< Acts 2 >

1 When the day of Pentecost was fully come, and they were all together in the same place,
Litafika tsiku la chikondwerero cha Pentekosite, onse anali pamodzi.
2 there came suddenly from the sky a sound like the onrush of a mighty wind, and it filled all the house where they were sitting.
Mwadzidzidzi kunamveka mkokomo kuchokera kumwamba ngati wa mphepo yamphamvu, ndipo inadzaza nyumba yonse imene amakhala.
3 There appeared to them tongues, like flame, distributing themselves, one resting upon the head of each one,
Iwo anaona zinthu zokhala ngati malilime amoto ogawikana ndipo anakhala pa aliyense wa iwo.
4 and they were all filled with the Holy Spirit, and began to speak with other tongues as the Spirit was giving them utterance.
Ndipo onse anadzazidwa ndi Mzimu Woyera, nayamba kuyankhula mu ziyankhulo zina, monga Mzimu Woyerayo anawayankhulitsa.
5 Now there were, staying in Jerusalem. devout Jews from many and distant lands.
Ayuda woopa Mulungu ochokera ku mayiko onse a dziko lapansi ankakhala mu Yerusalemu nthawi imeneyi.
6 So when this noise was heard, the crowd gathered in bewilderment because each man heard them speaking in his own language.
Utamveka mkokomo uja, gulu la anthu linasonkhana. Anthuwo anadabwa chifukwa aliyense anawamva atumwiwo akuyankhula ziyankhulo zosiyanasiyana.
7 The were beside themselves with wonder. "Are not these Galileans who are speaking?" they exclaimed.
Mothedwa nzeru anafunsana kuti, “Kodi anthu onse amene akuyankhulawa si Agalileya?
8 "Then how is it that each one of us hears them speak his own mother tongue?
Nanga bwanji aliyense wa ife akuwamva iwo mu chinenero cha kwawo?
9 Parthians, Medes, Elamites, dwellers in Mesopotamia, in Judea, in Cappadocia, in Pontus and Asia,
Apanti, Amedi ndi Aelami; okhala ku Mesopotamiya, ku Yudeya ndi ku Kapadokiya, ku Ponto ndi ku Asiya,
10 in Phrygia, Pamphylia, Egypt, and the district of Lybia around Cretans and Arabians,
ku Frugiya ndi Pamfiliya, ku Igupto ndi ku madera a ku Libiya kufupi ndi ku Kurene; alendo ochokera ku Roma,
11 we all hear these men telling in our own tongue what great things God has done."
Ayuda ndi otsatira chipembedzo cha Chiyuda onse pamodzi; Akrete ndi Aarabu, ife tonse tikuwamva akuyankhula za ntchito zodabwitsa za Mulungu mu ziyankhulo zathu.”
12 All were astonished and bewildered and kept saying to one another, "What can this mean?"
Modabwa ndi mothedwa nzeru anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Zimenezi zikutanthauzanji?”
13 But others were saying with jeer, "These men are full of sweet wine."
Koma ena anawaseka nati, “Aledzera vinyo watsopano.”
14 Then Peter, with the Eleven, stood up and addresses them in a loud voice. "Men of Judea and dwellers in Jerusalem, have no doubt about this matter, but listen to what I say.
Koma Petro anayimirira pamodzi ndi atumwi khumi ndi mmodziwo ndipo anakweza mawu ake nayankhula kwa gulu la anthu nati: “Ayuda anzanga, ndi nonse amene muli mu Yerusalemu, mvetsetsani izi ndipo tcherani khutu ku zimene ndikunena.
15 "These men are not drunk, as you suppose, since it is only nine o’clock in the morning.
Kunena zoona, anthu awa sanaledzere ayi, monga momwe mukuganizira, pakuti ino ndi 9 koloko mmawa!
16 "No, this is what the prophet Joel predicted.
Koma izi ndi zimene ananena Mneneri Yoweli kuti:
17 "In the last days, God says, it shall come to pass that I will pour out my Spirit upon all mankind; "Your sons and your daughters shall prophesy, your young men shall see visions, your old men shall dream dreams;
“‘Mulungu akuti, mʼmasiku otsiriza ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi aakazi adzanenera, anyamata anu adzaona masomphenya, nkhalamba zanu zidzalota maloto.
18 upon my slaves, both men and women, in those days, will I pour out my Spirit, and they shall prophesy.
Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo, ndipo iwo adzanenera.
19 In the sky above I will show marvels, And signs in the earth beneath; Blood and fire, and vapor of smoke.
Ndipo ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi zizindikiro pa dziko lapansi pano, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
20 Into darkness shall the sun be turned, And into blood the moon, Ere the day of the Lord come, that great and terrible day.
Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi laulemerero la Ambuye.
21 And every one who calls upon the name of the Lord will be saved.
Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.’
22 "Men of Israel, listen to these words. Jesus the Nazarene, a man accredited to you by God, through mighty works and wonders and signs which God did by him among you, as you yourselves know;
“Inu Aisraeli mverani mawu awa; Yesu wa ku Nazareti anali munthu amene anaperekedwa kwa inu ndi Mulungu. Ndipo Mulungu anakutsimikizirani zimenezi ndi zamphamvu, zodabwitsa ndi zizindikiro zimene anachita mwa Iye pakati panu, monga inu mukudziwa.
23 him, delivered up by the settled purpose and fore-knowledge of God, you crucified and killed at the hands of lawless men;
Yesu ameneyu anaperekedwa kwa inu mwa kufuna ndi kudziwiratu kwa Mulungu; ndipo inu mothandizidwa ndi anthu oyipa, munamupha Iye pomupachika pa mtanda.
24 but God has raised him to life, having loosed the pangs of death, because it was not possible for death to hold him.
Koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa, kumumasula Iye ku zowawa za imfa, chifukwa kunali kosatheka kuti agwiridwe ndi imfa.
25 For David says of him. "I beheld the Lord always before my face; For he is at my right hand lest I be shaken.
Pakuti Davide ananena za Iye kuti, “‘Ndinaona Ambuye pamaso panga nthawi zonse. Chifukwa Iye ali kudzanja langa lamanja, Ine sindidzagwedezeka.
26 "Therefore my heart is glad, my tongue exults, my very body also shall pitch its tent in hope.
Chifukwa chake mtima wanga ndi wokondwa ndipo lilime langa likukondwera; thupi langanso lidzakhala ndi chiyembekezo.
27 "For thou wilt not leave my soul in Hades, Nor give up thy Holy One to see corruption. (Hadēs g86)
Chifukwa simudzasiya moyo wanga kumalo a anthu akufa, ku manda, kapena kulekerera Woyerayo kuti awole. (Hadēs g86)
28 "Thou hast made known to me the paths of life, Thou wilt fill me with gladness in thy presence.
Inu munandidziwitsa ine njira zamoyo; Inu mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu.’
29 "Men and brothers, I can speak plainly to you concerning the patriarch David, because he not only died and was buried, but his tomb is among us even to this very day.
“Abale, ine ndikuwuzani motsimikiza kuti kholo lathu Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda, ndipo manda ake alipo lero lino.
30 "Because he was a prophet and knew that God had sworn to him with an oath that of the fruit of his loins he would set one on his throne,
Koma iye anali mneneri ndipo anadziwa kuti Mulungu analonjeza ndi lumbiro kuti adzayika mmodzi wa zidzukulu zake pa mpando waufumu.
31 "he, foreseeing this, spoke of the resurrection of Christ that neither was he left in Hades, nor did his flesh see corruption. (Hadēs g86)
Davide ataoneratu zimene zinali mʼtsogolo anayankhula za kuuka kwa Khristu, kuti Iye sanasiyidwe mʼmanda, ndipo thupi lake silinawole. (Hadēs g86)
32 This Jesus God has raised up, of this we are all witnesses.
Mulungu wamuukitsa Yesu ameneyu, ndipo ife ndife mboni za zimenezi.
33 Since he is by the mighty hand of God exalted, and has received from his Father the promise of the Holy Spirit, he has poured forth this which you now see and hear.
Khristu anakwezedwa kukhala kudzanja lamanja la Mulungu, nalandira Mzimu Woyera amene Atate anamulonjeza, ndipo watipatsa ife zimene mukuona ndi kumvazi.
34 For David did not ascend into heaven; but he himself said, "The Lord said to my Lord Sit thou on my right hand
Pakuti si Davide anakwera kumwamba koma iye akuti, “‘Ambuye anawuza Ambuye anga kuti: Khala kudzanja langa lamanja
35 "Until I make thine enemies A footstool under thy feet.
mpaka nditasandutsa adani ako kukhala chopondapo mapazi ako.’
36 "Therefore let the whole House of Israel know assuredly that Gods has made him both Lord and Christ, this Jesus whom you have crucified."
“Nʼchifukwa chake, Aisraeli onse adziwe ndithu kuti, Yesu amene inu munamupachika, Mulungu wamuyika kukhala Ambuye ndiponso Mpulumutsi.”
37 When they heard these words they were stung to the heart, and said to Peter and the rest of the apostles. "Men and brothers, what shall we do?"
Anthu atamva zimenezi, anatsutsika kwambiri mu mtima ndipo anati kwa Petro ndi atumwi enawo, “Abale, kodi ife tichite chiyani?”
38 "Repent," answered Peter, "and be baptized, every one of you, in the name of Jesus Christ, for the remission of your sins, and you shall receive the gift of the Holy Spirit.
Petro anawayankha kuti, “Lapani ndipo mubatizidwe aliyense wa inu, mʼdzina la Yesu Khristu kuti machimo anu akhululukidwe. Ndipo mudzalandira mphatso ya Mzimu Woyera.
39 "For the promise belongs to you and to your children and to all who are afar off, whomever the Lord may call."
Pakuti lonjezoli ndi lanu ndi ana anu ndiponso la onse amene ali kutali, ndi iwo onse amene Ambuye Mulungu wathu adzawayitane.”
40 With many other words he continued to bear testimony, and kept entreating them, saying, "Save yourselves from this perverse generation."
Petro anawachenjeza ndi mawu ena ambiri, ndipo anawadandaulira iwo kuti, “Mudzipulumutse ku mʼbado owonongeka uno.”
41 Then those who welcomed his message were baptized, and in that day about three thousand souls were added to them;
Iwo amene anawulandira uthenga wake anabatizidwa ndipo tsiku lomwelo miyoyo pafupifupi 3,000 inawonjezedwa ku gulu lawo.
42 and they stedfastly continued in the teaching of the apostles, and in the fellowship, in the breaking of the bread, and in the prayers.
Iwo ankasonkhana pamodzi kuphunzitsidwa ndi atumwi, pachiyanjano, pachakudya ndi popemphera.
43 And awe came upon every soul, and many wonders and signs were wrought by the apostles.
Aliyense ankachita mantha chifukwa cha zodabwitsa ndi zizindikiro zambiri zimene atumwi ankachita.
44 And all the believers were together, and had all things in common.
Okhulupirira onse anali pamodzi ndipo aliyense ankapereka zinthu zake kuti zikhale za onse.
45 They would sell their lands and other property, and distribute the proceeds among all, just as any one from time had need.
Ankagulitsa minda yawo ndi katundu wawo, ndi kugawira kwa aliyense molingana ndi zosowa zake.
46 Day after day they continued stedfastly with one accord in the Temple; and breaking bread together in their own homes, they continued to eat their food with gladness and an undivided heart,
Tsiku ndi tsiku ankasonkhana pamodzi pa bwalo la pa Nyumba ya Mulungu. Ankadya pamodzi mʼnyumba zawo mwasangala ndi mtima woona.
47 praising God, and looked on with favor by all the people. Meanwhile the Lord kept adding to them daily those that were being saved.
Ankayamika Mulungu ndipo anthu onse ankawakomera mtima. Ndipo tsiku ndi tsiku Ambuye ankawonjezera ena pa chiwerengero cha olandira chipulumutso.

< Acts 2 >