< Mark 1 >

1 The beginning of the Gospel of Jesus Christ, the Son of God.
Chiyambi cha Uthenga Wabwino wa Yesu Khristu, Mwana wa Mulungu,
2 As it has been written by the prophet Isaiah: “Behold, I send my Angel before your face, who shall prepare your way before you.
monga zalembedwera mʼbuku la mneneri Yesaya: “Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu, amene adzakonza njira yanu,”
3 The voice of one crying out in the desert: Prepare the way of the Lord; make straight his paths.”
“Mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.’”
4 John was in the desert, baptizing and preaching a baptism of repentance, as a remission of sins.
Ndipo Yohane anabwera mʼmadera a mʼchipululu nabatiza, ndi kulalikira za ubatizo wa kutembenuka mtima ndi wa chikhululukiro cha machimo.
5 And there went out to him all the region of Judea and all those of Jerusalem, and they were baptized by him in the river Jordan, confessing their sins.
Madera onse a ku Yudeya ndi anthu onse a ku Yerusalemu anatuluka napita kwa iye. Akavomereza machimo awo, amawabatiza mu mtsinje wa Yorodani.
6 And John was clothed with camel’s hair and with a leather belt around his waist. And he ate locusts and wild honey.
Yohane amavala zovala zopangidwa ndi ubweya wangamira, ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake, ndipo amadya dzombe ndi uchi wamthengo.
7 And he preached, saying: “One stronger than me comes after me. I am not worthy to reach down and loosen the laces of his shoes.
Ndipo uthenga wake unali uwu: “Pambuyo panga pakubwera wina wondiposa ine mphamvu. Ine si woyenera kuwerama ndi kumasula zingwe za nsapato zake.
8 I have baptized you with water. Yet truly, he will baptize you with the Holy Spirit.”
Ine ndikubatizani ndi madzi, koma Iye adzakubatizani ndi Mzimu Woyera.”
9 And it happened that, in those days, Jesus arrived from Nazareth of Galilee. And he was baptized by John in the Jordan.
Pa nthawi imeneyo Yesu anabwera kuchokera ku Nazareti wa ku Galileya ndipo anabatizidwa ndi Yohane mu mtsinje wa Yorodani.
10 And immediately, upon ascending from the water, he saw the heavens opened and the Spirit, like a dove, descending, and remaining with him.
Pamene Yesu ankatuluka mʼmadzi, anaona kumwamba kukutsekuka ndipo Mzimu Woyera akutsikira pa Iye ngati nkhunda.
11 And there was a voice from heaven: “You are my beloved Son; in you I am well pleased.”
Ndipo Mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndipo ndikondwera nawe.”
12 And immediately the Spirit prompted him into the desert.
Nthawi yomweyo Mzimu Woyera anamutumiza Iye ku chipululu,
13 And he was in the desert for forty days and forty nights. And he was tempted by Satan. And he was with the wild animals, and the Angels ministered to him.
ndipo anali mʼchipululumo masiku makumi anayi, akuyesedwa ndi Satana. Anali pakati pa nyama zakuthengo; ndipo angelo anamutumikira.
14 Then, after John was handed over, Jesus went into Galilee, preaching the Gospel of the kingdom of God,
Yohane atamutsekera mʼndende, Yesu anapita ku Galileya nalalikira Uthenga Wabwino wa Mulungu nati,
15 and saying: “For the time has been fulfilled and the kingdom of God has drawn near. Repent and believe in the Gospel.”
“Nthawi yafika, ufumu wa Mulungu wayandikira. Tembenukani mtima ndi kukhulupirira Uthenga Wabwino!”
16 And passing by the shore of the Sea of Galilee, he saw Simon and his brother Andrew, casting nets into the sea, for they were fishermen.
Pamene Yesu ankayenda mʼmbali mwa nyanja ya Galileya, anaona Simoni ndi mʼbale wake Andreya akuponya khoka mʼnyanja, popeza anali asodzi.
17 And Jesus said to them, “Come after me, and I will make you fishers of men.”
Yesu anati, “Bwerani, tsateni Ine, ndipo ndidzakusandutsani asodzi a anthu.”
18 And at once abandoning their nets, they followed him.
Nthawi yomweyo anasiya makoka awo namutsata Iye.
19 And continuing on a little ways from there, he saw James of Zebedee and his brother John, and they were mending their nets in a boat.
Atapita patsogolo pangʼono, anaona Yakobo ndi mʼbale wake Yohane ana a Zebedayo, ali mʼbwato akukonza makoka awo.
20 And immediately he called them. And leaving behind their father Zebedee in the boat with his hired hands, they followed him.
Mosataya nthawi anawayitana, ndipo anasiya abambo awo Zebedayo ndi anyamata aganyu ali mʼbwatomo, namutsata Iye.
21 And they entered into Capernaum. And entering into the synagogue promptly on the Sabbaths, he taught them.
Iwo anapita ku Kaperenawo, ndipo tsiku la Sabata litafika, Yesu analowa mʼsunagoge nayamba kuphunzitsa.
22 And they were astonished over his doctrine. For he was teaching them as one who has authority, and not like the scribes.
Anthu anadabwa ndi chiphunzitso chake, chifukwa anawaphunzitsa ngati munthu amene anali ndi ulamuliro, osati ngati aphunzitsi amalamulo.
23 And in their synagogue, there was a man with an unclean spirit; and he cried out,
Pomwepo munthu wina mʼsunagogemo amene anali wogwidwa ndi mzimu woyipa anafuwula kuti,
24 saying: “What are we to you, Jesus of Nazareth? Have you come to destroy us? I know who you are: the Holy One of God.”
“Mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”
25 And Jesus admonished him, saying, “Be silent, and depart from the man.”
Yesu anadzudzula chiwandacho mwamphamvu nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye!”
26 And the unclean spirit, convulsing him and crying out with a loud voice, departed from him.
Mzimu woyipawo unamugwedeza mwamphamvu ndipo unatuluka mwa iye ukufuwula.
27 And they were all so amazed that they inquired among themselves, saying: “What is this? And what is this new doctrine? For with authority he commands even the unclean spirits, and they obey him.”
Anthu anadabwa kwambiri kotero kuti anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Ichi nʼchiyani? Chiphunzitso chatsopano ndi ulamuliro! Iye akulamula, ngakhale mizimu yoyipa ikumumvera.”
28 And his fame went out quickly, throughout the entire region of Galilee.
Mbiri yake inafalikira kudera lonse la Galileya mofulumira.
29 And soon after departing from the synagogue, they went into the house of Simon and Andrew, with James and John.
Atangochoka mu sunagoge, Yesu pamodzi ndi Yakobo ndi Yohane anakalowa mʼnyumba ya Simoni ndi Andreya.
30 But the mother-in-law of Simon lay ill with a fever. And at once they told him about her.
Mpongozi wa Simoni anali chigonere akudwala malungo, ndipo anamuwuza Yesu za iye.
31 And drawing near to her, he raised her up, taking her by the hand. And immediately the fever left her, and she ministered to them.
Ndipo Yesu anapita kwa iye, namugwira dzanja namuthandiza kudzuka. Malungo anachoka ndipo anayamba kuwatumikira.
32 Then, when evening arrived, after the sun had set, they brought to him all who had maladies and those who had demons.
Madzulo omwewo dzuwa litalowa anthu anabweretsa kwa Yesu anthu onse odwala ndi ogwidwa ndi ziwanda.
33 And the entire city was gathered together at the door.
Anthu onse a mʼmudzimo anasonkhana pa khomo,
34 And he healed many who were troubled with various illnesses. And he cast out many demons, but he would not permit them to speak, because they knew him.
Yesu anachiritsa ambiri amene anali ndi matenda osiyanasiyana, komanso anatulutsa ziwanda zambiri, ndipo sanalole kuti ziwandazo ziyankhule chifukwa zinkamudziwa Iye.
35 And rising up very early, departing, he went out to a deserted place, and there he prayed.
Mmamawa, kukanali kamdima, Yesu anadzuka, nachoka pa nyumbapo kupita kumalo kwa yekha, kumene anakapemphera.
36 And Simon, and those who were with him, followed after him.
Simoni ndi anzake anapita kokamufunafuna Iye,
37 And when they had found him, they said to him, “For everyone is seeking you.”
ndipo atamupeza, anamuwuza kuti, “Aliyense akukufunani!”
38 And he said to them: “Let us go into the neighboring towns and cities, so that I may preach there also. Indeed, it was for this reason that I came.”
Yesu anayakha kuti, “Tiyeni tipite kwina ku midzi ya pafupi kuti ndikalalikirenso kumeneko. Ichi ndi chifukwa chimene ndinabwerera.”
39 And he was preaching in their synagogues and throughout all of Galilee, and casting out demons.
Potero anayendayenda mu Galileya, kulalikira mʼmasunagoge awo ndi kutulutsa ziwanda.
40 And a leper came to him, begging him. And kneeling down, he said to him, “If you are willing, you are able to cleanse me.”
Munthu wakhate anabwera kwa Iye, nagwada, namupempha kuti, “Ngati mukufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
41 Then Jesus, taking pity on him, reached out his hand. And touching him, he said to him: “I am willing. Be cleansed.”
Yesu pomva naye chifundo, anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo nati, “Ndikufuna, yeretsedwa!”
42 And after he had spoken, immediately the leprosy departed from him, and he was cleansed.
Nthawi yomweyo khate linachoka ndipo anachiritsidwa.
43 And he admonished him, and he promptly sent him away.
Nthawi yomweyo Yesu anamuwuza kuti apite koma anamuchenjeza kuti,
44 And he said to him: “See to it that you tell no one. But go and show yourself to the high priest, and offer for your cleansing that which Moses instructed, as a testimony for them.”
“Wonetsetsa kuti usawuze aliyense za zimenezi. Koma pita, kadzionetse wekha kwa wansembe ndi kukapereka nsembe zimene Mose analamulira zotsimikizira kuyeretsedwa kwanu, ngati umboni kwa iwo.”
45 But having departed, he began to preach and to disseminate the word, so that he was no longer able to openly enter a city, but had to remain outside, in deserted places. And they were gathered to him from every direction.
Mʼmalo mwake anapita nayamba kuyankhula momasuka, nafalitsa mbiriyo. Zotsatira zake, Yesu sanathe kulowa mʼmudzi moonekera, koma anakhala kunja kumalo kopanda anthu. Komabe anthu amabwera kwa Iye kuchokera kulikonse.

< Mark 1 >