< Psalms 141 >

1 A Psalm of David. LORD, I have called Thee; make haste unto me; give ear unto my voice, when I call unto Thee.
Salimo la Davide. Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine. Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu.
2 Let my prayer be set forth as incense before Thee, the lifting up of my hands as the evening sacrifice.
Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani; kukweza manja kwanga kukhale ngati nsembe yamadzulo.
3 Set a guard, O LORD, to my mouth; keep watch at the door of my lips.
Yehova ikani mlonda pakamwa panga; londerani khomo la pa milomo yanga.
4 Incline not my heart to any evil thing, to be occupied in deeds of wickedness with men that work iniquity; and let me not eat of their dainties.
Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa; kuchita ntchito zonyansa pamodzi ndi anthu amene amachita zoyipa; musalole kuti ndidye nawo zokoma zawo.
5 Let the righteous smite me in kindness, and correct me; oil so choice let not my head refuse; for still is my prayer because of their wickedness.
Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo; andidzudzule ndiye mafuta pa mutu wanga. Mutu wanga sudzakana zimenezi. Komabe pemphero langa nthawi zonse ndi lotsutsana ndi ntchito za anthu ochita zoyipa.
6 Their judges are thrown down by the sides of the rock; and they shall hear my words, that they are sweet.
Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri, ndipo anthu oyipa adzaphunzira kuti mawu anga anayankhulidwa bwino.
7 As when one cleaveth and breaketh up the earth, our bones are scattered at the grave's mouth. (Sheol h7585)
Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza, ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.” (Sheol h7585)
8 For mine eyes are unto Thee, O GOD the Lord; in Thee have I taken refuge, O pour not out my soul.
Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse; ndimathawira kwa Inu, musandipereke ku imfa.
9 Keep me from the snare which they have laid for me, and from the gins of the workers of iniquity.
Mundipulumutse ku misampha imene anditchera, ku makhwekhwe amene anthu oyipa andikonzera.
10 Let the wicked fall into their own nets, whilst I withal escape.
Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo, mpaka ine nditadutsa mwamtendere.

< Psalms 141 >