< Ezekiel 4 >

1 Du Mennneskesøn tag dig en teglsten, læg den for dig og indrids i den et Billede af en By, Jerusalem;
Mulungu anati, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga njerwa, uliyike pamaso pako ndipo ujambulepo chithunzi cha mzinda wa Yerusalemu.
2 og kast en Vold op omkring den, byg Belejringstårne, opkast Stormvold, lad Hære lejre sig imod den og rejs Stormbukke mod den fra alle Sider;
Ndipo uwuzinge mzindawo motere: uwumangire nsanja zowuzinga, uwumbire mitumbira ya nkhondo, uwumangire misasa ya nkhondo ndipo uyike zida zogumulira kuzungulira mzindawo.
3 tag dig så en Jernpande og sæt den som en Jernvæg op mellem dig og Byen og ret dit Ansigt imod den. Således skal den være omringet, og du skal trænge den. Det skal være Israels Hus et Tegn.
Kenaka utenge chiwaya chachitsulo uchiyike ngati khoma lachitsulo pakati pa iwe ndi mzindawo. Uyangʼanitsitse mzindawo ndipo udzakhala wozingidwa ndi nsanja za nkhondo. Choncho umangire nsanja zankhondo. Chimenechi chidzakhala chizindikiro kwa Aisraeli.
4 Og læg du dig på din venstre Side og tag, Israels Huss Misgerning på dig; alle de Dage du ligger således, skal du bære deres Misgerning.
“Tsono iwe ugonere kumanzere kwako ndipo ndidzayika pa iwe tchimo la Aisraeli. Iwe udzasenza tchimolo masiku onse amene udzagonere mbali imeneyo.
5 Deres Misgernings År gør jeg til lige så mange Dage for dig, 190 Dage; så længe skal du bære Israels Huss Misgerning.
Ine ndakuyikira masiku okwana 390 malingana ndi zaka za machimo awo. Umu ndi mmene udzasenzere machimo a Aisraeli.
6 Og når de er til Ende, læg dig så på din højre Side og bær Judas Huss Misgerning 40 Dage; for hvert År giver jeg dig en Dag.
“Utatha zimenezo udzagonerenso mbali ya kudzanja lamanja, ndipo udzasenza machimo a anthu a ku Yuda masiku makumi anayi, tsiku lililonse kuyimira chaka chimodzi.
7 Og du skal rette dit Ansigt og din blottede Arm mod det omringede Jerusalem og profetere imod det.
Tsono udzayangʼanitsitse nsanja za nkhondo zozinga. Dzanja la mkanjo wako utalikwinya ndi dzanja lako utakweza, udzalosere modzudzula Yerusalemu.
8 Og se, jeg lægger Bånd på dig, så du ikke kan vende dig fra den ene Side til den anden, før din Belejrings Dage er til Ende.
Ine ndidzakumanga ndi zingwe kotero kuti sudzatha kutembenukira uku ndi uku mpaka utatsiriza masiku akuzingidwa ako.
9 Og tag du dig Hvede, Byg, Bønner, Linser, Hirse og Spelt, kom det i et og samme Kar og lav dig Brød deraf; alle de Dage du ligger på Siden, 190 Dage, skal det være din Mad;
“Tsono tenga tirigu ndi barele, nyemba ndi mphodza, mapira ndi mchewere; ndipo uyike zonsezi mʼmbale imodzi ndipo upange buledi wako. Uzidya pa masiku 390 amene udzakhala ukugonera mbali imodzi.
10 og Maden, du får, skal være efter Vægt, tyve Sekel daglig; du skal spise den een Gang daglig.
Uyeze theka la kilogalamu la chakudyacho kuti uzidya tsiku lililonse kamodzi kokha.
11 Og Vand skal du drikke efter Mål, en Sjettedel Hin; du skal drikke een Gang daglig.
Uyezenso zikho ziwiri zamadzi ndipo uzimwa tsiku ndi tsiku.
12 Og som Bygkager skal du spise det og bage det ved Menneskeskarn i deres Påsyn.
Uzidya chakudya chako ngati momwe amadyera keke ya barele. Uzidzaphika chakudyacho anthu akuona pogwiritsa ntchito ndowe ya munthu ngati nkhuni.”
13 Og du skal sige: "Så sige HERREN: Således skal Israeliterne have urent Brød til Føde blandt de Folk, jeg bortstøder dem til!"
Yehova anati, “Chimodzimodzi anthu a Israeli adzadya chakudya chodetsedwa ku mayiko achilendo kumene Ine ndidzawapirikitsira.”
14 Men jeg sagde: "Ak, Herre, HERRE, jeg har endnu aldrig været uren; noget selvdødt eller sønderrevet har jeg fra Barnsben aldrig spist, og urent Kød kom aldrig i min Mund!"
Koma ine ndinati, “Zisatero, Ambuye Yehova! Ine sindinadziyipitsepo pa zachipembedzo. Kuyambira ubwana wanga mpaka tsopano, sindinadyepo kanthu kalikonse kopezeka katafa kapena kophedwa ndi zirombo za kutchire. Palibe nyama yodetsedwa pa zachipembedzo imene inalowa pakamwa panga.”
15 Da svarede han: "Vel, jeg tillader dig at tage Oksegødning i Stedet for Menneskeskarn og bage dit Brød derved."
Iye anati, “Chabwino, ndidzakulola kuti uphike buledi wako ndi ndowe za ngʼombe mʼmalo mwa ndowe za munthu.”
16 Videre sagde han til mig: Menneskesøn! Se, jeg bryder Brødets Støttestav i Jerusalem; Brød skal de spise efter Vægt og i Angst, og Vand skal de drikke efter Mål og i Rædsel,
Pambuyo pake anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Yerusalemu ndidzawachepetsera chakudya. Anthuwo adzadya chakudya chochita kuyeza ndipo azidzadya mwa nkhawa. Azidzamwanso madzi ochita kuyeza ndiponso mwa mantha.
17 for at de må mangle Brød og Vand og alle som een være slagne af Rædsel og hensmægte i deres Misgerning.
Ndidzachita zimenezi kuti adzasowe chakudya ndi madzi. Choncho adzachita nkhawa akumapenyana ndipo adzatheratu ndi kuwonda chifukwa cha machimo awo.”

< Ezekiel 4 >