< Salme 71 >

1 HERRE, jeg lider på dig, lad mig aldrig i evighed skuffes.
Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
2 Frels mig og udfri mig i din Retfærdighed, du bøjede dit Øre til mig;
Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
3 red mig og vær mig en Tilflugtsklippe, en Klippeborg til min Frelse; thi du er min Klippe og Borg!
Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
4 Min Gud, fri mig ud af gudløses Hånd, af Niddings og Voldsmands Kløer;
Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
5 thi du er mit Håb, o Herre! Fra min Ungdom var HERREN min Tillid;
Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
6 fra Moders Skød har jeg støttet mig til dig, min Forsørger var du fra Moders Liv, dig gælder altid min Lovsang.
Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
7 For mange står jeg som mærket af Gud, men du er min stærke Tilflugt;
Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
8 min Mund er fuld af din Lovsang, af din Ære Dagen lang.
Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
9 Forkast mig ikke i Alderdommens Tid og svigt mig ikke, nu Kraften svinder;
Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
10 thi mine Fjender taler om mig, de der lurer på min Sjæl, holder Råd:
Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
11 "Gud har svigtet ham! Efter ham! Grib ham, thi ingen frelser!"
Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
12 Gud, hold dig ikke borte fra mig, il mig til Hjælp, min Gud;
Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
13 lad dem blive til Skam og Skændsel, dem, der står mig imod, lad dem hylles i Spot og Spe, dem, der vil mig ondt!
Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
14 Men jeg, jeg vil altid håbe, blive ved at istemme din Pris;
Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
15 min Mund skal vidne om din Retfærd, om din Frelse Dagen lang; thi jeg kender ej Ende derpå.
Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
16 Jeg vil minde om den Herre HERRENs Vælde, lovsynge din Retfærd, kun den alene.
Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
17 Gud, du har vejledt mig fra min Ungdom af, dine Undere har jeg forkyndt til nu;
Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
18 indtil Alderdommens Tid og de grånende Hår svigte du mig ikke, o Gud. End skal jeg prise din Arm for alle kommende Slægter.
Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
19 Din Vælde og din Retfærdighed når til Himlen, o Gud; du, som øvede store Ting, hvo er din Lige, Gud?
Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
20 Du, som lod os skue mange fold Trængsel og Nød, du kalder os atter til Live og drager os atter af Jordens Dyb;
Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
21 du vil øge min Storhed og atter trøste mig.
Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
22 Til Gengæld vil jeg til Harpespil prise din Trofasthed, min Gud, lege på Citer for dig, du Israels Hellige;
Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
23 juble skal mine Læber - ja, jeg vil lovsynge dig og min Sjæl, som du udløste;
Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
24 også min Tunge skal Dagen igennem forkynde din Retfærd, thi Skam og Skændsel får de, som vil mig ilde.
Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.

< Salme 71 >