< Acts 2 >

1 AND when the days of pentecost were fulfilled, while they were assembled all together,
Litafika tsiku la chikondwerero cha Pentekosite, onse anali pamodzi.
2 there was suddenly from heaven the voice as of a mighty wind, and all that house in which they were sitting was filled with it;
Mwadzidzidzi kunamveka mkokomo kuchokera kumwamba ngati wa mphepo yamphamvu, ndipo inadzaza nyumba yonse imene amakhala.
3 and tongues that were divided like fire appeared to them, and sat upon each one of them.
Iwo anaona zinthu zokhala ngati malilime amoto ogawikana ndipo anakhala pa aliyense wa iwo.
4 And they were all filled with the Holy Spirit, and they began to speak in several tongues as the Spirit gave them to speak.
Ndipo onse anadzazidwa ndi Mzimu Woyera, nayamba kuyankhula mu ziyankhulo zina, monga Mzimu Woyerayo anawayankhulitsa.
5 But there were men dwelling in Urishlem who feared Aloha; Jihudoyee, from all the peoples who are under heaven.
Ayuda woopa Mulungu ochokera ku mayiko onse a dziko lapansi ankakhala mu Yerusalemu nthawi imeneyi.
6 And when that voice was made, the whole people assembled and were perturbed, because every man of them heard as they spoke in their (several) tongues.
Utamveka mkokomo uja, gulu la anthu linasonkhana. Anthuwo anadabwa chifukwa aliyense anawamva atumwiwo akuyankhula ziyankhulo zosiyanasiyana.
7 (And) they were all astonished, and wondered, saying one to another, These all who speak, behold, are they not Galiloyee?
Mothedwa nzeru anafunsana kuti, “Kodi anthu onse amene akuyankhulawa si Agalileya?
8 How hear we (then) each in his own tongue in which we were born?
Nanga bwanji aliyense wa ife akuwamva iwo mu chinenero cha kwawo?
9 Parthoyee and Medoyee and Alanoyee, and they who dwell in the Place of Rivers, Jihudoyee and Kapadukoyee, and of the region of Pontos and of Asia;
Apanti, Amedi ndi Aelami; okhala ku Mesopotamiya, ku Yudeya ndi ku Kapadokiya, ku Ponto ndi ku Asiya,
10 and from the land of Phrygia and of Pamphylia and of Metsreen, and the regions of Lybi neighbouring upon Kyrine, and those who come from Rumi, Jihudoyee, and Proselytes,
ku Frugiya ndi Pamfiliya, ku Igupto ndi ku madera a ku Libiya kufupi ndi ku Kurene; alendo ochokera ku Roma,
11 and from Krete and Arabia, behold, we hear them speaking in our tongues the wonders of Aloha.
Ayuda ndi otsatira chipembedzo cha Chiyuda onse pamodzi; Akrete ndi Aarabu, ife tonse tikuwamva akuyankhula za ntchito zodabwitsa za Mulungu mu ziyankhulo zathu.”
12 But all of them were amazed and admired, saying one to another, Of whom is this thing?
Modabwa ndi mothedwa nzeru anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Zimenezi zikutanthauzanji?”
13 But others mocked them, saying, These have drunk new wine, and are inebriate.
Koma ena anawaseka nati, “Aledzera vinyo watsopano.”
14 And afterwards arose Shemun Kipha with the eleven apostles, and lifted up his voice and said to them: Men, Jihudoyee, and all who dwell at Urishlem, be this known to you, and hearken to my words.
Koma Petro anayimirira pamodzi ndi atumwi khumi ndi mmodziwo ndipo anakweza mawu ake nayankhula kwa gulu la anthu nati: “Ayuda anzanga, ndi nonse amene muli mu Yerusalemu, mvetsetsani izi ndipo tcherani khutu ku zimene ndikunena.
15 For not as you suppose are these drunken; for, behold, until now are three hours.
Kunena zoona, anthu awa sanaledzere ayi, monga momwe mukuganizira, pakuti ino ndi 9 koloko mmawa!
16 But this is that spoken of by Joel the prophet:
Koma izi ndi zimene ananena Mneneri Yoweli kuti:
17 It shall be in the last days, saith Aloha, I will pour my Spirit upon all flesh: And your sons and your daughters shall prophesy, And your youths shall see visions,
“‘Mulungu akuti, mʼmasiku otsiriza ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi aakazi adzanenera, anyamata anu adzaona masomphenya, nkhalamba zanu zidzalota maloto.
18 And your elders shall dream dreams: And upon the servants and upon the handmaids Will I pour my Spirit in those days; And they shall prophesy.
Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo, ndipo iwo adzanenera.
19 And I will give signs in heaven, And mighty (deeds) on earth; Blood and fire and clouds of smoke:
Ndipo ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi zizindikiro pa dziko lapansi pano, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
20 The sun shall be turned into darkness, And the moon into blood, Before shall come the day of the Lord, great and fearful;
Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi laulemerero la Ambuye.
21 And every one who shall call the name Of the Lord shall be saved.
Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.’
22 MEN, sons of Israel, hear these words; Jeshu Natsroya, the man who from Aloha appeared with you, with powers and mighty acts, which Aloha wrought among you by his hand, (even) as you know,
“Inu Aisraeli mverani mawu awa; Yesu wa ku Nazareti anali munthu amene anaperekedwa kwa inu ndi Mulungu. Ndipo Mulungu anakutsimikizirani zimenezi ndi zamphamvu, zodabwitsa ndi zizindikiro zimene anachita mwa Iye pakati panu, monga inu mukudziwa.
23 This, who was separated thereunto by the foreknowledge and by the will of Aloha, you delivered into the hands of the wicked, and crucified and slew.
Yesu ameneyu anaperekedwa kwa inu mwa kufuna ndi kudziwiratu kwa Mulungu; ndipo inu mothandizidwa ndi anthu oyipa, munamupha Iye pomupachika pa mtanda.
24 But Aloha raised him, and loosed the bands of Shiul, because it was not possible that he should be holden in Shiul.
Koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa, kumumasula Iye ku zowawa za imfa, chifukwa kunali kosatheka kuti agwiridwe ndi imfa.
25 For David said concerning him, I have foreseen my Lord at all time, Who is at my right hand that I should not be moved;
Pakuti Davide ananena za Iye kuti, “‘Ndinaona Ambuye pamaso panga nthawi zonse. Chifukwa Iye ali kudzanja langa lamanja, Ine sindidzagwedezeka.
26 Wherefore my heart is glad, And my glory rejoiceth: And also my body shall sojourn in hope;
Chifukwa chake mtima wanga ndi wokondwa ndipo lilime langa likukondwera; thupi langanso lidzakhala ndi chiyembekezo.
27 For thou wilt not leave my soul in Shiul, Nor give thy Saint to see corruption. (Hadēs g86)
Chifukwa simudzasiya moyo wanga kumalo a anthu akufa, ku manda, kapena kulekerera Woyerayo kuti awole. (Hadēs g86)
28 Thou wilt reveal to me the way of life, Thou wilt fill me with joy with thy presence.
Inu munandidziwitsa ine njira zamoyo; Inu mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu.’
29 Men, brethren, suffer me to speak openly with you concerning the chief-father David, that he is dead and also buried, and his sepulchre is with us till this day.
“Abale, ine ndikuwuzani motsimikiza kuti kholo lathu Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda, ndipo manda ake alipo lero lino.
30 For he was a prophet, and knew that the oath Aloha had sworn to him, Of the fruit of thy loins I will cause to sit upon thy throne:
Koma iye anali mneneri ndipo anadziwa kuti Mulungu analonjeza ndi lumbiro kuti adzayika mmodzi wa zidzukulu zake pa mpando waufumu.
31 And he foresaw and spake concerning, the resurrection of the Meshiha, that He would not be left in Shiul, nor would his body see corruption. (Hadēs g86)
Davide ataoneratu zimene zinali mʼtsogolo anayankhula za kuuka kwa Khristu, kuti Iye sanasiyidwe mʼmanda, ndipo thupi lake silinawole. (Hadēs g86)
32 This Jeshu hath Aloha raised, and we all are his witnesses.
Mulungu wamuukitsa Yesu ameneyu, ndipo ife ndife mboni za zimenezi.
33 And he it is who at the right hand of Aloha is exalted, and hath received of the Father the promise of the Holy Spirit, and hath shed forth this gift, which, behold, you see and you hear.
Khristu anakwezedwa kukhala kudzanja lamanja la Mulungu, nalandira Mzimu Woyera amene Atate anamulonjeza, ndipo watipatsa ife zimene mukuona ndi kumvazi.
34 For David hath not ascended into heaven, because he himself hath said, The Lord said unto my Lord, Sit thou at my right hand
Pakuti si Davide anakwera kumwamba koma iye akuti, “‘Ambuye anawuza Ambuye anga kuti: Khala kudzanja langa lamanja
35 Until I place thine adversaries the stool of thy feet.
mpaka nditasandutsa adani ako kukhala chopondapo mapazi ako.’
36 Assuredly, then, let all the house of Israel know, that Lord and Meshiha hath Aloha made this Jeshu, whom you crucified.
“Nʼchifukwa chake, Aisraeli onse adziwe ndithu kuti, Yesu amene inu munamupachika, Mulungu wamuyika kukhala Ambuye ndiponso Mpulumutsi.”
37 AND when they heard, they were pierced in their heart, and said to Shemun and to the rest of the apostles, What shall we do, brethren?
Anthu atamva zimenezi, anatsutsika kwambiri mu mtima ndipo anati kwa Petro ndi atumwi enawo, “Abale, kodi ife tichite chiyani?”
38 Shemun saith to them, Repent, and be baptized, every man of you, in the name of the Lord Jeshu, for the remission of sins, and you shall receive the gift of the Holy Spirit.
Petro anawayankha kuti, “Lapani ndipo mubatizidwe aliyense wa inu, mʼdzina la Yesu Khristu kuti machimo anu akhululukidwe. Ndipo mudzalandira mphatso ya Mzimu Woyera.
39 For to you is the promise, and to your children, and to all them who are afar off, whom Aloha himself shall call.
Pakuti lonjezoli ndi lanu ndi ana anu ndiponso la onse amene ali kutali, ndi iwo onse amene Ambuye Mulungu wathu adzawayitane.”
40 And with many other words he testified to them and entreated of them, saying, Save (yourselves) from this perverse generation.
Petro anawachenjeza ndi mawu ena ambiri, ndipo anawadandaulira iwo kuti, “Mudzipulumutse ku mʼbado owonongeka uno.”
41 And some of them eagerly received his word and believed and were baptized, and there were added in that day as three thousand souls.
Iwo amene anawulandira uthenga wake anabatizidwa ndipo tsiku lomwelo miyoyo pafupifupi 3,000 inawonjezedwa ku gulu lawo.
42 And they were faithful in the doctrine of the apostles, and participated in prayer and in the breaking of the eucharist.
Iwo ankasonkhana pamodzi kuphunzitsidwa ndi atumwi, pachiyanjano, pachakudya ndi popemphera.
43 And solemnity was on every soul; and many signs and mighty acts were done by the hand of the apostles in Urishlem.
Aliyense ankachita mantha chifukwa cha zodabwitsa ndi zizindikiro zambiri zimene atumwi ankachita.
44 And all those who believed were together, and every thing they had was in common.
Okhulupirira onse anali pamodzi ndipo aliyense ankapereka zinthu zake kuti zikhale za onse.
45 And they who had property sold it, and divided to each according to that which he needed.
Ankagulitsa minda yawo ndi katundu wawo, ndi kugawira kwa aliyense molingana ndi zosowa zake.
46 And every day they continued in the temple with one soul, and in the house they brake the bread, and took their food rejoicing and in the cleanness of their hearts,
Tsiku ndi tsiku ankasonkhana pamodzi pa bwalo la pa Nyumba ya Mulungu. Ankadya pamodzi mʼnyumba zawo mwasangala ndi mtima woona.
47 praising Aloha, (and) given (to be) in favour before all the people. And our Lord added daily them who were saved into the church.
Ankayamika Mulungu ndipo anthu onse ankawakomera mtima. Ndipo tsiku ndi tsiku Ambuye ankawonjezera ena pa chiwerengero cha olandira chipulumutso.

< Acts 2 >