< 1 Corinthians 3 >

1 And I, brethren, have not been able to speak to you as to spiritual, but as to fleshly; as to babes in Christ.
Ndipo abale sindikanakuyankhulani ngati auzimu koma adziko lapansi, makanda chabe mwa Khristu.
2 I have given you milk to drink, not meat, for ye have not yet been able, nor indeed are ye yet able;
Ndinakupatsani mkaka osati chakudya cholimba pakuti munali musanakonzeke kuchilandira. Zoonadi, simunakonzekebe.
3 for ye are yet carnal. For whereas [there are] among you emulation and strife, are ye not carnal, and walk according to man?
Mukanali adziko lapansi. Pakuti pakati panu pali kaduka ndi kukangana, kodi si inu a dziko lapansi? Kodi simukuchita ngati anthu wamba?
4 For when one says, I am of Paul, and another, I of Apollos, are ye not men?
Pamene wina anena kuti, “Ine ndimatsatira Paulo,” ndipo wina akuti, “Ine ndimatsatira Apolo,” Kodi si inu akunja?
5 Who then is Apollos, and who Paul? Ministering servants, through whom ye have believed, and as the Lord has given to each.
Ndiponso kodi Apolo ndi ndani? Nanga Paulo ndi ndani? Otumikira chabe, omwe kudzera mwa iwo inu munakhulupirira monga Ambuye anawagawira aliyense ntchito yake.
6 I have planted; Apollos watered; but God has given the increase.
Ine ndinadzala mbewu, Apolo anayithirira, koma Mulungu ndiye anayikulitsa.
7 So that neither the planter is anything, nor the waterer; but God the giver of the increase.
Choncho kuphatikiza iye wodzala ndi iye wothirira, onse sali kanthu, koma Mulungu yekha amene amakulitsa zinthu.
8 But the planter and the waterer are one; but each shall receive his own reward according to his own labour.
Munthu wodzala ndi munthu wothirira ali ndi cholinga chimodzi, ndipo aliyense adzapatsidwa mphotho molingana ndi ntchito yake.
9 For we are God's fellow-workmen; ye are God's husbandry, God's building.
Pakuti ife ndife antchito anzake a Mulungu; inu ndinu munda wa Mulungu, Nyumba ya Mulungu.
10 According to the grace of God which has been given to me, as a wise architect, I have laid the foundation, but another builds upon it. But let each see how he builds upon it.
Mwachisomo chimene Mulungu wandipatsa, ine ndinayika maziko monga mmisiri waluntha, ndipo ena akumangapo. Koma aliyense ayenera kuchenjera mmene akumangira.
11 For other foundation can no man lay besides that which [is] laid, which is Jesus Christ.
Pakuti wina sangayikenso maziko ena oposera amene anakhazikitsidwa kale, amene ndi Yesu Khristu.
12 Now if any one build upon [this] foundation, gold, silver, precious stones, wood, grass, straw,
Ngati munthu aliyense amanga pa maziko awa pogwiritsa ntchito golide, siliva, miyala yamtengowapatali, milimo yamitengo, tsekera kapena udzu,
13 the work of each shall be made manifest; for the day shall declare [it], because it is revealed in fire; and the fire shall try the work of each what it is.
ntchito yake idzaonekera pamene Tsiku la chiweruzo lidzazionetsa poyera. Tsikulo lidzafika ndi moto, ndipo motowo ndi umene udzayesa ntchito ya munthu aliyense.
14 If the work of any one which he has built upon [the foundation] shall abide, he shall receive a reward.
Ngati zimene zamangidwazo sizidzagwa, adzalandira mphotho yake.
15 If the work of any one shall be consumed, he shall suffer loss, but he shall be saved, but so as through [the] fire.
Ndipo ngati zidzanyeke ndi moto, sadzalandira mphotho koma iye mwini adzapulumukabe, koma monga ngati munthu amene wapulumuka mʼmoto.
16 Do ye not know that ye are [the] temple of God, and [that] the Spirit of God dwells in you?
Kodi inu simukudziwa kuti ndinu Nyumba ya Mulungu ndipo kuti Mzimu wa Mulungu amakhala mwa inu?
17 If any one corrupt the temple of God, him shall God destroy; for the temple of God is holy, and such are ye.
Ngati wina aliyense awononga Nyumba ya Mulunguyo, Mulungu nayenso adzamuwononga ameneyo; popeza Nyumba ya Mulungu ndi yopatulika ndipo Nyumbayo ndi inu amene.
18 Let no one deceive himself: if any one thinks himself to be wise among you in this world, let him become foolish, that he may be wise. (aiōn g165)
Choncho musadzinyenge. Ngati wina wa inu akuganiza kuti ndi wanzeru pa mulingo wa mʼbado uno, ayenera kukhala “wopusa” kuti athe kukhala wanzeru. (aiōn g165)
19 For the wisdom of this world is foolishness with God; for it is written, He who takes the wise in their craftiness.
Pakuti nzeru ya dziko lapansi ndi yopusa pamaso pa Mulungu. Monga kwalembedwera kuti, “Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,”
20 And again, [The] Lord knows the reasonings of the wise that they are vain.
ndiponso, “Ambuye amadziwa kuti maganizo a wanzeru ndi opandapake.”
21 So that let no one boast in men; for all things are yours.
Choncho, wina asanyadire anthu chabe! Zonse ndi zanu,
22 Whether Paul, or Apollos, or Cephas, or [the] world, or life, or death, or things present, or things coming, all are yours;
kaya Paulo kapena Apolo kapena Kefa kapena dziko lapansi, kapena moyo, kapena imfa, kapena tsopano, kapena mʼtsogolo, zonse ndi zanu,
23 and ye [are] Christ's, and Christ [is] God's.
ndipo inu ndinu a Khristu, ndipo Khristu ndi wa Mulungu.

< 1 Corinthians 3 >