< Lukáš 9 >

1 I svolav dvanácte učedlníků svých, dal jim sílu a moc nad všelikým ďábelstvím, a aby neduhy uzdravovali.
Yesu atawayitana khumi ndi awiriwo pamodzi, Iye anawapatsa mphamvu ndi ulamuliro wotulutsa ziwanda zonse ndi kuchiritsa matenda.
2 I poslal je, aby kázali království Boží, a uzdravovali nemocné.
Ndipo Iye anawatumiza kukalalikira za ufumu wa Mulungu ndi kukachiritsa odwala.
3 A řekl jim: Nic nebeřte na tu cestu, ani hůlky, ani mošny, ani chleba, ani peněz, ani po dvou sukních mívejte.
Iye anawawuza kuti, “Musatenge kanthu paulendo. Musatenge ndodo, thumba, buledi, ndalama, ndi malaya apadera.
4 A do kteréhožkoli domu vešli byste, tu zůstaňte, a odtud vyjděte.
Nyumba iliyonse imene mulowa, mukhale momwemo kufikira mutachoka mu mzindawo.
5 A kteříž by vás koli nepřijali, vyjdouce z města toho, také i ten prach z noh svých vyrazte na svědectví proti nim.
Ngati anthu sakulandirani, sasani fumbi la kumapazi anu pomwe mukuchoka mu mzinda wawo ngati umboni owatsutsa.”
6 I vyšedše, chodili po městečkách vůkol, zvěstujíce evangelium, a uzdravujíce všudy.
Ndipo iwo ananyamuka napita, mudzi ndi mudzi, kulalikira Uthenga Wabwino ndi kuchiritsa anthu paliponse.
7 Uslyšel pak Heródes čtvrták o všech věcech, kteréž se dály od něho. I rozjímal to v mysli své, proto že bylo praveno od některých, že by Jan vstal z mrtvých,
Tsopano Herode olamulirayo anamva zonse zimachitikazi. Ndipo iye anavutika kwambiri chifukwa ena amati Yohane waukitsidwa kwa akufa,
8 A od jiných, že by se Eliáš zjevil, od některých pak, že by jeden z proroků starých vstal.
ena amati Eliya waonekera, ndipo ena anatinso mmodzi wa aneneri akalekale waukanso.
9 I řekl Heródes: Jana jsem já sťal. Kdož pak jest tento, o kterémž já slyším takové věci? I žádostiv byl ho viděti.
Koma Herode anati, “Ine ndinamudula mutu Yohane. Nanga uyu ndani amene ndikumva zinthu zotere za Iye?” Ndipo iye anayesetsa kuti amuone Iye.
10 Vrátivše se pak apoštolé, vypravovali jemu, cožkoli činili. A pojav je, odšel soukromí na místo pusté města řečeného Betsaida.
Atumwi atabwerera, anamuwuza Yesu zimene anachita. Kenaka Iye anawatenga napita kwa okha ku mudzi wa Betisaida.
11 Zvěděvše pak zástupové, šli za ním; i přijal je, a mluvil jim o království Božím, a ty, kteříž uzdravení potřebovali, uzdravoval.
Koma gulu la anthu linadziwa ndipo anamutsatira. Iye anawalandira ndi kuyankhula nawo za ufumu wa Mulungu, ndi kuchiritsa amene amafuna machiritso.
12 Den pak počal se nachylovati. I přistoupivše dvanácte, řekli jemu: Propusť zástupy, ať rozejdouce se do městeček okolních a do vesnic, jdou a hledají pokrmů, nebo jsme tuto na místě pustém.
Chakumadzulo dzuwa litapita, khumi ndi awiriwo anabwera kwa Iye ndipo anati, “Uzani gulu la anthuli lichoke kuti apite ku midzi yotizungulira ndi madera a ku mudzi kuti akapeze chakudya ndi pogona, chifukwa kuno ndi kuthengo.”
13 I řekl jim: Dejte vy jim jísti. A oni řekli: Nemámeť víc než pět chlebů a dvě rybě, leč bychom my snad šli a nakoupili na tento všecken lid pokrmů?
Iye anayankha kuti, “Apatseni chakudya kuti adye.” Iwo anayankha kuti, “Ife tili ndi malofu a buledi asanu okha ndi nsomba ziwiri, pokhapokha titapita kukagula chakudya cha gulu la anthu onsewa.”
14 Nebo bylo mužů okolo pěti tisíců. I řekl učedlníkům svým. Rozkažte se jim posaditi v každém řadu po padesáti.
(Pamenepo panali amuna pafupifupi 5,000). Koma Iye anati kwa ophunzira ake, “Akhazikeni pansi mʼmagulu a anthu pafupifupi makumi asanu.”
15 I učinili tak, a posadili se všickni.
Ophunzira ake anachita zomwezo ndipo aliyense anakhala pansi.
16 A vzav těch pět chlebů a ty dvě rybě, vzhlédl v nebe, a dobrořečil jim, i lámal, a rozdával učedlníkům, aby kladli před zástup.
Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri zija anayangʼana kumwamba, nayamika ndipo anazigawa. Kenaka anazipereka kwa ophunzira ake kuti azipereke kwa anthu.
17 I jedli, a nasyceni jsou všickni. A sebráno jest, což jim bylo ostalo drobtů, dvanácte košů.
Onse anadya nakhuta, ndipo ophunzira ake anatolera madengu khumi ndi awiri odzaza ndi nyenyeswa zomwe zinatsala.
18 I stalo se, když se on modlil obzvláštně, že byli s ním učedlníci. I otázal se jich, řka: Kým mne praví býti zástupové?
Nthawi ina pamene Yesu amapemphera malo a yekha ali ndi ophunzira ake, Iye anawafunsa kuti, “Kodi anthu amati Ine ndine yani?”
19 A oni odpověděvše, řekli: Janem Křtitelem, a jiní Eliášem, jiní pak, že prorok jeden z starých vstal.
Iwo anayankha kuti, “Ena amati Yohane Mʼbatizi; ena amati Eliya; ndipo enanso amati mmodzi wa aneneri akalekale waukanso.”
20 I řekl jim: Vy pak kým mne býti pravíte? Odpověděv Petr, řekl: Krista toho Božího.
Iye anafunsa kuti, “Koma nanga inu mumati Ine ndine yani?” Petro anayankha kuti, “Mpulumutsi wolonjezedwa uja wa Mulungu.”
21 A on s pohrůžkou jim přikázal, aby toho žádnému nepravili,
Yesu anawachenjeza kwambiri kuti asawuze wina aliyense za izi.
22 Pravě: Že Syn člověka musí mnoho trpěti, a potupen býti od starších a od předních kněží i od zákonníků, a zamordován býti, a třetího dne z mrtvých vstáti.
Ndipo Iye anati, “Mwana wa Munthu ayenera kuzunzika kwambiri ndi kukanidwa ndi akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, Iye ayenera kuphedwa ndipo tsiku lachitatu adzauka kwa akufa.”
23 I pravil všechněm: Chce-li kdo přijíti za mnou, zapři sám sebe, a beř svůj kříž na každý den, a následuj mne.
Ndipo Iye anawuza onse kuti, “Ngati wina aliyense akufuna kutsata Ine, ayenera kudzikana yekha ndi kusenza mtanda wake tsiku ndi tsiku nʼkumanditsata Ine.
24 Nebo kdož bude chtíti duši svou zachovati, ztratíť ji; a kdož ztratí duši svou pro mne, tenť ji zachová,
Popeza aliyense amene akufuna kupulumutsa moyo wake adzawutaya, koma aliyense amene adzataya moyo wake chifukwa cha Ine adzawupulumutsa.
25 Nebo co jest platno člověku, by všecken svět získal, kdyby sám sebe ztratil, aneb sám sebe zmrhal?
Kodi chabwino ndi chiti kwa munthu, kupata zonse zapansi pano, koma ndi kutaya moyo wake kapena kudziwononga iye mwini?
26 Nebo kdož by se za mne styděl a za mé řeči, za tohoť se Syn člověka styděti bude, když přijde v slávě své a Otcově i svatých andělů.
Ngati wina aliyense achita nane manyazi ndi ndiponso mawu anga, Mwana wa Munthu adzachita naye manyazi pamene adzabwera mu ulemerero wake ndi mu ulemerero wa Atate ndi angelo oyera.
27 Ale pravímť vám jistě: Jsou někteří z stojících tuto, kteříž neokusí smrti, až uzří království Boží.
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti ena mwa inu amene mwayima pano simudzalawa imfa musanaone ufumu wa Mulungu.”
28 I stalo se po těch řečech, jako po osmi dnech, že vzav s sebou Petra a Jakuba a Jana, vstoupil na horu, aby se modlil.
Patatha pafupifupi masiku asanu ndi atatu Yesu atanena izi, Iye anatenga Petro, Yohane ndi Yakobo ndi kukwera ku phiri kukapemphera.
29 A když se modlil, učiněna jest tvář jeho proměněná, a oděv jeho bílý a stkvoucí.
Pamene Iye ankapemphera, maonekedwe a nkhope yake, ndi zovala zake zinawala monyezimira kwambiri.
30 A aj, dva muži mluvili s ním, a ti byli Mojžíš a Eliáš.
Anthu awiri, Mose ndi Eliya,
31 Kteříž okázavše se v slávě, vypravovali o smrti jeho, kterouž měl podstoupiti v Jeruzalémě.
anaonekera mu ulemerero opambana akuyankhulana ndi Yesu. Iwo amayankhulana za kuchoka kwake, kumene Iye anali pafupi kukakwaniritsa ku Yerusalemu.
32 Petr pak a ti, kteříž s ním byli, obtíženi byli snem, a procítivše, viděli slávu jeho a ty dva muže, ani stojí s ním.
Petro ndi anzake anali ndi tulo tambiri, koma atadzuka, iwo anaona ulemerero wake ndi anthu awiri atayima pamodzi ndi Iye.
33 I stalo se, když oni odešli od něho, řekl Petr Ježíšovi: Mistře, dobréť jest nám zde býti. Protož udělejme tři stánky, tobě jeden, a Mojžíšovi jeden, a Eliášovi jeden, nevěda, co mluví.
Pamene anthuwo ankamusiya Yesu, Petro anati kwa Iye, “Ambuye, ndi chabwino kwa ife kuti tikhale pano. Tiloleni kuti timange misasa itatu, umodzi wanu, umodzi wa Mose ndi umodzi wa Eliya.” (Iye sanadziwe chimene amayankhula).
34 A když on to mluvil, stal se oblak, i zastínil je. Báli se pak, když onino vcházeli do oblaku.
Pamene Iye ankayankhula, mtambo unaonekera ndi kuwaphimba iwo, ndipo anachita mantha pamene mtambowo unawakuta.
35 I stal se hlas z oblaku řkoucí: Tentoť jest ten Syn můj milý, toho poslouchejte.
Mawu anachokera mu mtambomo nati, “Uyu ndi Mwana wanga amene ndamusankha; mumvereni Iye.”
36 A když se ten hlas stal, nalezen jest Ježíš sám. A oni mlčeli, a nepravili žádnému v těch dnech ničeho z těch věcí, kteréž viděli.
Atamveka mawuwa, anaona kuti Yesu anali yekha. Ophunzirawo anazisunga izi mwa iwo okha ndipo sanawuze wina aliyense pa nthawiyi za zomwe iwo anaziona.
37 Stalo se pak druhého dne, když sstupovali s hory, potkal jej zástup mnohý.
Mmawa mwake, akutsika ku phiri, anthu ambiri anakumana naye.
38 A aj, muž z zástupu zvolal, řka: Mistře, prosím tebe, vzhlédni na syna mého, neboť jediného toho mám.
Munthu wina mʼgulu la anthulo anayitana kuti, “Aphunzitsi, ndikupemphani kuti muone mwana wangayu, pakuti ndi mmodzi yekhayu.
39 A aj, duch jej napadá, a on i hned křičí, a lomcuje jím slinícím se, a nesnadně odchází od něho, sápaje jím.
Chiwanda chikamugwira amafuwula mwadzidzidzi; chimamugwedeza kolimba mpaka kutuluka thovu kukamwa. Sichimusiya ndipo chikumuwononga.
40 I prosil jsem učedlníků tvých, aby jej vyvrhli, ale nemohli.
Ine ndinapempha ophunzira anu kuti achitulutse, koma alephera.”
41 I odpověděv Ježíš, řekl: Ó pokolení nevěrné a převrácené, dokudž budu u vás, a snášeti budu vás? Přiveď sem syna svého.
Yesu anayankha kuti, “Haa! Anthu osakhulupirira ndi mʼbado wokhota. Kodi Ine ndidzakhala nanu nthawi yayitali yotani ndi kukupirirani? Bweretsa mwana wako kuno.”
42 A v tom, když on přicházel, porazil jej ďábel, a lomcoval jím. I přimluvil duchu nečistému Ježíš, a uzdravil toho mládence, a navrátil jej otci jeho.
Ngakhale pamene mnyamata amabwera kwa Yesu, chiwandacho chinamugwetsa pansi ndi kumugwedeza. Koma Yesu anadzudzula mzimu woyipawo nachiritsa mwa mnyamatayo ndi kumuperekanso kwa abambo ake.
43 I děsili se všickni nad velikomocností Božskou. A když se všickni divili všem věcem, kteréž činil Ježíš, řekl učedlníkům svým:
Ndipo iwo onse anadabwa ndi ukulu wa Mulungu. Aliyense akudabwa ndi zimene Yesu anachita, Iyeyo anati kwa ophunzira ake,
44 Složte vy v uších svých řeči tyto, neboť Syn člověka bude vydán v ruce lidské.
“Tamvetsetsani zimene ndikufuna kukuwuzani: Mwana wa Munthu akupita kukaperekedwa mʼmanja mwa anthu.”
45 Ale oni nesrozuměli slovu tomu, a bylo před nimi skryto, aby nevyrozuměli jemu. A nesměli se ho otázati o tom slovu.
Koma iwo sanazindikire zimene amatanthauza. Izi zinawadabwitsa kotero sanathe kuzimvetsa ndipo anaopa kumufunsa.
46 I vznikla mezi nimi hádka o to, kdo by z nich byl největší.
Mkangano unayambika pakati pa ophunzira wa kuti wamkulu koposa akanakhala ndani mwa iwo.
47 Ježíš pak viděv přemyšlování srdce jejich, vzav dítě, postavil je podlé sebe,
Yesu podziwa maganizo awo, anatenga kamwana nakayimika pambali pake.
48 A řekl jim: Kdožkoli přijal by dítě toto ve jménu mém, mneť přijímá; a kdož by koli mne přijal, přijímá toho, kterýž mne poslal. Nebo kdožť jest nejmenší mezi všemi vámi, tenť bude veliký.
Ndipo Iye anawawuza kuti, “Aliyense wolandira bwino kamwana aka mʼdzina langa, ndiye kuti akulandiranso bwino Ine; ndipo aliyense wolandira bwino Ine, ndiye kuti akulandiranso bwino amene anandituma Ine. Pakuti amene ndi wamngʼono pakati panu, ndiye amene ali wamkulu koposa.”
49 I odpověděv Jan, řekl: Mistře, viděli jsme jednoho, an ve jménu tvém ďábly vymítá; i bránili jsme mu, proto že nechodí s námi.
Yohane anati, “Ambuye, ife tinaona munthu akutulutsa ziwanda mʼdzina lanu ndipo tinayesa kumuletsa, chifukwa iyeyo si mmodzi wa ife.”
50 I dí jemu Ježíš: Nebraňtež. Nebo kdoť není proti nám, s námiť jest.
Yesu anati, “Wosamuletsa, pakuti amene satsutsana nanu ali mbali yanu.”
51 I stalo se, když se doplnili dnové vzetí jeho zhůru, že on se na tom ustavil, aby šel do Jeruzaléma.
Nthawi itayandikira yoti Iye atengedwe kupita kumwamba, Yesu anatsimikiza zopita ku Yerusalemu,
52 I poslal posly před sebou. A oni jdouce, vešli do městečka Samaritánského, aby jemu připravili.
ndipo anatuma nthumwi kuti zitsogole. Iwo anapita mʼmudzi wa Asamariya kuti akonzekere kumulandira,
53 Ale nepřijali ho, proto že oblíčej jeho byl obrácen k jití do Jeruzaléma.
koma anthu kumeneko sanamulandire chifukwa Iye ankapita ku Yerusalemu.
54 A viděvše to učedlníci jeho Jakub a Jan, řekli: Pane, chceš-li, ať díme, aby oheň sstoupil s nebe, a spálil je, jako i Eliáš učinil?
Ophunzira awa, Yohane ndi Yakobo ataona zimenezi, anafunsa kuti, “Ambuye, kodi mukufuna ife tiyitane moto kuchokera kumwamba kuti uwawononge?”
55 Ale obrátiv se, potrestal jich, řka: Nevíte, čího jste vy duchu.
Koma Yesu anatembenuka ndi kuwadzudzula,
56 Syn zajisté člověka nepřišel zatracovati duší lidských, ale aby spasil. I odešli do jiného městečka.
ndipo iwo anapita ku mudzi wina.
57 Stalo se pak, když šli, že řekl jemu na cestě jeden: Pane, půjdu za tebou, kam se koli obrátíš.
Pamene iwo ankayenda mu msewu, munthu wina anati kwa Iye, “Inu ndikutsatirani kulikonse kumene mudzapita.”
58 I řekl jemu Ježíš: Lišky doupata mají, a ptáci nebeští hnízda, ale Syn člověka nemá, kde by hlavu sklonil.
Yesu anayankha kuti, “Nkhandwe zili ndi mapanga ake, mbalame zili ndi zisa zake, koma Mwana wa Munthu alibe malo wogonekapo mutu wake.”
59 I řekl jinému: Poď za mnou. Ale on řekl: Pane, dopusť mi prvé jíti a pochovati otce mého.
Iye anati kwa wina, “Nditsate Ine.” Koma munthuyo anayankha kuti, “Ambuye, choyamba loleni ndipite kuti ndikayike maliro a abambo anga.”
60 I dí jemu Ježíš: Nech ať mrtví pochovávají mrtvé své, ale ty jda, zvěstuj království Boží.
Yesu anati kwa iye, “Aleke akufa ayikane akufa okhaokha, koma iwe pita ukalalikire ufumu wa Mulungu.”
61 I řekl opět jiný: Půjdu za tebou, Pane, ale prvé dopusť mi, ať se rozžehnám s těmi, kteříž jsou v domě mém.
Koma winanso anati, “Ine ndidzakutsatani Ambuye; koma choyamba ndiloleni ndibwerere kuti ndikatsanzikane nalo banja langa.”
62 Řekl jemu Ježíš: Žádný, kdož vztáhna ruku svou k pluhu, ohlídal by se nazpět, není způsobný k království Božímu.
Yesu anayankha kuti, “Munthu amene akulima ndi khasu lokokedwa nʼkumayangʼana mʼmbuyo, si woyenera kugwira ntchito mu ufumu wa Mulungu.”

< Lukáš 9 >