< Job 3 >

1 After this Job opened his mouth, and cursed his day,
Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa.
2 saying,
Ndipo Yobu anati:
3 Let the day perish in which I was born, and that night in which they said, Behold a boy!
“Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
4 Let that night be darkness, and let not the Lord regard it from above, neither let light come upon it.
Tsiku limenelo lisanduke mdima; Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso; kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
5 But let darkness and the shadow of death seize it; let blackness come upon it;
Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli; mtambo uphimbe tsikuli; mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
6 let that day and night be cursed, let darkness carry them away; let it not come into the days of the year, neither let it be numbered with the days of the months.
Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani; usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka, kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
7 But let that night be pain, and let not mirth come upon it, nor joy.
Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino; kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
8 But let him that curses that day curse it, [even] he that is ready to attack the great whale.
Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo, iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
9 Let the stars of that night be darkened; let it remain [dark], and not come into light; and let it not see the morning star arise:
Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima; tsikulo liyembekezere kucha pachabe ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
10 because it shut not up the gates of my mother's womb, for [so] it would have removed sorrow from my eyes.
Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.
11 For why died I not in the belly? and [why] did I not come forth from the womb and die immediately?
“Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
12 and why did the knees support me? and why did I suck the breasts?
Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo ndi mawere woti andiyamwitsepo?
13 Now I should have lain down and been quiet, I should have slept and been at rest,
Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere; ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
14 with kings [and] councillors of the earth, who gloried in [their] swords;
pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi, amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
15 or with rulers, whose gold was abundant, who filled their houses with silver:
pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide, amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
16 or [I should have been] as an untimely birth proceeding from his mother's womb, or as infants who never saw light.
Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale, ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
17 There the ungodly have burnt out the fury of rage; there the wearied in body rest.
Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto, ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
18 And the men of old time have together ceased to hear the exactor's voice.
A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere; sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
19 The small and great are there, and the servant that feared his lord.
Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko, ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.
20 For why is light given to those who are in bitterness, and life to those souls which are in griefs?
“Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto, ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
21 who desire death, and obtain it not, digging [for it] as [for] treasures;
kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera, amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
22 and would be very joyful if they should gain it?
amene amakondwa ndi kusangalala akamalowa mʼmanda?
23 Death [is] rest to [such] a man, for God has hedged him in.
Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu amene njira yake yabisika, amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
24 For my groaning comes before my food, and I weep being beset with terror.
Mʼmalo moti ndidye, ndimalira, ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
25 For the terror of which I meditated has come upon me, and that which I had feared has befallen me.
Chimene ndinkachiopa chandigwera; chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
26 I was not at peace, nor quiet, nor had I rest; yet wrath came upon me.
Ndilibe mtendere kapena bata, ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”

< Job 3 >