< 5 Mosebog 25 >

1 Når der opstår Strid mellem Mænd, og de møder for Retten, skal man dømme dem imellem; den, der har Ret, skal frikendes, den skyldige dømmes.
Anthu akasemphana mawu, ayenera kupita ku bwalo la milandu ndipo woweruza adzaweruza mlanduwo. Adzamasula wosalakwa nalanga wolakwa.
2 Og dersom den skyldige idømmes Prygl, skal Dommeren lade ham lægge sig på Jorden og i sit Påsyn lade ham få det Antal Slag, der svarer til hans Forseelse.
Munthu akapezeka wolakwa ayenera kukwapulidwa, woweruza amugoneke pansi wolakwayo ndipo akwapulidwe pamaso pake zikoti zochuluka molingana ndi mlandu wake,
3 Fyrretyve Slag må han lade ham få, men heller ikke flere, for at din Broder ikke skal vanæres for dine Øjne, når han får endnu flere Slag.
koma asamukwapule zikoti zopitirira makumi anayi. Akakwapulidwa kupitirira apo ndiye kuti mʼbale wanuyo anyozeka pamaso panu.
4 Du må ikke binde Munden til på en Okse, når den tærsker.
Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu.
5 Når flere Brødre bor sammen, og en af dem dør uden at efterlade sig nogen Søn, må hans Enke ikke gifte sig med en fremmed Mand uden for Slægten; men hendes Svoger skal gå til hende og tage hende til Ægte, idet han indgår Svogerægteskab med hende.
Ngati abale akukhala pamodzi ndipo wina mwa iwo akamwalira wosasiya mwana wamwamuna, mkazi wamasiyeyo asakakwatiwe ndi mlendo. Mʼbale wake wa mwamuna wakeyo amukwatire kukwaniritsa chimene akuyenera kuchita kwa mlamu wakeyo.
6 Og den første Søn, hun føder, skal bære den afdøde Broders Navn, for at hans Navn ikke skal udslettes af Israel.
Mwana wamwamuna woyamba amene mayiyo angabereke ayenera kutenga dzina la mwamuna wake womwalirayo kuti dzina lake lisafafanizike mu Israeli.
7 Men hvis Manden er uvillig til af ægte sin Svigerinde, skal hun gå hen til de Ældste i Byporten og sige: "Min Svoger vægrer sig ved at opretholde sin Broders Navn i Israel og vil ikke indgå Svogerægteskab med mig!"
Komabe, ngati munthu sakufuna kukwatira mkazi wa mʼbale wakeyo, mkaziyo ayenera kupita kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda ndi kukanena kuti, “Mʼbale wake wa mwamuna wanga akukana kupitiriza dzina la mʼbale wake mu Israeli. Iye akukana kulowa chokolo.”
8 Derpå skal de Ældste i Byen stævne ham for sig og tale ham til, og hvis han da fastholder sin Beslutning og erklærer sig uvillig til at ægte hende,
Pamenepo akuluakulu a mu mzinda wawowo adzamuyitanitsa nakamba naye. Ngati alimbikirabe kunena kuti, “Ine sindikufuna kumukwatira mkaziyu,”
9 skal hans Svigerinde i de Ældstes Påsyn gå hen til ham, drage hans Sko af hans Fod og spytte ham i Ansigtet og tage til Orde og sige: "Således gør man ved den Mand, som ikke vil opbygge sin Broders Slægt!"
mkazi wamasiye wa mʼbale wakeyo adzapita kwa iye pamaso pa akuluakuluwo namuvula nsapato imodzi, adzamulavulire kumaso nʼkunena kuti, “Izi ndi zimene amachitira munthu amene safuna kupitiriza mbiri ya banja la mʼbale wake.”
10 Og hans Navn i Israel skal være: den barfodedes Hus.
Mbiri ya banja la munthu ameneyo idzadziwika mu Israeli kuti ndi Banja la Wovulidwa nsapato.
11 Når der opstår Trætte mellem to Mænd, og den enes Hustru kommer til for at fri sin Mand fra den andens Slag, og hun rækker sin Hånd ud og tager fat i den andens Blusel,
Ngati anthu awiri akuchita ndewu ndipo mkazi wa mmodzi wa iwo abwera kudzaleretsa mwamuna wake kwa mnzakeyo natambasula dzanja lake kugwira ku maliseche kwa winayo,
12 da skal du hugge hendes Hånd af; du må ikke vise Skånsel.
muyenera kumudula dzanja, osamumvera chisoni.
13 Du må ikke have to Slags Vægtlodder i din Pung, større og mindre.
Musamakhale ndi miyeso iwiri yosiyana mʼthumba mwanu, wolemera ndi wopepuka.
14 Du må ikke have to Slags Efaer i dit Hus, en større og en mindre.
Musamakhale ndi milingo iwiri yosiyana mʼnyumba mwanu, waukulu ndi waungʼono.
15 Fuldvægtige Lodder og Efaer, der holder Mål, skal du have, for at du kan få et langt Liv i det Land, HERREN din Gud vil give dig.
Muyenera kukhala ndi miyeso ndi milingo yoyenera ndi yosanyenga kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
16 Thi en Vederstyggelighed for HERREN din Gud er enhver, der øver sligt, enhver, der begår Svig.
Pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita za chinyengo zoterezi.
17 Kom i Hu, hvad Amalekiterne gjorde imod dig undervejs, da I drog bort fra Ægypten,
Kumbukirani zimene Aamaleki anakuchitirani pamene munali pa ulendo wochokera ku Igupto.
18 hvorledes de kom imod dig undervejs og uden at frygte Gud huggede alle dine udmattede Efternølere ned, da du var træt og nødig.
Pamene munali otopa ndi ofowoka, iwo anakumana nanu pa ulendo wanu ndi kukantha onse otsalira mʼmbuyo ndipo iwo sanaope Mulungu.
19 Når derfor HERREN din Gud giver dig Ro for alle dine Fjender rundt om i det Land, HERREN din Gud vil give dig i Arv og Eje, da skal du udrydde ethvert Minde om Amalek. Glem det ikke!
Pamene Yehova Mulungu wanu akupumulitsani kwa adani onse okuzungulirani mʼdziko limene akupatsani inu ngati cholowa chanu, mudzawafafanize Aamaleki, asadzawakumbukirenso pa dziko lapansi. Musadzayiwale chimenechi!

< 5 Mosebog 25 >