< 1 Corinthians 3 >

1 And I could not speake vnto you, brethren, as vnto spirituall men, but as vnto carnall, euen as vnto babes in Christ.
Ndipo abale sindikanakuyankhulani ngati auzimu koma adziko lapansi, makanda chabe mwa Khristu.
2 I gaue you milke to drinke, and not meat: for yee were not yet able to beare it, neither yet nowe are yee able.
Ndinakupatsani mkaka osati chakudya cholimba pakuti munali musanakonzeke kuchilandira. Zoonadi, simunakonzekebe.
3 For yee are yet carnall: for whereas there is among you enuying, and strife, and diuisions, are ye not carnall, and walke as men?
Mukanali adziko lapansi. Pakuti pakati panu pali kaduka ndi kukangana, kodi si inu a dziko lapansi? Kodi simukuchita ngati anthu wamba?
4 For when one sayeth, I am Pauls, and another, I am Apollos, are yee not carnall?
Pamene wina anena kuti, “Ine ndimatsatira Paulo,” ndipo wina akuti, “Ine ndimatsatira Apolo,” Kodi si inu akunja?
5 Who is Paul then? and who is Apollos, but the ministers by whome yee beleeued, and as the Lord gaue to euery man?
Ndiponso kodi Apolo ndi ndani? Nanga Paulo ndi ndani? Otumikira chabe, omwe kudzera mwa iwo inu munakhulupirira monga Ambuye anawagawira aliyense ntchito yake.
6 I haue planted, Apollos watred, but God gaue the increase.
Ine ndinadzala mbewu, Apolo anayithirira, koma Mulungu ndiye anayikulitsa.
7 So then, neither is hee that planteth any thing, neither hee that watreth, but God that giueth the increase.
Choncho kuphatikiza iye wodzala ndi iye wothirira, onse sali kanthu, koma Mulungu yekha amene amakulitsa zinthu.
8 And he that planteth, and he that watreth, are one, and euery man shall receiue his wages, according to his labour.
Munthu wodzala ndi munthu wothirira ali ndi cholinga chimodzi, ndipo aliyense adzapatsidwa mphotho molingana ndi ntchito yake.
9 For we together are Gods labourers: yee are Gods husbandrie, and Gods building.
Pakuti ife ndife antchito anzake a Mulungu; inu ndinu munda wa Mulungu, Nyumba ya Mulungu.
10 According to the grace of God giuen to mee, as a skilfull master builder, I haue laide the foundation, and another buildeth thereon: but let euery man take heede how he buildeth vpon it.
Mwachisomo chimene Mulungu wandipatsa, ine ndinayika maziko monga mmisiri waluntha, ndipo ena akumangapo. Koma aliyense ayenera kuchenjera mmene akumangira.
11 For other foundation can no man laie, then that which is laied, which is Iesus Christ.
Pakuti wina sangayikenso maziko ena oposera amene anakhazikitsidwa kale, amene ndi Yesu Khristu.
12 And if any man builde on this foundation, golde, siluer, precious stones, timber, haye, or stubble,
Ngati munthu aliyense amanga pa maziko awa pogwiritsa ntchito golide, siliva, miyala yamtengowapatali, milimo yamitengo, tsekera kapena udzu,
13 Euery mans worke shalbe made manifest: for the day shall declare it, because it shalbe reueiled by the fire: and the fire shall trie euery mans worke of what sort it is.
ntchito yake idzaonekera pamene Tsiku la chiweruzo lidzazionetsa poyera. Tsikulo lidzafika ndi moto, ndipo motowo ndi umene udzayesa ntchito ya munthu aliyense.
14 If any mans worke, that he hath built vpon, abide, he shall receiue wages.
Ngati zimene zamangidwazo sizidzagwa, adzalandira mphotho yake.
15 If any mans worke burne, he shall lose, but he shalbe saued himselfe: neuerthelesse yet as it were by the fire.
Ndipo ngati zidzanyeke ndi moto, sadzalandira mphotho koma iye mwini adzapulumukabe, koma monga ngati munthu amene wapulumuka mʼmoto.
16 Knowe ye not that ye are the Temple of God, and that the Spirit of God dwelleth in you?
Kodi inu simukudziwa kuti ndinu Nyumba ya Mulungu ndipo kuti Mzimu wa Mulungu amakhala mwa inu?
17 If any man destroy the Temple of God, him shall God destroy: for the Temple of God is holy, which ye are.
Ngati wina aliyense awononga Nyumba ya Mulunguyo, Mulungu nayenso adzamuwononga ameneyo; popeza Nyumba ya Mulungu ndi yopatulika ndipo Nyumbayo ndi inu amene.
18 Let no man deceiue himselfe: If any man among you seeme to be wise in this world, let him be a foole, that he may be wise. (aiōn g165)
Choncho musadzinyenge. Ngati wina wa inu akuganiza kuti ndi wanzeru pa mulingo wa mʼbado uno, ayenera kukhala “wopusa” kuti athe kukhala wanzeru. (aiōn g165)
19 For the wisdome of this worlde is foolishnesse with God: for it is written, He catcheth the wise in their owne craftinesse.
Pakuti nzeru ya dziko lapansi ndi yopusa pamaso pa Mulungu. Monga kwalembedwera kuti, “Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,”
20 And againe, The Lord knoweth that the thoughtes of the wise be vaine.
ndiponso, “Ambuye amadziwa kuti maganizo a wanzeru ndi opandapake.”
21 Therefore let no man reioyce in men: for all things are yours.
Choncho, wina asanyadire anthu chabe! Zonse ndi zanu,
22 Whether it be Paul, or Apollos, or Cephas, or the world, or life, or death: whether they be things present, or thinges to come, euen all are yours,
kaya Paulo kapena Apolo kapena Kefa kapena dziko lapansi, kapena moyo, kapena imfa, kapena tsopano, kapena mʼtsogolo, zonse ndi zanu,
23 And ye Christes, and Christ Gods.
ndipo inu ndinu a Khristu, ndipo Khristu ndi wa Mulungu.

< 1 Corinthians 3 >