamutchula ‘Ambuye,’ zingatheke bwanji kukhala mwana wake?”
46 No one [who heard what Jesus said] was able to think of even one word to say to him [in response]. And after that, no one else ever dared to ask him another question [to try to trap him].
Panalibe wina anatha kuyankha, ndipo kuchokera pamenepo, panalibe wina anayerekeza kumufunsa funso.

< Matthew 22 >