< Psalms 38 >

1 A psalm for David, for a remembrance of the sabbath. Rebuke me not, O Lord, in thy indignation; nor chastise me in thy wrath.
Salimo la Davide. Kupempha. Yehova musandidzudzule mutapsa mtima kapena kundilanga muli ndi ukali.
2 For thy arrows are fastened in me: and thy hand hath been strong upon me.
Pakuti mivi yanu yandilasa, ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.
3 There is no health in my flesh, because of thy wrath: there is no peace for my bones, because of my sins.
Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa; mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.
4 For my iniquities are gone over my head: and as a heavy burden are become heavy upon me.
Kulakwa kwanga kwandipsinja ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.
5 My sores are putrified and corrupted, because of my foolishness.
Mabala anga akuwola ndipo akununkha chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.
6 I am become miserable, and am bowed down even to the end: I walked sorrowful all the day long.
Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri; tsiku lonse ndimangolira.
7 For my loins are filled with illusions; and there is no health in my flesh.
Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika, mulibe thanzi mʼthupi langa.
8 I am afflicted and humbled exceedingly: I roared with the groaning of my heart.
Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu; ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.
9 Lord, all my desire is before thee, and my groaning is not hidden from thee.
Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye, kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.
10 My heart is troubled, my strength hath left me, and the light of my eyes itself is not with me.
Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha; ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.
11 My friends and my neighbours have drawn near, and stood against me. And they that were near me stood afar off:
Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga; anansi anga akhala kutali nane.
12 And they that sought my soul used violence. And they that sought evils to me spoke vain things, and studied deceits all the day long.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo, oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga; tsiku lonse amakonza zachinyengo.
13 But I, as a deaf man, heard not: and as a dumb man not opening his mouth.
Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve, monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;
14 And I became as a man that heareth not: and that hath no reproofs in his mouth.
Ndakhala ngati munthu amene samva, amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.
15 For in thee, O Lord, have I hoped: thou wilt hear me, O Lord my God.
Ndikudikira Inu Yehova; mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.
16 For I said: Lest at any time my enemies rejoice over me: and whilst my feet are moved, they speak great things against me.
Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”
17 For I am ready for scourges: and my sorrow is continually before me.
Pakuti ndili pafupi kugwa, ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.
18 For I will declare my inequity: and I will think for my sin.
Ndikuvomereza mphulupulu zanga; ndipo ndavutika ndi tchimo langa.
19 But my enemies live, and are stronger that I: and they hate me wrongfully are multiplied.
Ambiri ndi adani anga amphamvu; amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.
20 They that render evil for good, have detracted me, because I followed goodness.
Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino amandinyoza pamene nditsatira zabwino.
21 Forsake me not, O Lord my God: do not thou depart from me.
Inu Yehova, musanditaye; musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.
22 Attend unto my help, O Lord, the God of my salvation.
Bwerani msanga kudzandithandiza, Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.

< Psalms 38 >