< Obdias 1 >

1 The vision of Obdias. Thus saith the Lord God to Idumea; I have heard a report from the Lord, and he has sent forth a message to the nations.
Masomphenya a Obadiya. Ambuye Yehova akunena kwa Edomu kuti, Tamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu kukanena kuti, “Konzekani, tiyeni tikachite nkhondo ndi Edomu.”
2 Arise ye, and let us rise up against her to war.
“Taona, ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina; udzanyozedwa kwambiri.
3 Behold, I have made thee small among the Gentiles: thou art greatly dishonoured. The pride of thine heart has elated thee, dwelling [as thou dost] in the holes of the rocks, [as one that] exalts his habitation, saying in his heart, Who will bring me down to the ground?
Kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndipo umamanga nyumba zako pa mapiri ataliatali, iwe amene umanena mu mtima mwako kuti, ‘Ndani anganditsitse pansi?’
4 If thou shouldest mount up as the eagle, and if thou shouldest make thy nest among the stars, thence will I bring thee down, saith the Lord.
Koma ngakhale umawuluka ngati chiwombankhanga ndi kumanga chisa chako pakati pa nyenyezi, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
5 If thieves came in to thee, or robbers by night, where wouldest thou have been cast away? would they not have stolen [just] enough for themselves? and if grape-gatherers went in to thee, would they not leave a gleaning?
“Anthu akuba akanabwera kwa iwe, kapena anthu olanda zinthu akanafika usiku, aa, tsoka lanji limene likukudikira iwe! Kodi akanangotengako zimene akuzifuna zokha? Ngati anthu othyola mphesa akanafika, kodi akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?
6 How has Esau been searched out, and [how] have his hidden things been detected?
Koma Esau adzalandidwa zinthu zonse, chuma chake chobisika chidzabedwa!
7 They sent thee to thy coasts: all the men of thy covenant have withstood thee; thine allies have prevailed against thee, they have set snares under thee: they have no understanding.
Anthu onse ogwirizana nawo adzakupirikitsira kumalire; abwenzi ako adzakunyenga ndi kukugonjetsa; amene amadya chakudya chako adzakutchera msampha, koma iwe sudzazindikira zimenezi.”
8 In that day, saith the Lord, I will destroy the wise men out of Idumea, and understanding out of the mount of Esau.
Yehova akunena kuti, “Tsiku limenelo, kodi sindidzawononga anthu onse anzeru a ku Edomu, anthu odziwa zinthu mʼmapiri a Esau?
9 And thy warriors from Thaeman shall be dismayed, to the end that man may be cut off from the mount of Esau.
Ankhondo ako, iwe Temani, adzachita mantha, ndipo aliyense amene ali mʼphiri la Esau adzaphedwa pa nkhondo.
10 Because of the slaughter and the sin [committed against] thy brother Jacob, shame shall cover thee, and thou shalt be cut off for ever.
Chifukwa cha nkhanza zimene unachitira mʼbale wako Yakobo, udzakhala wamanyazi; adzakuwononga mpaka muyaya.
11 From the day that thou stoodest in opposition [to him], in the days when foreigners were taking captive his forces, and strangers entered into his gates, and cast lots on Jerusalem, thou also wast as one of them.
Pamene adani ankamulanda chuma chake pamene alendo analowa pa zipata zake ndi kuchita maere pa Yerusalemu, pa tsikulo iwe unali ngati mmodzi wa iwo.
12 And thou shouldest not have looked on the day of thy brother in the day of strangers; nor shouldest thou have rejoiced against the children of Juda in the day of their destruction; neither shouldest thou have boasted in the day of [their] affliction.
Iwe sunayenera kunyoza mʼbale wako pa nthawi ya tsoka lake, kapena kunyogodola Ayuda chifukwa cha chiwonongeko chawo, kapena kuwaseka pa nthawi ya mavuto awo.
13 Neither shouldest thou have gone into the gates of the people in the day of their troubles; nor yet shouldest thou have looked upon their gathering in the day of their destruction, nor shouldest thou have attacked their host in the day of their perishing.
Iwe sunayenera kudutsa pa zipata za anthu anga pa nthawi ya masautso awo, kapena kuwanyogodola pa tsiku la tsoka lawo, kapena kulanda chuma chawo pa nthawi ya masautso awo.
14 Neither shouldest thou have stood at the opening of their passages, to destroy utterly those of them that were escaping; neither shouldest thou have shut up his fugitives in the day of affliction.
Sunayenera kudikirira pamphambano ya misewu kuti uphe Ayuda othawa, kapena kuwapereka kwa adani awo Ayuda opulumuka pa nthawi ya mavuto awo.”
15 For the day of the Lord is near upon all the Gentiles: as thou have done, so shall it be [done] to thee: thy recompense shall be returned on thine [own] head.
“Tsiku la Yehova layandikira limene adzaweruza mitundu yonse ya anthu. Adzakuchitira zomwe unawachitira ena; zochita zako zidzakubwerera wekha.
16 For as thou hast drunk upon my holy mountain, [so] shall all the nations drink wine; they shall drink, and go down, and be as if they were not.
Iwe unamwa pa phiri langa loyera, koteronso mitundu ina yonse idzamwa kosalekeza; iwo adzamwa ndi kudzandira ndipo adzayiwalika pa mbiri ya dziko lapansi.
17 But on mount Sion there shall be deliverance, and there shall be a sanctuary; and the house of Jacob shall take for an inheritance those that took them for an inheritance.
Koma pa Phiri la Ziyoni padzakhala chipulumutso; phirilo lidzakhala lopatulika, ndipo nyumba ya Yakobo idzalandira cholowa chake.
18 And the house of Jacob shall be fire, and the house of Joseph a flame, and the house of Esau [shall be] for stubble; and [Israel] shall flame forth against them, and shall devour them, and there shall not be a corn-field [left] to the house of Esau; because the Lord has spoken.
Nyumba ya Yakobo idzasanduka moto ndipo nyumba ya Yosefe idzasanduka lawi la moto; nyumba ya Esau idzasanduka chiputu, ndipo adzayitenthe pa moto ndi kuyipsereza. Sipadzakhala anthu opulumuka kuchokera mʼnyumba ya Esau.” Yehova wayankhula.
19 And they [that dwell] in the south shall inherit the mount of Esau, and they in the plain the Philistines: and they shall inherit the mount of Ephraim, and the plain of Samaria, and Benjamin, and the land of Galaad.
Anthu ochokera ku Negevi adzakhala ku mapiri a Esau, ndipo anthu ochokera mʼmbali mwa mapiri adzatenga dziko la Afilisti. Adzakhala mʼminda ya Efereimu ndi Samariya, ndipo Benjamini adzatenga Giliyadi.
20 And this [shall be] the domain of the captivity of the children of Israel, the land of the Chananites as far as Sarepta; and the captives of Jerusalem [shall inherit] as far as Ephratha; they shall inherit the cities of the south.
Aisraeli amene ali ku ukapolo adzalandira dziko la Kanaani mpaka ku Zarefati; a ku Yerusalemu amene ali ku ukapolo ku Sefaradi adzalandira mizinda ya ku Negevi.
21 And they that escape shall come up from mount Sion, to take vengeance on the mount of Esau; and the kingdom shall be the Lord's.
Opulumukawo adzapita ku Phiri la Ziyoni ndipo adzalamulira mapiri a Esau. Koma ufumuwo udzakhala wa Yehova.

< Obdias 1 >