< John 1 >

1 From the first he was the Word, and the Word was in relation with God and was God.
Pachiyambi panali Mawu, ndipo Mawu anali kwa Mulungu, ndipo Mawu ndiye Mulungu.
2 This Word was from the first in relation with God.
Mawuwa anali ndi Mulungu pachiyambi.
3 All things came into existence through him, and without him nothing was.
Zinthu zonse zinalengedwa ndi Iye; ndipo popanda Iye sikukanakhala kanthu kalikonse kolengedwa.
4 What came into existence in him was life, and the life was the light of men.
Mwa Iye munali moyo, ndipo moyowo unali kuwunika kwa anthu.
5 And the light goes on shining in the dark; it is not overcome by the dark.
Kuwunika kunawala mu mdima, koma mdimawo sunakuzindikire.
6 There was a man sent from God, whose name was John.
Kunabwera munthu amene anatumizidwa kuchokera kwa Mulungu; Iyeyo dzina lake linali Yohane.
7 He came for witness, to give witness about the light, so that all men might have faith through him.
Iye anabwera ngati mboni kudzachitira umboni kuwunikako kuti kudzera mwa iye anthu onse akhulupirire.
8 He himself was not the light: he was sent to give witness about the light.
Iyeyu sanali kuwunika; koma anabwera ngati mboni ya kuwunika.
9 The true light, which gives light to every man, was then coming into the world.
Kuwunika koona kumene kuwunikira munthu aliyense kunabwera ku dziko lapansi.
10 He was in the world, the world which came into being through him, but the world had no knowledge of him.
Iye anali mʼdziko lapansi, ndipo ngakhale kuti dziko lapansi linalengedwa ndi Iye, dziko lapansilo silinamuzindikire Iye.
11 He came to the things which were his and his people did not take him to their hearts.
Iye anabwera kwa iwo amene anali akeake, koma akewo sanamulandire Iye.
12 To all those who did so take him, however, he gave the right of becoming children of God — that is, to those who had faith in his name:
Koma kwa onse amene anamulandira Iye, kwa amene anakhulupirira mʼdzina lake, Iye anawapatsa mphamvu yokhala ana a Mulungu;
13 Whose birth was from God and not from blood, or from an impulse of the flesh and man's desire.
ana wobadwa osati monga mwachilengedwe, kapena chisankho cha munthu, kapena chifuniro cha mwamuna koma wobadwa mwa Mulungu.
14 And so the Word became flesh and took a place among us for a time; and we saw his glory — such glory as is given to an only son by his father — saw it to be true and full of grace.
Mawu anasandulika thupi ndipo anakhala pakati pathu. Ife tinaona ulemerero wake, ulemerero wa Iye amene ndi Mwana mmodzi yekhayo wa Atate, wodzaza ndi chisomo ndi choonadi.
15 John gave witness about him, crying, This is he of whom I said, He who is coming after me is put over me because he was in existence before me.
Yohane achitira umboni za Iye. Iye akufuwula kuti, “Uyu ndi Iye amene ndinati, ‘Iye amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa, Iyeyo analipo ine ndisanabadwe.’”
16 From his full measure we have all been given grace on grace.
Kuchokera mʼkuchuluka kwa chisomo chake ife tonse talandira madalitso pamwamba pa madalitso.
17 For the law was given through Moses; grace and the true way of life are ours through Jesus Christ.
Pakuti lamulo linapatsidwa kudzera mwa Mose; chisomo ndi choonadi zinabwera kudzera mwa Yesu Khristu.
18 No man has seen God at any time; the only Son, who is on the breast of the Father, he has made clear what God is.
Palibe munthu amene anaona Mulungu, koma Mwana mmodzi yekhayo amene ali wa pamtima pa Atate, ndiye anafotokoza za Iye.
19 And this is the witness of John when the Jews sent priests and Levites from Jerusalem to him with the question, Who are you?
Tsopano uwu ndi umboni wa Yohane pamene Ayuda a ku Yerusalemu anatumiza ansembe ndi Alevi kudzamufunsa kuti iye anali yani.
20 He said quite openly and straightforwardly, I am not the Christ.
Iye sanalephere kuvomereza, koma iye anavomereza momasuka kuti, “Ine sindine Khristu.”
21 And they said to him, What then? Are you Elijah? And he said, I am not. Are you the prophet? And his answer was, I am not.
Iwo anamufunsa kuti, “Nanga iwe ndiwe yani? Kodi ndiwe Eliya?” Iye anati, “Sindine.” “Kodi ndiwe Mneneri?” Iye anayankha kuti, “Ayi.”
22 So they said to him, Who are you then? We have to give some answer to those who sent us. What have you to say about yourself?
Pomaliza iwo anati, “Ndiwe yani? Tipatse yankho kuti tipite nalo kwa amene anatituma. Kodi iwe ukuti chiyani za iwe mwini?”
23 He said, I am the voice of one crying in the waste land, Make straight the way of the Lord, as said Isaiah the prophet.
Yohane anayankha ndi mawu a mneneri Yesaya kuti, “Ine ndi mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Wongolani njira ya Ambuye.’”
24 Those who had been sent came from the Pharisees.
Tsopano Afarisi ena amene anatumidwa
25 And they put this question to him, saying, Why then are you giving baptism if you are not the Christ, or Elijah, or the prophet?
anamufunsa Iye kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani, umabatiza ngati iwe si Khristu, kapena Eliya, kapena Mneneri?”
26 John's answer was: I give baptism with water; but there is one among you of whom you have no knowledge;
Yohane anayankha kuti, “Ine ndimabatiza ndi madzi, koma pakati panu payima amene simukumudziwa.
27 It is he who is coming after me; I am not good enough to undo his shoes.
Iye ndi amene akubwera pambuyo panga, ine siwoyenera kumasula zingwe za nsapato zake.”
28 These things took place at Bethany on the other side of the Jordan, where John was giving baptism.
Zonsezi zinachitika ku Betaniya kutsidya lina la mtsinje wa Yorodani, kumene Yohane ankabatizira.
29 The day after, John sees Jesus coming to him and says, See, here is the Lamb of God who takes away the sin of the world!
Pa tsiku lotsatira Yohane anaona Yesu akubwera kwa iye ndipo anati, “Taonani, Mwana Wankhosa wa Mulungu, amene achotsa tchimo la dziko lapansi!
30 This is he of whom I said, One is coming after me who is put over me because he was in existence before me.
Uyu ndi amene ndimatanthauza pamene ndinanena kuti, ‘Munthu amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa analipo ine ndisanabadwe.’
31 I myself had no knowledge of him, but I came giving baptism with water so that he might be seen openly by Israel.
Ine mwini sindinamudziwe Iye, koma ndinabwera kubatiza ndi madzi kuti Iye adziwike mu Israeli.”
32 And John gave this witness, saying, I saw the Spirit coming down from heaven like a dove and resting on him.
Kenaka Yohane anapereka umboni uwu: “Ine ndinaona Mzimu Woyera ngati nkhunda kuchokera kumwamba nakhala pa Iye.
33 I had no knowledge who he was, but he who sent me to give baptism with water said to me, The one on whom you see the Spirit coming down and resting, it is he who gives baptism with the Holy Spirit.
Ine sindikanamudziwa Iye, koma kuti amene anandituma ine kudzabatiza ndi madzi anati kwa ine, ‘Munthu amene udzaona Mzimu Woyera akutsika nakhazikika pa Iye ndi amene adzabatize ndi Mzimu Woyera.’
34 This I saw myself and my witness is that he is the Son of God.
Ine ndaona ndipo ndikuchitira umboni kuti uyu ndi Mwana wa Mulungu.”
35 The day after, John was there again with two of his disciples;
Pa tsiku lotsatira Yohane analinso pamenepo pamodzi ndi awiri a ophunzira ake.
36 And looking at Jesus while he was walking he said, See, there is the Lamb of God!
Iye ataona Yesu akudutsa anati, “Taonani Mwana Wankhosa wa Mulungu!”
37 Hearing what he said, the two disciples went after Jesus.
Ophunzira ake awiriwo atamva iye akunena izi, iwo anamutsatira Yesu.
38 And Jesus, turning round, saw them coming after him and said to them, What are you looking for? They said to him, Rabbi (which is to say, Master), where are you living?
Atatembenuka, Yesu anaona iwo akumutsatira ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?” Iwo anati, “Rabi (kutanthauza kuti Aphunzitsi), kodi mukukhala kuti?”
39 He said to them, Come and see. They went with him then and saw where he was living; and they were with him all that day: it was then about the tenth hour of the day.
Iye anayankha kuti, “Bwerani mudzaone.” Choncho iwo anapita ndi kukaona kumene Iye amakhala, ndipo anakhala naye tsiku limenelo. Linali ngati pafupifupi ora la khumi.
40 Andrew, Simon Peter's brother, was one of the two men who, hearing what John said, went after Jesus.
Andreya mʼbale wake wa Simoni Petro, anali mmodzi wa awiriwo amene anamva zimene Yohane ananena ndiponso amene anamutsata Yesu.
41 Early in the morning he came across his brother and said to him, We have made discovery! It is the Messiah! (which is to say, the Christ).
Choncho chimene Andreya anachita ndi kukapeza mʼbale wake Simoni ndipo anamuwuza kuti, “Ife tamupeza Mesiya,” (kutanthauza kuti Khristu).
42 And he took him to Jesus. Looking at him fixedly Jesus said, You are Simon, the son of John; your name will be Cephas (which is to say, Peter).
Kenaka iye anabweretsa Simoni kwa Yesu, amene anamuyangʼana ndipo anati, “Iwe ndiwe Simoni, mwana wa Yohane. Udzatchedwa Kefa” (limene litanthauza kuti Petro).
43 The day after this, Jesus had a desire to go into Galilee. He came across Philip and said to him, Come and be my disciple.
Pa tsiku lotsatira Yesu anaganiza zopita ku Galileya. Atamupeza Filipo, anati kwa iye, “Nditsate.”
44 Now Philip's town was Beth-saida, where Andrew and Peter came from.
Filipo monga Andreya ndi Petro, anali wochokera ku mzinda mudzi Betisaida.
45 Philip came across Nathanael and said to him, We have made a discovery! It is he of whom Moses, in the law, and the prophets were writing, Jesus of Nazareth, the son of Joseph.
Filipo anakapeza Natanieli ndipo anamuwuza kuti, “Ife tapeza amene Mose analemba za Iye mʼmalamulo, ndi zimene aneneri analembanso za Iye, Yesu wa ku Nazareti, mwana wa Yosefe.”
46 Nazareth! said Nathanael, Is it possible for any good to come out of Nazareth? Philip said to him, Come and see.
Natanieli anafunsa kuti, “Nazareti! Kodi kanthu kalikonse kabwino kangachokere kumeneko?” Filipo anati, “Bwera udzaone.”
47 Jesus saw Nathanael coming to him and said of him, See, here is a true son of Israel in whom there is nothing false.
Yesu atamuona Natanieli akuyandikira, anati kwa iye, “Uyu ndi Mwisraeli weniweni, mwa iye mulibe chinyengo.”
48 Nathanael said to him, Where did you get knowledge of me? In answer Jesus said, Before Philip was talking with you, while you were still under the fig-tree, I saw you.
Natanieli anafunsa kuti, “Kodi mwandidziwa bwanji?” Yesu anayankha kuti, “Ine ndinakuona iwe utakhala pansi pamtengo wamkuyu Filipo asanakuyitane.”
49 Nathanael said to him, Rabbi, you are the Son of God, you are King of Israel!
Kenaka Natanieli ananena kuti, “Rabi, Inu ndinu Mwana wa Mulungu; Inu ndinu Mfumu ya Israeli.”
50 In answer Jesus said to him, You have faith because I said to you, I saw you under the fig-tree. You will see greater things than these.
Yesu anati, “Ukukhulupirira chifukwa chakuti ndakuwuza kuti Ine ndinakuona iwe uli pansi pamtengo wamkuyu? Iwe udzaona zinthu zazikulu kuposa izo.”
51 And he said to him, Truly I say to you all, You will see heaven opening and God's angels going up and coming down on the Son of man.
Ndipo Iye anapitirira kuti, “Zoonadi, Ine ndikuwuza kuti iwe udzaona kumwamba, kutatsekuka ndi angelo a Mulungu akukwera ndi kutsika pa Mwana wa Munthu.”

< John 1 >