< 4 Mosebog 29 >

1 På den første Dag i den syvende Måned skal I holde Højtidsstævne, intet som helst Arbejde må I udføre; I skal fejre den som en Hornblæsningsdag.
“‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
2 Da skal I som Brændoffer til en liflig Duft for HERREN ofre en ung Tyr, en Væder og syv årgamle Lam, lydefri Dyr;
Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
3 som Afgrødeoffer dertil fint Hvedemel, rørt i Olie, tre Tiendedele Efa for Tyren, to Tiendedele for Væderen
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
4 og en Tiendedel for hvert af de syv Lam;
Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
5 desuden en Gedebuk som Syndoffer for at skaffe eder Soning;
Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
6 alt foruden Nymånebrændofferet med tilhørende Afgrødeoffer og det daglige Brændoffer med tilhørende Afgrødeoffer og Drikofre efter de derom gældende forskrifter, til en liflig Duft, et Ildoffer for HERREN.
Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
7 På den tiende dag i samme syvende Måned skal I holde Højtidsstævne, I skal faste og må intet som helst Arbejde udføre.
“‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
8 Da skal I som Brændoffer til en liflig duft for HERREN ofre en ung Tyr, en Væder og syv årgamle Lam, lydefri Dyr skal I tage,
Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
9 og som Afgrødeoffer dertil fint Hvedemel, rørt i Olie, tre Tiendedele Efa for Tyren, to Tiendedele for Væderen
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
10 og en Tiendedel for hvert af de syv Lam;
kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
11 desuden en Gedebuk som Syndoffer; alt foruden Soningssyndoffe, det og det daglige Brændoffer med tilhørende Afgrødeoffer og Drikofre.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
12 På den femtende Dag i den syvende Måned skal I holde Højtidsstævne, I må intet som helst Atbejde udføre, og I skal holde Højtid for HERREN i syv Dage.
“‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
13 Da skal I som Brændoffer, som Ildoffer til en liflig Duft for HERREN ofre tretten unge Tyre, to Vædre og fjorten årgamle Lam, lydefri Dyr skal det være,
Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
14 og som Afgrødeoffer dertil fint Hvedemel, rørt i Olie, tre Tiendedele Efa for hver af de tretten Tyre, to Tiendedele for hver af de to Vædre
Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
15 og en Tiendedel for hvert af de fjorten Lam;
Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
16 desuden en Gedebuk som Syndoffer; alt foruden det daglige Brændoffer med tilhørende Afgrødeoffer og Drikoffer.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
17 På den anden Dag skal I ofre tolv unge Tyre, to Vædre og fjorten årgamle Lam, lydefri Dyr,
“‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
18 med tilhørende Afgrødeoffer og Drikofre for Tyrene, Vædrene og Lammene efter deres Tal på den foreskrevne Måde;
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
19 desuden en Gedebuk som Syndoffer; alt foruden det daglige Brændoffer med tilhørende Afgrødeoffer og Drikoffer.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
20 På den tredje Dag skal I ofre elleve unge Tyre, to Vædre og fjorten årgamle Lam, lydefri Dyr,
“‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
21 med tilhørende Afgrødeoffer og Drikofre for Tyrene, Vædrene og Lammene efter deres Tal på den foreskrevne Måde;
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
22 desuden en Gedebuk som Syndoffer; alt foruden det daglige Brændoffer med tilhørende Afgrødeoffer og Drikoffer.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
23 På den fjerde Dag skal I ofre ti Tyre, to Vædre og fjorten årgamle Lam, lydefri Dyr,
“‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
24 med tilhørende Afgrødeoffer og Drikofre for Tyrene, Vædrene og Lammene efter deres Tal på den foreskrevne Måde;
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
25 desuden en Gedebuk som Syndoffer; alt foruden det daglige Brændoffer med tilhørende Afgrødeoffer og Drikoffer.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
26 På den femte Dag skal I ofre ni Tyre, to Vædre og fjorten årgamle Lam, lydefri Dyr,
“‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
27 med tilhørende Afgrødeoffer og Drikofre for Tyrene, Vædrene og Lammene efter deres Tal på den foreskrevne Måde;
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
28 desuden en Gedebuk som Syndoffer; alt foruden det daglige Brændoffer med tilhørende Afgrødeoffer og Drikoffer.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
29 På den sjette Dag skal I ofre otte Tyre, to Vædre og fjorten årgamle Lam, lydefri Dyr,
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
30 med tilhørende Afgrødeoffer og Drikofre for Tyrene, Vædrene og Lammene efter deres Tal på den foreskrevne Måde;
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
31 desuden en Gedebuk til Syndoffer; alt foruden det daglige Brændoffer med tilhørende Afgrødeoffer og Drikoffer.
Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
32 På den syvende dag skal I ofre syv Tyre, to Vædre og fjorten årgamle Lam, lydefri Dyr,
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
33 med tilhørende Afgrødeoffer og Drikofre for Tyrene, Vædrene og Lammene efter deres Tal på den foreskrevne Måde;
Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
34 desuden en Gedebuk som Syndoffer; alt foruden det daglige Brændoffer med tilhørende Afgrødeoffer og Drikoffer.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
35 På den ottende Dag skal I holde festlig Samling, I må intet som helst Arbejde udføre.
“‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
36 Da skal I som Brændoffer, som Ildoffer til en liflig Duft for HERREN ofre en Tyr, en Væder og syv årgamle Lam, lydefri Dyr,
Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
37 med tilhørende Afgrødeoffer og Drikofre for Tyren, Væderen og Lammene efter deres Tal på den foreskrevne Måde;
Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
38 desuden en Gedebuk som Syndoffer; alt foruden det daglige Brændoffer med tilhørende Afgrødeoffer og Drikoffer.
Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
39 Disse Ofre skal I bringe HERREN på eders Højtider, bortset fra eders Løfte og Frivilligofre, hvad enten det nu er Brændofre, Afgrødeofre, Drikofre eller Takofre.
“‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
40 Og Moses talte til Israeliterne, ganske som HERREN havde pålagt Moses.
Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.

< 4 Mosebog 29 >