< Nehemias 3 >

1 Ypperstepræsten Eljasjib og hans Brødre Præsterne tog fat på at bygge Fåreporten; de forsynede den med Bjælkeværk og indsatte Portfløjene; derefter byggede de videre hen til Meatårnet og helligede det og igen videre hen til Hanan'eltårnet.
Pambuyo pake Eliyasibu mkulu wa ansembe ndi ansembe anzake anayamba kugwira ntchito ndipo anamanganso Chipata cha Nkhosa. Iwo anachipatulira Mulungu ndipo anayika zitseko zake. Khoma limene analipatula linafika mpaka pa Nsanja ya Zana ndi Nsanja ya Hananeli.
2 Ved Siden af ham byggede Mændene fra Jeriko, ved Siden af dem Zakkur, Imris Søn.
Anthu a ku Yeriko anamanga chigawo china pambali pake ndipo Zakuri mwana wa Imuri anamanga chigawo chinanso choyandikana nawo.
3 Fiskeporten byggede Sena'as Efterkommere; de forsynede den med Bjælkeværk og indsatte Portfløje, Kramper og Portslåer.
Chipata cha Nsomba chinamangidwanso ndi ana a fuko la Hasena. Iwo anayika mitanda yake ndi zitseko, zotsekera zake, ndi mipiringidzo yake.
4 Ved Siden af dem arbejdede Meremot, en Søn af Hakkoz's Søn Uruja, med at istandsætte Muren. Ved Siden af ham arbejdede Mesjullam, en Søn af Berekja, en Søn af Mesjezab'el, ved Siden af ham Zadok, Ba'anas Søn.
Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi, anakonza chigawo choyandikana nacho. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya, mwana wa Mesezabeli anakonza chigawo china. Pambali pake, Zadoki mwana wa Baana anakonzanso chigawo china.
5 Ved Siden af ham arbejdede Folkene fra Tekoa, men de store iblandt dem bøjede ikke deres Nakke under deres Herres Arbejde.
Pambali pa iwowa anthu a ku Tekowa anakonza chigawo china. Koma wolemekezeka awo anakana kugwira ntchito imene akuluakulu awo anawapatsa.
6 Jesjanaporten istandsatte Jojada, Paseas Søn, og Mesjullam, Besodejas Søn; de forsynede den med Bjælkeværk og indsatte Portfløje, Kramper og Portslåer.
Chipata cha Yesana chinakonzedwa ndi Yoyada mwana wa Paseya ndi Mesulamu mwana wa Besodeya. Iwo anayika mitanda yake ndi kuyika zitseko, zotsekera zake ndi mipiringidzo yake.
7 Ved Siden af dem arbejdede Gibeoniten Melatja og Meronotiten Jadon sammen med Mændene fra Gibeon og Mizpa, der stod under Statholderen hinsides Floden.
Pambali pawo Melatiya Mgibeyoni ndi Yadoni Mmerenoti ndiponso anthu a ku Gibiyoni ndi a ku Mizipa anakonza chigawo chawo mpaka ku nyumba ya bwanamkubwa wa chigawo cha Patsidya pa Yufurate.
8 Ved Siden af ham arbejdede Uzziel, en Søn af Harhaja, en af Guldsmedene. Ved Siden af ham arbejdede Hananja, en af Salvehandlerne; de udbedrede Jerusalem hen til den brede Mur.
Pambali pawo Uzieli mwana wa Harihaya wa mʼgulu amisiri osula golide anakonzanso chigawo china. Pambali pake Hananiya mmodzi mwa anthu oyenga mafuta onunkhira, anakonzanso chigawo china. Iwo anakonzanso Yerusalemu mpaka ku Khoma Lotambasuka.
9 Ved Siden af dem arbejdede Øversten over den ene Halvdel af Jerusalems Område, Refaja, Hurs Søn.
Refaya mwana wa Huri wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu anakonza chigawo china motsatana nawo.
10 Ved Siden af ham arbejdede Jedaja, Harumafs Søn, ud for sit eget Hus. Ved Siden af ham arbejdede Hattusj, Hasjabnejas Søn.
Kulumikiza ichi, Yedaya mwana wa Harumafi anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba yake, ndipo Hatusi mwana wa Hasabaneya anakonzanso motsatana naye.
11 En anden Strækningistandsatte Malkija, Harims Søn, og Hassjub, Pahat-Moabs Søn, hen til Ovntårnet.
Malikiya mwana wa Harimu ndi Hasubu mwana wa Pahati-Mowabu anakonzanso chigawo china ndiponso Nsanja ya Ngʼanjo.
12 Ved Siden af ham arbejdede Øversten over den anden Halvdel af Jerusalems Område, Sjallum, Hallohesj's Søn, sammen med sine Døtre.
Salumu mwana wa Halohesi wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu, anakonzanso chigawo chotsatana nawo mothandizidwa ndi ana ake akazi.
13 Dalporten istandsatte Hanun og Folkene fra Zanoa; de byggede den og indsatte Portfløje, Kramper og Portslåer, og desuden 1000 Alen af Muren hen til Møgporten.
Chipata cha ku chigwa chinakonzedwa ndi Hanuni ndi anthu okhala ku Zanowa. Iwo anachimanganso ndi kuyika zitseko zake ndi zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iwo anakonzanso khoma lotalika mamita 450 mpaka ku Chipata cha Zinyalala.
14 Møgporten istandsatte Øversten over Bet-Kerems Område, Malkija, Rekabs Søn; han byggede den og indsatte Portfløje, Kramper og Portslåer.
Chipata cha Zinyalala chinakonzedwa ndi Malikiya mwana wa Rekabu, wolamulira chigawo cha Beti-Hakeremu. Iye anachimanganso ndi kuyika zitseko zake, zotsekera zake ndi mipiringidzo.
15 Kildeporten istandsatte Øversten over Mizpas Område, Sjallun, Kol-Hozes Søn; han byggede den, forsynede den med Tag og indsatte Portfløje, Kramper og Portslåer; han byggede også Muren ved Dammen, fra hvilken Vandledningen fører til Kongens Have, og hen til Trinene, der fører ned fra Davidsbyen.
Chipata cha Kasupe chinakonzedwa ndi Saluni mwana wa Koli-Hoze, wolamulira chigawo cha Mizipa. Iye anachimanganso ndi kuyikanso denga ndiponso zitseko, zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iye anakonzanso khoma la Dziwe la Siloamu limene lili pafupi ndi munda wa mfumu mpaka ku makwerero otsikira potuluka mzinda wa Davide.
16 Efter ham arbejdede Øversten over den ene Halvdel af Bet-Zurs Område, Nehemja, Azbuks Søn, hen til Pladsen ud for Davids Grave, til den udgravede Dam og til Kærnetroppernes Hus.
Pambali pa iyeyo, Nehemiya mwana wa Azibuki, wolamulira theka la chigawo cha Beti Zuri anakonza chigawo china mpaka kumalo oyangʼanana ndi manda a Davide, mpaka ku dziwe lokumba ndi ku nyumba ya anthu ankhondo.
17 Efter ham arbejdede Leviterne, ført af Rehum, Banis Søn. Ved Siden af ham arbejdede Øversten over den ene Halvdel af Ke'ilas Område, Hasjabja.
Pambali pake Alevi anakonza chigawo china, ndipo mtsogoleri wawo anali Rehumi mwana wa Bani. Pambali pa iye Hasabiya wolamulira theka la chigawo cha Keyila anagwira ntchito ku chigawo chake.
18 Efter ham arbejdede deres Bysbørn, ført af Binnuj, Henadads Søn, Øversten over den anden Halvdel af Ke'ilas Område.
Pambuyo pa iyeyu abale awo anapitiriza kukonza, ndipo mtsogoleri wawo anali Bawai mwana wa Henadadi, wolamulira theka lina la chigawo cha Keyila.
19 Ved Siden af ham istandsatte Øversten over Mizpa, Ezer, Jesuas Søn, en anden Strækning lige ud for Opgangen til Tøjhuset i Hro'en'
Motsatana naye Ezeri mwana wa Yesuwa, wolamulira Mizipa anakonza chigawo chinanso choyangʼanana ndi chikweza chofikira ku nyumba yosungira zida za nkhondo pa ngodya.
20 Efter ham istandsatte Baruk, Zabbajs Søn, op ad Bjerget en Strækning fra Krogen til Indgangen til Ypperstepræsten El-jasjibs Hus.
Motsatana naye, Baruki mwana wa Zakai anakonzanso chigawo china kuchokera pa ngodya mpaka pa chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mkulu wa ansembe.
21 Efter ham istandsatte Meremot, en Søn af Hakkoz's Søn Urija, en Strækning fra Indgangen til Eljasjibs Hus til Gavlen.
Motsatana naye, Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi anakonzanso chigawo china kuchokera ku chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mpaka kumapeto kwake.
22 Efter ham arbejdede Præsterne, Mændene fra Omegnen.
Pambuyo pake ansembe okhala ku chidikha anakonzanso chigawo china.
23 Efter dem arbejdede Binjamin og Hassjub ud for deres Huse. Efter ham arbejdede Azarja, en Søn af Ma'aseja, en Søn af Ananja, ved Siden af sit Hus.
Pambuyo pawo, Benjamini ndi Hasubu anakonza kutsogolo kwa nyumba zawo. Ndipo motsatana nawo, Azariya mwana wa Maaseya mwana wa Ananiya, anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba zawo.
24 Efter ham istandsatte Binnuj, Henadads Søn, en Strækning fra Azarjas Hus til Krogen og til Hjørnet.
Motsatana naye, Binuyi mwana wa Henadadi anakonzanso chigawo china, kuchokera pa nyumba ya Azariya kukafika potsirizira pa ngodya.
25 Efter ham arbejdede Palal, Uzajs Søn, lige ud for Krogen og det Tårn, der springer frem fra det øvre kongelige Hus ved Fængselsgården. Efter ham arbejdede Pedaja, Par'osj's Søn,
Palali mwana Uzai anakonza chigawo china choyangʼanana ndi ngodya ndi nsanja yotuluka pa nyumba yapamwamba ya mfumu ku bwalo la alonda. Motsatana naye, Pedaya mwana wa Parosi,
26 til Stedet ud for Vandporten mod Øst og det fremspringende Tårn.
ndi otumikira mʼNyumba ya Mulungu amene amakhala pa khoma la Ofeli anakonza chigawo china mpaka pa malo oyangʼanana ndi Chipata cha Madzi kuloza kummawa ndiponso nsanja yayitali ija.
27 Efter ham istandsatte Folkene fra Tekoa en Strækning fra Stedet ud for det store, fremspringende Tårn til Ofels Mur. (På Ofel boede Tempeltrællene).
Motsatana nawo, anthu a ku Tekowa anakonzanso chigawo china choyangʼanana ndi nsanja ija yayikulu ndi yayitali mpaka ku khoma la Ofeli.
28 Over for Hesteporten arbejdede Præsterne, hver lige ud for sit Hus.
Kuyambira ku Chipata cha Akavalo anakonza ndi ansembe ena ndipo aliyense amakonza khoma loyangʼanana ndi nyumba yake.
29 Efter dem arbejdede Zadok, Immers Søn, ud for sit Hus. Efter ham arbejdede Østportens Vogter Sjemaja, Sjekanjas Søn.
Motsatana nawo, Zadoki mwana wa Imeri anakonza chigawo china choyangʼanana ndi nyumba yake. Motsatana naye, Semeya mwana wa Sekaniya, mlonda wa Chipata cha Kummawa, anakonzanso khoma.
30 Efter ham istandsatte Hananja, Sjelemjas Søn, og Hanun, Zalafs sjette Søn, en Strækning. Efter ham arbejdede Mesjullam, Berekjas Søn, ud for sit Kammer.
Hananiya mwana wa Selemiya ndiponso Hanuni mwana wachisanu ndi chimodzi wa Zalafi anakonza chigawo china. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya anakonza chigawo choyangʼanana ndi chipinda chake.
31 Efter ham arbejdede Malkija, en af Guldsmedene, hen til Tempeltrællenes Hus. Og Kræmmeme istandsatte Stykket ud for Mifkadporten og hen til Tagbygningen ved Hjørnet.
Motsatana naye, Malikiya mmodzi mwa amisiri a golide anakonza chigawo china mpaka ku nyumba ya atumiki a ku Nyumba ya Mulungu ndiponso ku nyumba ya anthu amalonda moyangʼanana ndi chipata cha Mifikade ndiponso mpaka pa chipinda chapamwamba chapangodya.
32 Og mellem Tagbygningen ved Hjørnet og Fåreporten arbejdede Guldsmedene og Kræmmerne.
Ndipo pakati pa chipinda chapamwamba chapangodya ndi Chipata cha Nkhosa anakonza ndi amisiri a golide ndi anthu amalonda.

< Nehemias 3 >