< 3 Mosebog 11 >

1 HERREN talede til Moses og Aron og sagde til dem:
Yehova anayankhula ndi Mose ndi Aaroni kuti,
2 Tal til Israeliterne og sig: Af alle Dyr på Jorden må du spise følgende:
“Awuze Aisraeli kuti, ‘Nyama zomwe mukhoza kudya mwa nyama zonse za dziko lapansi ndi izi:
3 Alle Dyr, der har Klove, helt spaltede Klove, og tygger Drøv, må I spise.
Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
4 Men følgende må I ikke spise af dem der tygger Drøv, og af dem, der har Klove: Kamelen, thi den tygger vel Drøv, men har ikke Klove; den skal være eder uren;
“‘Koma pali nyama zina zimene zimabzikula kokha kapena ndi zogawikana zipondero zimene simukuyenera kudya. Nyama zimenezi ndi ngamira, ngakhale imabzikula ilibe zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
5 Klippegrævlingen, thi den tygger vel Drøv, men har ikke Klove: den skal være eder uren;
Ina ndi mbira, ngakhale imabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
6 Haren, thi den tygger vel Drøv, men har ikke Klove; den skal være eder uren;
Inanso ndi kalulu, ngakhale amabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi wodetsedwa, musadye.
7 Svinet, thi det har vel Klove, helt spaltede Klove, men tygger ikke Drøv; det skal være eder urent.
Nkhumba simabzikula ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
8 Deres Kød må I ikke spise, og ved Åslerne af dem må I ikke røre; de skal være eder urene.
Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa chifukwa ndi yodetsedwa.
9 Af alt, hvad der lever i Vandet, må I spise følgende: Alt i Vandet, både i Havet og i Floderne, som har Finner og Skæl, må I spise;
“‘Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi a mʼnyanja ndi a mʼmitsinje mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
10 men af alt, hvad der rører sig i Vandet, af alle levende Væsener i Vandet, skal det, som ikke har Finner eller Skæl, hvad enten det er i Havet eller Floderne, være eder en Vederstyggelighed.
Koma zamoyo zonse za mʼnyanja kapena za mʼmitsinje zimene zilibe minga ya pa msana ndi mamba, kaya ndi tizirombo tonse ta mʼmadzi ndi zamoyo zonse zopezeka mʼmenemo ndi zodetsedwa kwa inu.
11 De skal være eder en Vederstyggelighed, deres Kød må I ikke spise, og Ådslerne af dem skal I regne for en Vederstyggelighed.
Pakuti zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu, nyama yake musadye, ndipo zikafa zikhalebe zodetsedwa kwa inu.
12 Alt i Vandet, som ikke har Finner eller Skæl, skal være eder en Vederstyggelighed.
Chamoyo chilichonse cha mʼmadzi chimene chilibe minga ya pa msana kapena mamba ndi chodetsedwa kwa inu.
13 Følgende er de Fugle, I skal regne for en Vederstyggelighed, de må ikke spises, de er en Vederstyggelighed: Ørnen, Lammegribben, Havørnen,
“‘Mbalame zimene simukuyenera kudya chifukwa ndi zodetsedwa ndi izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
14 Glenten, de forskellige Arter af Falke,
nankapakapa, akamtema a mitundu yonse,
15 alle de forskellige Arter af Ravne,
akhungubwi a mitundu yonse,
16 Strudsen, Takmasfuglen, Mågen, de forskellige Arter af Høge,
kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo ndi mtundu uliwonse wa akabawi
17 Uglen, Fiskepelikanen, Hornuglen,
kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
18 Tinsjemetfuglen, Pelikanen, Ådselgribben,
tsekwe, vuwo, dembo,
19 Storken, de forskellige Arter af Hejrer, Hærfuglen og Flagermusen.
indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
20 Alt vinget Kryb der går på fire, skal være eder en Vederstyggelighed.
“‘Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa.
21 Af alt det vingede Kryb, som går på fire, må I dog spise følgende: Dem, der har Skinneben oven over Fødderne til at hoppe med på Jorden.
Komabe mwa zowuluka zokhala ndi miyendo inayi zimene mukhoza kudya ndi zokhazo zimene zili ndi miyendo yolumphira.
22 Af dem må I spise følgende: De forskellige Arter af Græshopper, Solamgræshopper, Hargolgræshopper og Hagabgræshopper.
Pa zimenezo mungathe kudya izi: dzombe la mitundu yonse, atsokonombwe a mitundu yonse, nkhululu za mitundu yonse, ndi ziwala za mitundu yonse.
23 Men alt andet vinget Kryb, der går på fire, skal være eder en Vederstyggelighed.
Koma za mapiko zina zonse zokhala ndi miyendo inayi muzitenge kukhala zodetsedwa kwa inu.
24 Ved følgende Dyr bliver I urene, enhver, der rører ved Ådslerne af dem, bliver uren til Aften,
“‘Zimenezi zidzakudetsani. Aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
25 og enhver, der bærer et Ådsel af dem, skal tvætte sine Klæder og være uren til Aften:
Aliyense wonyamula chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
26 Alle Dyr, der har Klove, men ikke helt spaltede, og som ikke tygger Drøv, skal være urene; enhver, der rører ved dem, bliver uren.
“‘Nyama iliyonse imene ili ndi ziboda zogawikana koma mapazi ake wosagawikana, kapena imene sibzikula muyiyese yodetsedwa kwa inu ndipo munthu aliyense akakhudza nyama yakufayo, adzakhala wodetsedwa.
27 Alle firføddede Dyr, der går på Poter, skal være eder urene; enhver der rører ved et Ådsel af dem, bliver uren til Aften,
Mwa nyama zonse zoyenda ndi miyendo inayi, nyama zonse zokhala ndi zikhadabo kuphazi muzitenge kukhala zodetsedwa ndipo aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
28 og den, som bærer et Ådsel af dem, skal tvætte sine Klæder og være uren til Aften; de skal være eder urene.
Aliyense wonyamula nyamazi zitafa ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu.
29 Af Krybet, der kryber på Jorden, skal følgende være eder urene: Væselen, Musen, de forskellige Arter af Firben,
“‘Mwa nyama zokwawa, zimene zili zodetsedwa kwa inu ndi izi: likongwe, mbewa, msambulu za mitundu yonse,
30 Anakaen, Koadyret, Letåen, Homedyret og Tinsjemetdyret.
gondwa, mngʼazi, buluzi, dududu ndi nanzikambe.
31 Det er dem, som skal være eder urene af alt Krybet. Enhver, der rører ved dem, når de er døde, skal være uren til Aften;
Mwa nyama zonse zoyenda pansi, zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu. Munthu aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
32 alt, hvad et dødt Dyr af den Slags falder ned på, bliver urent, alle Træting, Klæder, Skind, Sække, overhovedet alt, hvad der bruges ved et eller andet Arbejde; det skal lægges i Vand og være urent til Aften; derpå skal det være rent.
Iliyonse mwa nyama zimenezi ikafa ndi kugwera pa chiwiya chilichonse, kaya chimagwira ntchito yotani, kaya ndi chopangidwa ndi mtengo, kaya ndi cha nsalu, kaya ndi cha chikopa kapena chiguduli chiwiyacho chidzakhala chodetsedwa. Muchiviyike mʼmadzi chiwiyacho komabe chidzakhala chodetsedwa mpaka madzulo, ndipo kenaka chidzakhala choyeretsedwa.
33 Og falder et af den Slags ned i et Lerkar, så bliver alt, hvad der er deri, urent, og ethvert sådant Kar skal I slå i Stykker;
Tsono nyama ina iliyonse mwa zimenezi ikagwera mʼmbiya ya dothi, ndiye kuti chilichonse cha mʼmbiyamo chidzakhala chodetsedwa, ndipo muyenera kuswa mbiyayo.
34 alt spiseligt, som man kommer Vand på, og alt flydende, der tjener til Drikke, bliver urent i et sådant Kar.
Chakudya chilichonse chimene mungadye chikakhala kuti chathiridwa mʼmbiyamo, ndiye kuti chakudyacho chidzakhala chodetsedwa, ndipo madzi akumwa wochokera mʼmbiya zotere ndi wodetsedwa.
35 Alt, hvad et dødt Dyr af den Slags falder ned på, bliver urent; Ovne og Ildsteder skal nedbrydes, de er urene, og urene skal de være eder.
Chiwalo chilichonse cha nyama yakufa chikagwera pa chinthu chilichonse kaya pa uvuni, kapena pa mʼphika, ndiye kuti zinthuzo zidzakhala zodetsedwa, ndipo ziphwanyidwe popeza ndi zodetsedwa.
36 Dog bliver Kilder og Cisterner, Steder, hvor der samler sig Vand, ved at være rene; men den, der rører ved Ådslerne deri, bliver uren.
Koma kasupe kapena chitsime chamadzi chidzakhala choyeretsedwa ngakhale kuti chilichonse chokhudza nyama yakufayo chidzakhala chodetsedwa. Zimenezi muzitenge kukhala zodetsedwa.
37 Falder et dødt Dyr af den Slags ned på nogen som helst Slags Sæd, der bruges til Udsæd, bliver denne ved at være ren;
Chiwalo chilichonse cha nyama yakufayo chikagwera pa mbewu zimene akuti adzale, mbewu zimenezo zidzakhalabe zabwino.
38 men kommes der Vand på Sæden, og der så falder et dødt Dyr af den Slags ned på den, skal den være eder uren.
Koma mbewuzo zikakhala zonyowa ndi madzi, ndipo chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo chikagwera pa mbewuzo, mbewuzo zikhale zodetsedwa kwa inu.
39 Når noget af det Kvæg, der tjener eder til Føde, dør, skal den, der rører ved den døde Krop, være uren til Aften.
“‘Ngati nyama imene mumaloledwa kudya yafa yokha, ndiye kuti aliyense wokhudza nyama yakufayo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
40 Den, der spiser noget af den døde Krop, skal tvætte sine Klædet og være uren til Aften, og den, der bærer den døde Krop, skal tvætte sine Klæder og være uren til Aften.
Aliyense amene adyako nyama yakufayo achape zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Aliyense amene wanyamula nyama yakufayo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
41 Alt Kryb, der kryber på Jorden, er en Vederstyggelighed, det må ikke spises;
“‘Chinthu chilichonse chokwawa pansi ndi chonyansa, simuyenera kudya.
42 intet af det, der kryber på Bugen, og intet af det, der går på fire, så lidt som det, der har mange Ben, intet af Krybet, der kryber på Jorden, må I spise thi det er en Vederstyggelighed.
Musadye chilichonse chokwawa pansi, choyenda chamimba kapena choyenda ndi miyendo inayi kapenanso yambiri popeza ndi chodetsedwa.
43 Gør ikke eder selv til en Vederstyggelighed ved noget som helst krybende Kryb, gør eder ikke urene derved, så I bliver urene deraf:
Musadzisandutse nokha odetsedwa ndi chokwawa chilichonse. Musadziyipitse nazo, kuti mukhale odetsedwa.
44 thi jeg er HERREN eders Gud, og I skal hellige eder og være hellige, thi jeg er hellig. Gør eder ikke urene ved noget som helst Kryb, der rører sig på Jorden;
Ine ndine Yehova Mulungu wanu, choncho dziyeretseni kuti mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera. Musadzisandutse odetsedwa ndi chokwawa chilichonse.
45 thi jeg er HERREN, der førte eder op fra Ægypten for at være eders Gud; I skal være hellige, thi jeg er hellig!
Ine ndine Yehova amene ndinakutulutsani ku Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Tsono mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera.
46 Det er Loven om Dyr og Fugle og alle levende Væsener, der bevæger sig i Vandet, og alle levende Væsener, der kryber på Jorden,
“‘Amenewa ndi malamulo onena za nyama, mbalame, chamoyo chilichonse choyenda mʼmadzi ndiponso chamoyo chilichonse chokwawa.
47 til Skel mellem det urene og det rene, mellem de Dyr, der må spises, og dem, der ikke må spises.
Muzisiyanitsa pakati pa chodetsedwa ndi choyeretsedwa, komanso pakati pa zomwe mutha kudya ndi zomwe simuyenera kudya.’”

< 3 Mosebog 11 >