< Ordsprogene 10 >

1 Salomos ordsprog. Viis søn glæder sin fader, tåbelig søn er sin moders sorg.
Miyambo ya Solomoni: Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.
2 Gudløsheds skatte gavner intet, men retfærd redder fra død.
Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa, koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.
3 HERREN lader ej en retfærdig sulte, men gudløses attrå støder han fra sig.
Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala; koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.
4 Doven hånd skaber fattigdom, flittiges hånd gør rig.
Wochita zinthu mwaulesi amasauka, koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.
5 En klog søn samler om sommeren, en dårlig sover om høsten.
Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru, koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.
6 Velsignelse er for retfærdiges hoved, på uret gemmer gudløses mund.
Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama, koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.
7 Den retfærdiges minde velsignes, gudløses navn smuldrer hen.
Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso, koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.
8 Den vise tager mod påbud, den brovtende dåre styrtes.
Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo, koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.
9 Hvo lydefrit vandrer, vandrer trygt; men hvo der går krogveje, ham går det ilde.
Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka; koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.
10 Blinker man med øjet, volder man ondt, den brovtende dåre styrtes.
Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto, koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.
11 Den retfærdiges mund er en livsens kilde, på uret gemmer gudløses mund.
Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo, koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.
12 Had vækker Splid, Kærlighed skjuler alle Synder.
Udani umawutsa mikangano, koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.
13 På den kloges Læber fnder man Visdom, Stok er til Ryg på Mand uden Vid.
Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu, koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.
14 De vise gemmer den indsigt, de har, Dårens Mund er truende Våde.
Anzeru amasunga chidziwitso koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.
15 Den riges Gods er hans faste Stad, Armod de ringes Våde.
Chuma cha munthu wolemera ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.
16 Den retfærdiges Vinding tjener til Liv, den gudløses Indtægt til Synd.
Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama, koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.
17 At vogte på Tugt er Vej til Livet, vild farer den, som viser Revselse fra sig.
Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo, koma wonyoza chidzudzulo amasochera.
18 Retfærdige Læber tier om Had, en Tåbe er den, der udspreder Rygter.
Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama, ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.
19 Ved megen Tale undgås ej Brøde, klog er den, der vogter sin Mund.
Mawu akachuluka zolakwa sizisowa, koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.
20 Den retfærdiges Tunge er udsøgt Sølv, gudløses Hjerte er intet værd.
Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri, koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.
21 Den retfærdiges Læber nærer mange, Dårerne dør af Mangel på Vid.
Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri; koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.
22 HERRENs Velsignelse, den gør rig, Slid og Slæb lægger intet til.
Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma, ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.
23 For Tåben er Skændselsgerning en Leg, Visdom er Leg for Mand med Indsigt.
Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa, koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.
24 Hvad en gudløs frygter, kommer over hans Hoved, hvad retfærdige ønsker, bliver dem givet.
Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira; chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.
25 Når Storm farer frem, er den gudløse borte, den retfærdige står på evig Grund.
Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa, koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.
26 Som Eddike for Tænder og Røg for Øjne så er den lade for dem, der sender ham.
Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso, ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.
27 HERRENs Frygt lægger dage til, gudløses År kortes af.
Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo; koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.
28 Retfærdige har Glæde i Vente, gudløses Håb vil briste.
Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe, koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.
29 For lydefri Vandel er HERREN et Værn, men en Rædsel for Udådsmænd.
Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino, koma wochita zoyipa adzawonongeka.
30 Den retfærdige rokkes aldrig, ikke skal gudløse bo i Landet.
Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.
31 Den retfærdiges Mund bærer Visdoms Frugt, den falske Tunge udryddes.
Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru, koma lilime lokhota lidzadulidwa.
32 Den retfærdiges Læber søger yndest, gudløses Mund bærer Falskheds Frugt.
Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula, koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.

< Ordsprogene 10 >