< Første Krønikebog 27 >

1 Israeliterne efter deres Tal: Fædrenehusenes Overhoveder, Tusind- og Hundredførerne og deres Fogeder, som tjente Kongen i alle Sager vedrørende Skifterne, de, der skiftevis trådte til og fra hver Måned hele Året rundt, hvert Skifte på 24000 Mand:
Uwu ndi mndandanda wa Aisraeli, atsogoleri a mabanja, olamulira asilikali 1,000, olamulira asilikali 100 ndi akuluakulu awo, amene ankatumikira mfumu mʼzonse zokhudza magulu a ankhondo, amene amagwira ntchito mwezi ndi mwezi chaka chonse. Gulu lililonse linali ndi anthu 24,000.
2 Over det første Skifte, den første Måneds Skifte stod Isjba'al, Zabdiels Søn - til hans Skifte hørte 24000 Mand
Amene amalamulira gulu loyamba pa mwezi woyamba anali Yasobeamu mwana wa Zabidieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
3 af Perez's Efterkommere, Overhoved for alle Hærførerne; det var den første Måned.
Iyeyu anali chidzukulu cha Perezi ndipo anali mkulu wa atsogoleri onse a ankhondo mwezi woyamba.
4 Over den anden Måneds Skifte stod Ahohiten El'azar, Dodajs Søn; til hans Skifte hørte 24000 Mand.
Amene amalamulira gulu lachiwiri pa mwezi wachiwiri anali Dodai Mwahohi; Mikiloti ndiye anali mtsogoleri wa gulu lake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
5 Den tredje Hærfører, ham i den tredje Måned, var Benaja, Ypperstepræsten Jojadas Søn; til hans Skifte hørte 24000 Mand.
Wolamulira ankhondo wachitatu, pa mwezi wachitatu anali Benaya, mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anali mtsogoleri ndipo pa gulu lake panali ankhondo 24,000.
6 Denne Benaja var Helten blandt de tredive og stod i Spidsen for de tredive, og ved hans Skifte var hans Søn Ammizabad.
Uyu ndi Benaya uja amene anali wamphamvu pa gulu la anthu makumi atatu ndipo ndiye amatsogolera anthu makumi atatu aja. Mwana wake Amizabadi ndiye amatsogolera gulu lake.
7 Den fjerde, ham i den fjerde Måned, var Joabs Broder Asa'el og efter ham hans Søn Zebadja; til hans Skifte hørte 24000 Mand.
Wachinayi pa mwezi wachinayi anali Asaheli mʼbale wake wa Yowabu; ndipo mwana wake Zebadiya ndiye analowa mʼmalo mwake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
8 Den femte, ham i den femte Måned, var Hærføreren Zeraiten Sjamhut; til hans Skifte hørte 24000 Mand.
Wachisanu pa mwezi wachisanu anali Samihuti, mdzukulu wa Izira. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
9 Den sjette, ham i den sjette Måned, var Ira, Ikkesjs Søn, fra Tekoa; til hans Skifte hørte 24000 Mand.
Wa 6 pa mwezi wa 6 anali Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
10 Den syvende, ham i den syvende Måned, var Peloniten Helez af Efraimiterne; til hans Skifte hørte 24000 Mand.
Wa 7 pa mwezi wa 7 anali Helezi Mpeloni wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
11 Den ottende, ham i den ottende Måned, var Husjatiten Sibbekaj af Zeras Slægt; til hans Skifte hørte 24000 Mand.
Wa 8 pa mwezi wa 8 anali Sibekai Mhusati, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000
12 Den niende, ham i den niende Måned, var Abiezer fra Anatot at Benjaminiterne; til hans Skifte hørte 24000 Mand.
Wa 9 pa mwezi wa 9 anali Abiezeri wa banja la Anatoti, wa fuko la Benjamini. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
13 Den tiende, ham i den tiende Måned, var Maharaj fra Netofa af Zeras Slægt, til hans Skifte hørte 24000 Mand.
Wa khumi pa mwezi wa khumi anali Mahazayi wa ku Netofa, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
14 Den ellevte, ham i den ellevte Måned, var Benaja fra Pir'aton af Efraimiterne; til hans Skifte hørte 24000 Mand.
Mtsogoleri wa 11, pa mwezi wa 11 anali Benaya wa ku Piratoni, wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
15 Den tolvte, ham i den tolvte Måned, var Heldaj fra Netofa af Otniels Slægt; til hans Skifte hørte 24000 Mand.
Mtsogoleri wa 12, pa mwezi wa 12 anali Helidai Mnetofa, wa banja la Otanieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
16 I Spidsen for Israels Stammer stod: Som Fyrste for Rubeniterne Eliezer, Zikris Søn; for Simeoniterne Sjefatja, Ma'akas Søn;
Akuluakulu amene amatsogolera mafuko a Israeli ndi awa: Mtsogoleri wa fuko la Rubeni: Eliezara mwana wa Zikiri; mtsogoleri wa fuko la Simeoni: Sefatiya mwana wa Maaka;
17 for Levi Hasjabja, Hemuels Søn, for Aron Zadok;
mtsogoleri wa fuko la Levi: Hasabiya mwana wa Kemueli, mtsogoleri wa banja la Aaroni: Zadoki;
18 for Juda Eliab, en af Davids Brødre; for Issakar Omri, Mikaels Søn;
mtsogoleri wa fuko la Yuda: Elihu, mʼbale wake wa Davide; mtsogoleri wa fuko la Isakara: Omuri mwana wa Mikayeli;
19 for Zebulon Jisjmaja, Obadjas Søn; for Naftali Jerimot, Azriels Søn;
mtsogoleri wa fuko la Zebuloni: Isimaiya mwana wa Obadiya; mtsogoleri wa fuko la Nafutali: Yerimoti mwana wa Azirieli;
20 for Efraimiterne Hosea, Azazjas Søn; for Manasses halve Stamme Joel, Pedajas Søn;
mtsogoleri wa fuko la Efereimu: Hoseya mwana wa Azaziya; mtsogoleri wa fuko la theka la Manase: Yoweli mwana wa Pedaya;
21 for Manasses anden Halvdel i Gilead Jiddo, Zekarjas Søn; for Benjamin Ja'asiel, Abners Søn;
mtsogoleri wa fuko la theka la Manase limene linali ku Giliyadi: Ido mwana wa Zekariya; mtsogoleri wa fuko la Benjamini: Yaasieli mwana wa Abineri;
22 for Dan Azar'el, Jerobams Søn. Det var Israels Stammers Øverster.
mtsogoleri wa fuko la Dani: Azareli mwana wa Yerohamu. Awa anali akuluakulu a mafuko a Israeli.
23 David tog ikke Tal på dem, dervar under tyve År, thi HERREN havde forjættet at ville gøre Israel talrigt som Himmelens Stjerner.
Davide sanawerenge amuna amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kucheperapo, chifukwa Yehova analonjeza kuti adzachulukitsa Aisraeli ngati nyenyezi zamumlengalenga.
24 Joab, Zerujas Søn, begyndte at tælle dem, men fuldførfe det ikke; thi for den Sags Skyld ramtes Israel af Vrede, og Tallet indførtes ikke i Kong Davids Krønike.
Yowabu mwana wa Zeruya anayamba kuwerenga amuna koma sanamalize. Mkwiyo unagwera Aisraeli chifukwa cha zimenezi ndipo chiwerengerochi sanachilowetse mʼbuku la mbiri ya mfumu Davide.
25 Over Kongens Skatte havde Azmavet, Adiels Søn, Opsynet, og over Forrådene ude på Landet, i Byerne, Landsbyerne og Fæstningerne Jonatan, Uzzijas Søn;
Azimaveti mwana wa Adieli ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa mfumu. Yonatani mwana wa Uziya ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa maboma ozungulira, mizinda, midzi ndi malo olondera.
26 over Markarbejderne ved Jordens Dyrkning Ezri, Kelubs Søn;
Eziri mwana wa Kelubi ankayangʼanira anthu ogwira ntchito yolima ku munda.
27 over Vingårdene Sjim'i fra Rama; over Vinforrådene i Vingårdene Sjifmiten Zabdi;
Simei wa ku Rama ankayangʼanira minda ya mpesa. Zabidi wa ku Sifamu ankayangʼanira mphesa ndi mosungiramo mwake.
28 over Oliventræerne og Morbærfigentræerne i Lavlandet Ba'al-Hanan fra Geder; over Olieforrådene Joasj;
Baala-Hanani wa ku Gederi ankayangʼanira mitengo ya olivi ndi ya mikuyu ya ku Sefela. Yowasi ankayangʼanira mafuta a Olivi.
29 over Hornkvæget, der græssede på Saron, Saroniten Sjitraj; over Hornkvæget i Dalene Sjafat, Adlajs Søn;
Sitirayi wa ku Saroni ankayangʼanira ziweto zimene amaweta ku Saroni. Safati mwana wa Adilayi ankayangʼanira ngʼombe zakuzigwa.
30 over Kamelerne Ismaelitem Obil; over Æslerne Jedeja fra Meronot;
Obili Mwismaeli ankayangʼanira ngamira. Yehideya Mmerenoti ankayangʼanira abulu.
31 over Småkvæget Hagriten Jaziz. Alle disse var Overopsynsmænd over Kong Davids Ejendele.
Yazizi Mhagiri akayangʼanira nkhosa ndi mbuzi. Onsewa anali akuluakulu oyangʼanira chuma cha mfumu Davide.
32 Davids Farbroder Jonatan, en indsigtsfuld og skriffkyndig Mand, var Rådgiver. Jehiel, Hakmonis Søn, opdrog Kongens Sønner.
Yonatani, malume wake wa Davide, anali phungu wake ndipo anali munthu wanzeru komanso analinso mlembi. Yehieli mwana wa Hakimoni ankasamalira ana a mfumu.
33 Akitofel var Kongens Rådgiver og Arkiten Husjaj Kongens Ven.
Ahitofele anali phungu wa mfumu. Husai Mwariki anali bwenzi la mfumu.
34 Akitofels Eftermand var Jojada, Benajas Søn, og Ebjatar. Joab var Kongens Hærfører.
Ahitofele atamwalira mʼmalo mwake munalowa Yehoyada mwana wa Benaya ndi Abiatara. Yowabu anali mtsogoleri wa gulu lankhondo la mfumu.

< Første Krønikebog 27 >