< 1 Corinthians 3 >

1 And I, brothers, could not speak to you as to spiritual, but as to carnal, even as to babes in Christ.
Ndipo abale sindikanakuyankhulani ngati auzimu koma adziko lapansi, makanda chabe mwa Khristu.
2 I have fed you with milk, and not with meat: for till now you were not able to bear it, neither yet now are you able.
Ndinakupatsani mkaka osati chakudya cholimba pakuti munali musanakonzeke kuchilandira. Zoonadi, simunakonzekebe.
3 For you are yet carnal: for whereas there is among you envying, and strife, and divisions, are you not carnal, and walk as men?
Mukanali adziko lapansi. Pakuti pakati panu pali kaduka ndi kukangana, kodi si inu a dziko lapansi? Kodi simukuchita ngati anthu wamba?
4 For while one says, I am of Paul; and another, I am of Apollos; are you not carnal?
Pamene wina anena kuti, “Ine ndimatsatira Paulo,” ndipo wina akuti, “Ine ndimatsatira Apolo,” Kodi si inu akunja?
5 Who then is Paul, and who is Apollos, but ministers by whom you believed, even as the Lord gave to every man?
Ndiponso kodi Apolo ndi ndani? Nanga Paulo ndi ndani? Otumikira chabe, omwe kudzera mwa iwo inu munakhulupirira monga Ambuye anawagawira aliyense ntchito yake.
6 I have planted, Apollos watered; but God gave the increase.
Ine ndinadzala mbewu, Apolo anayithirira, koma Mulungu ndiye anayikulitsa.
7 So then neither is he that plants any thing, neither he that waters; but God that gives the increase.
Choncho kuphatikiza iye wodzala ndi iye wothirira, onse sali kanthu, koma Mulungu yekha amene amakulitsa zinthu.
8 Now he that plants and he that waters are one: and every man shall receive his own reward according to his own labor.
Munthu wodzala ndi munthu wothirira ali ndi cholinga chimodzi, ndipo aliyense adzapatsidwa mphotho molingana ndi ntchito yake.
9 For we are laborers together with God: you are God’s husbandry, you are God’s building.
Pakuti ife ndife antchito anzake a Mulungu; inu ndinu munda wa Mulungu, Nyumba ya Mulungu.
10 According to the grace of God which is given to me, as a wise master builder, I have laid the foundation, and another builds thereon. But let every man take heed how he builds thereupon.
Mwachisomo chimene Mulungu wandipatsa, ine ndinayika maziko monga mmisiri waluntha, ndipo ena akumangapo. Koma aliyense ayenera kuchenjera mmene akumangira.
11 For other foundation can no man lay than that is laid, which is Jesus Christ.
Pakuti wina sangayikenso maziko ena oposera amene anakhazikitsidwa kale, amene ndi Yesu Khristu.
12 Now if any man build on this foundation gold, silver, precious stones, wood, hay, stubble;
Ngati munthu aliyense amanga pa maziko awa pogwiritsa ntchito golide, siliva, miyala yamtengowapatali, milimo yamitengo, tsekera kapena udzu,
13 Every man’s work shall be made manifest: for the day shall declare it, because it shall be revealed by fire; and the fire shall try every man’s work of what sort it is.
ntchito yake idzaonekera pamene Tsiku la chiweruzo lidzazionetsa poyera. Tsikulo lidzafika ndi moto, ndipo motowo ndi umene udzayesa ntchito ya munthu aliyense.
14 If any man’s work abide which he has built thereupon, he shall receive a reward.
Ngati zimene zamangidwazo sizidzagwa, adzalandira mphotho yake.
15 If any man’s work shall be burned, he shall suffer loss: but he himself shall be saved; yet so as by fire.
Ndipo ngati zidzanyeke ndi moto, sadzalandira mphotho koma iye mwini adzapulumukabe, koma monga ngati munthu amene wapulumuka mʼmoto.
16 Know you not that you are the temple of God, and that the Spirit of God dwells in you?
Kodi inu simukudziwa kuti ndinu Nyumba ya Mulungu ndipo kuti Mzimu wa Mulungu amakhala mwa inu?
17 If any man defile the temple of God, him shall God destroy; for the temple of God is holy, which temple you are.
Ngati wina aliyense awononga Nyumba ya Mulunguyo, Mulungu nayenso adzamuwononga ameneyo; popeza Nyumba ya Mulungu ndi yopatulika ndipo Nyumbayo ndi inu amene.
18 Let no man deceive himself. If any man among you seems to be wise in this world, let him become a fool, that he may be wise. (aiōn g165)
Choncho musadzinyenge. Ngati wina wa inu akuganiza kuti ndi wanzeru pa mulingo wa mʼbado uno, ayenera kukhala “wopusa” kuti athe kukhala wanzeru. (aiōn g165)
19 For the wisdom of this world is foolishness with God. For it is written, He takes the wise in their own craftiness.
Pakuti nzeru ya dziko lapansi ndi yopusa pamaso pa Mulungu. Monga kwalembedwera kuti, “Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,”
20 And again, The Lord knows the thoughts of the wise, that they are vain.
ndiponso, “Ambuye amadziwa kuti maganizo a wanzeru ndi opandapake.”
21 Therefore let no man glory in men. For all things are yours;
Choncho, wina asanyadire anthu chabe! Zonse ndi zanu,
22 Whether Paul, or Apollos, or Cephas, or the world, or life, or death, or things present, or things to come; all are yours;
kaya Paulo kapena Apolo kapena Kefa kapena dziko lapansi, kapena moyo, kapena imfa, kapena tsopano, kapena mʼtsogolo, zonse ndi zanu,
23 And you are Christ’s; and Christ is God’s.
ndipo inu ndinu a Khristu, ndipo Khristu ndi wa Mulungu.

< 1 Corinthians 3 >