< 1 Chronicles 2 >

1 These are the sons of Israel; Reuben, Simeon, Levi, and Judah, Issachar, and Zebulun,
Ana a Israeli anali awa: Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Zebuloni,
2 Dan, Joseph, and Benjamin, Naphtali, Gad, and Asher.
Dani, Yosefe, Benjamini, Nafutali, Gadi ndi Aseri.
3 The sons of Judah; Er, and Onan, and Shelah: which three were born to him of the daughter of Shua the Canaanitess. And Er, the firstborn of Judah, was evil in the sight of the LORD; and he slew him.
Ana a Yuda anali awa: Eri, Onani ndi Sela. Ana atatu awa anabereka ndi mkazi wa Chikanaani, Batisuwa. Eri, mwana woyamba wa Yuda anali woyipa kwambiri pamaso pa Yehova, kotero Yehova anamupha.
4 And Tamar his daughter in law bore him Pharez and Zerah. All the sons of Judah were five.
Mpongozi wake Tamara anamuberekera Perezi ndi Zera. Ana onse a Yuda analipo asanu.
5 The sons of Pharez; Hezron, and Hamul.
Ana a Perezi anali awa: Hezironi ndi Hamuli.
6 And the sons of Zerah; Zimri, and Ethan, and Heman, and Calcol, and Dara: five of them in all.
Ana a Zera anali awa: Zimuri, Etani, Hemani, Kalikoli ndi Dara. Onse analipo asanu.
7 And the sons of Carmi; Achar, the troubler of Israel, who transgressed in the thing accursed.
Mwana wa Karimi anali Akani, amene anabweretsa mavuto pakati pa Israeli pamene anatenga zinthu zoyenera kuwonongedwa.
8 And the sons of Ethan; Azariah.
Mwana wa Etani anali Azariya.
9 The sons also of Hezron, that were born to him; Jerahmeel, and Ram, and Chelubai.
Ana amene anabadwa kwa Hezironi anali: Yerahimeeli, Ramu ndi Kelubai.
10 And Ram begat Amminadab; and Amminadab begat Nahshon, prince of the children of Judah;
Ramu anabereka Aminadabu ndipo Aminadabu anali abambo ake a Naasoni, mtsogoleri wa fuko la Yuda.
11 And Nahshon begat Salma, and Salma begat Boaz,
Naasoni anabereka Salima, Salima anabereka Bowazi,
12 And Boaz begat Obed, and Obed begat Jesse,
Bowazi anabereka Obedi ndipo Obedi anabereka Yese.
13 And Jesse begat his firstborn Eliab, and Abinadab the second, and Shimma the third,
Yese anabereka Eliabu mwana wake woyamba, wachiwiri Abinadabu, wachitatu Simea,
14 Nethaneel the fourth, Raddai the fifth,
wachinayi Netaneli, wachisanu Radai,
15 Ozem the sixth, David the seventh:
wachisanu ndi chimodzi Ozemu ndi wachisanu ndi chiwiri Davide.
16 Whose sisters were Zeruiah, and Abigail. And the sons of Zeruiah; Abishai, and Joab, and Asahel, three.
Alongo awo anali Zeruya ndi Abigayeli. Ana atatu a Zeruya anali Abisai Yowabu ndi Asaheli.
17 And Abigail bore Amasa: and the father of Amasa was Jether the Ishmeelite.
Abigayeli anali amayi ake a Amasa amene abambo ake anali Yeteri wa fuko la Ismaeli.
18 And Caleb the son of Hezron begat children of Azubah his wife, and of Jerioth: her sons are these; Jesher, and Shobab, and Ardon.
Kalebe mwana wa Hezironi anabereka ana mwa Azuba mkazi wake (ndi mwa Yerioti). Ana a mkaziyo anali awa: Yeseri, Sobabu ndi Aridoni.
19 And when Azubah was dead, Caleb took to him Ephrath, which bore him Hur.
Azuba atamwalira, Kalebe anakwatira Efurata, amene anamuberekera Huri.
20 And Hur begat Uri, and Uri begat Bezaleel.
Huri anabereka Uri ndipo Uri anabereka Bezaleli.
21 And afterward Hezron went in to the daughter of Machir the father of Gilead, whom he married when he was three score years old; and she bore him Segub.
Patapita nthawi, Hezironi anagona ndi mwana wamkazi wa Makiri abambo ake a Giliyadi (iye anamukwatira ali ndi zaka 60) ndipo anamuberekera Segubu.
22 And Segub begat Jair, who had three and twenty cities in the land of Gilead.
Segubu anabereka Yairi, amene anali ndi mizinda 23 ku Giliyadi.
23 And he took Geshur, and Aram, with the towns of Jair, from them, with Kenath, and the towns thereof, even three score cities. All these belonged to the sons of Machir the father of Gilead.
(Koma Gesuri ndi Aramu analanda Havoti Yairi komanso Kenati ndi madera ake onse ozungulira, mizinda makumi asanu ndi umodzi). Onsewa anali adzukulu, a Makiri abambo ake a Giliyadi.
24 And after that Hezron was dead in Calebephratah, then Abiah Hezron’s wife bore him Ashur the father of Tekoa.
Atamwalira Hezironi ku Kalebe Efurata, Abiya mkazi wa Hezironi anamuberekera Asihuri abambo a Tekowa.
25 And the sons of Jerahmeel the firstborn of Hezron were, Ram the firstborn, and Bunah, and Oren, and Ozem, and Ahijah.
Ana a Yerahimeeli, mwana woyamba wa Hezironi anali: Ramu, mwana wake woyamba, Buna, Oreni, Ozemu ndi Ahiya.
26 Jerahmeel had also another wife, whose name was Atarah; she was the mother of Onam.
Yerahimeeli anali ndi mkazi wina amene dzina lake linali Atara, amene anali amayi a Onamu.
27 And the sons of Ram the firstborn of Jerahmeel were, Maaz, and Jamin, and Eker.
Ana a Ramu, mwana woyamba wa Yerahimeeli, anali awa: Maazi, Yamini ndi Ekeri.
28 And the sons of Onam were, Shammai, and Jada. And the sons of Shammai; Nadab and Abishur.
Ana a Onamu anali awa: Shamai ndi Yada. Ana a Shamai anali awa: Nadabu ndi Abisuri.
29 And the name of the wife of Abishur was Abihail, and she bore him Ahban, and Molid.
Mkazi wa Abisuri anali Abihaili, amene anamuberekera Ahibani ndi Molidi.
30 And the sons of Nadab; Seled, and Appaim: but Seled died without children.
Ana a Nadabu anali awa: Seledi ndi Apaimu. Koma Seledi anamwalira wopanda ana.
31 And the sons of Appaim; Ishi. And the sons of Ishi; Sheshan. And the children of Sheshan; Ahlai.
Ana a Apaimu anali awa: Isi, amene anabereka Sesani. Sesani anabereka Ahilai.
32 And the sons of Jada the brother of Shammai; Jether, and Jonathan: and Jether died without children.
Ana a Yada, mʼbale wa Samai, anali awa: Yereri ndi Yonatani. Koma Yeteri anamwalira wopanda ana.
33 And the sons of Jonathan; Peleth, and Zaza. These were the sons of Jerahmeel.
Ana a Yonatani anali awa: Peleti ndi Zaza. Amenewa anali adzukulu a Yerahimeeli.
34 Now Sheshan had no sons, but daughters. And Sheshan had a servant, an Egyptian, whose name was Jarha.
Sesani sanabereke ana aamuna koma aakazi okhaokha. Iye anali ndi wantchito wa ku Igupto, dzina lake Yariha.
35 And Sheshan gave his daughter to Jarha his servant to wife; and she bore him Attai.
Sesani anapereka mwana wake wamkazi kwa Yariha wantchito wake kuti amukwatire ndipo anamuberekera Atayi.
36 And Attai begat Nathan, and Nathan begat Zabad,
Atayi anali abambo ake a Natani, Natani anali abambo ake a Zabadi,
37 And Zabad begat Ephlal, and Ephlal begat Obed,
Zabadi anali abambo a Efilali, Efilali anali abambo a Obedi,
38 And Obed begat Jehu, and Jehu begat Azariah,
Obedi anali abambo a Yehu, Yehu anali abambo a Azariya,
39 And Azariah begat Helez, and Helez begat Eleasah,
Azariya anali abambo a Helezi, Helezi anali abambo a Eleasa,
40 And Eleasah begat Sisamai, and Sisamai begat Shallum,
Eleasa anali abambo ake a Sisimai, Sisimai anali abambo a Salumu,
41 And Shallum begat Jekamiah, and Jekamiah begat Elishama.
Salumu anali abambo a Yekamiya, Yekamiya anali abambo a Elisama.
42 Now the sons of Caleb the brother of Jerahmeel were, Mesha his firstborn, which was the father of Ziph; and the sons of Mareshah the father of Hebron.
Ana a Kalebe mʼbale wa Yerahimeeli anali awa: Mesa mwana wachisamba, anali abambo a Zifi, ndipo mwana wake Maresa anali abambo a Hebroni.
43 And the sons of Hebron; Korah, and Tappuah, and Rekem, and Shema.
Ana a Hebroni anali awa: Kora, Tapuwa, Rekemu ndi Sema.
44 And Shema begat Raham, the father of Jorkoam: and Rekem begat Shammai.
Sema anali abambo ake Rahamu ndipo Rahamu anali abambo a Yorikeamu. Rekemu anali abambo a Samai.
45 And the son of Shammai was Maon: and Maon was the father of Bethzur.
Mwana wa Samai anali Maoni, ndipo Maoni anali abambo a Beti Zuri.
46 And Ephah, Caleb’s concubine, bore Haran, and Moza, and Gazez: and Haran begat Gazez.
Efai, mzikazi wa Kalebe, anali amayi a Harani, Moza ndi Gazezi. Harani anali abambo a Gazezi.
47 And the sons of Jahdai; Regem, and Jotham, and Gesham, and Pelet, and Ephah, and Shaaph.
Ana a Yahidai anali awa: Regemu, Yotamu, Gesani, Peleti, Efai ndi Saafi.
48 Maachah, Caleb’s concubine, bore Sheber, and Tirhanah.
Maaka mzikazi wa Kalebe anali mayi Seberi ndi Tirihana.
49 She bore also Shaaph the father of Madmannah, Sheva the father of Machbenah, and the father of Gibea: and the daughter of Caleb was Achsa.
Iye anaberekanso Saafi abambo a Madimena ndi Seva abambo a Makibena ndi Gibeya. Mwana wamkazi wa Kalebe anali Akisa.
50 These were the sons of Caleb the son of Hur, the firstborn of Ephratah; Shobal the father of Kirjathjearim.
Izi zinali zidzukulu za Kalebe. Ana a Huri mwana wachisamba wa Efurata anali awa: Sobala abambo a Kiriati Yearimu,
51 Salma the father of Bethlehem, Hareph the father of Bethgader.
Salima abambo a Betelehemu ndi Harefu abambo ake a Beti-Gadera.
52 And Shobal the father of Kirjathjearim had sons; Haroeh, and half of the Manahethites.
Zidzukulu za Sobala abambo a Kiriati Yearimu zinali izi: Harowe, theka la banja la Manahati,
53 And the families of Kirjathjearim; the Ithrites, and the Puhites, and the Shumathites, and the Mishraites; of them came the Zareathites, and the Eshtaulites,
ndipo mabanja a Kiriati-Yeyarimu anali awa: Aitiri, Aputi, Asumati ndi Amisirai. Azorati ndi Aesitaoli anachokera kwa amenewa.
54 The sons of Salma; Bethlehem, and the Netophathites, Ataroth, the house of Joab, and half of the Manahethites, the Zorites.
Zidzukulu za Salima zinali izi: Betelehemu, Anetofati, Atiroti-Beti-Yowabu, theka la banja la Manahati, Azori,
55 And the families of the scribes which dwelled at Jabez; the Tirathites, the Shimeathites, and Suchathites. These are the Kenites that came of Hemath, the father of the house of Rechab.
ndiponso mabanja a alembi amene amakhala ku Yabesi: Atiroti, Asimeati ndiponso Asukati. Awa ndi Akeni amene anachokera kwa Hamati, kholo la Arekabu.

< 1 Chronicles 2 >