< Ordsprogene 19 >

1 Bedre Fattigmand med lydefri færd end en, som går Krogveje, er han end rig.
Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro, aposa munthu wopusa woyankhula zokhota.
2 At mangle Kundskab er ikke godt, men den træder fejl, som har Hastværk.
Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru; ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira.
3 Et Menneskes Dårskab øder hans Vej, men på HERREN vredes hans Hjerte.
Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta, mtima wake umakwiyira Yehova.
4 Gods skaffer mange Venner, den ringe skiller hans Ven sig fra.
Chuma chimachulukitsa abwenzi; koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa.
5 Det falske Vidne undgår ej Straf; den slipper ikke, som farer med Løgn.
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa; ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka.
6 Mange bejler til Stormands Yndest, og alle er Venner med gavmild Mand.
Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima, ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense.
7 Fattigmands Frænder hader ham alle, end mere skyr hans Venner ham da. Ej frelses den, som jager efter Ord.
Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye, nanji abwenzi ake tsono! Iwo adzamuthawa kupita kutali. Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse.
8 Den, der vinder Vid, han elsker sin Sjæl, og den, der vogter på Indsigt, får Lykke.
Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake. Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino.
9 Det falske Vidne undgår ej Straf, og den, der farer med Løgn, går under.
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka.
10 Vellevned sømmer sig ikke for Tåbe, end mindre for Træl at herske over Fyrster.
Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado, nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga!
11 Klogskab gør Mennesket sindigt, hans Ære er at overse Brøde.
Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga; ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa.
12 Som Brøl af en Løve er Kongens Vrede, som Dug på Græs er hans Gunst.
Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango, koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu.
13 Tåbelig Søn er sin Faders Ulykke, Kvindekiv er som ustandseligt Tagdryp.
Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi.
14 Hus og Gods er Arv efter Fædre, en forstandig Hustru er fra HERREN.
Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo; koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.
15 Dovenskab sænker i Dvale, den lade Sjæl må sulte.
Ulesi umagonetsa tulo tofa nato ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala.
16 Den vogter sin Sjæl, som vogter på Budet, men skødesløs Vandel fører til Død.
Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake, koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa.
17 Er man god mod den ringe, låner man HERREN, han gengælder en, hvad godt man har gjort.
Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova, ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere.
18 Tugt din Søn, imens der er Håb, ellers stiler du efter at slå ham ihjel.
Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo; ngati sutero udzawononga moyo wake.
19 Den, som er hidsig, må bøde, ved Skånsel gør man det værre.
Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango; pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale.
20 Hør på Råd og tag ved Lære, så du til sidst bliver viis.
Mvera uphungu ndipo landira malangizo; pa mapeto pake udzakhala wanzeru.
21 I Mands Hjerte er mange Tanker, men HERRENs Råd er det, der står fast.
Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.
22 Vinding har man af Godhed, hellere fattig end Løgner.
Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha; nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza.
23 HERRENs Frygt er Vej til Liv, man hviler mæt og frygter ej ondt.
Kuopa Yehova kumabweretsa moyo; wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera.
24 Den lade rækker til Fadet, men fører ej Hånden til Munden.
Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale; koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake.
25 Får Spottere Hug, bliver tankeløs klog, ved Revselse får den forstandige Kundskab.
Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo; dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso.
26 Mishandle Fader og bortjage Moder gør kun en dårlig, vanartet Søn.
Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake, ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.
27 Hør op, min Søn, med at høre på Tugt og så fare vild fra Kundskabsord.
Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru.
28 Niddingevidne spotter Retten, gudløses Mund er glubsk efter Uret.
Mboni yopanda pake imanyoza cholungama, ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa.
29 Slag er rede til Spottere, Hug til Tåbers Ryg.
Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa, ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.

< Ordsprogene 19 >