< Skutky Apoštolů 2 >

1 A když přišel den padesátý, byli všickni jednomyslně spolu.
Litafika tsiku la chikondwerero cha Pentekosite, onse anali pamodzi.
2 I stal se rychle zvuk s nebe, jako valícího se větru prudkého, a naplnil všecken dům, kdež seděli.
Mwadzidzidzi kunamveka mkokomo kuchokera kumwamba ngati wa mphepo yamphamvu, ndipo inadzaza nyumba yonse imene amakhala.
3 I ukázali se jim rozdělení jazykové jako oheň, kterýž posadil se na každém z nich.
Iwo anaona zinthu zokhala ngati malilime amoto ogawikana ndipo anakhala pa aliyense wa iwo.
4 I naplněni jsou všickni Duchem svatým, a počali mluviti jinými jazyky, jakž ten Duch dával jim vymlouvati.
Ndipo onse anadzazidwa ndi Mzimu Woyera, nayamba kuyankhula mu ziyankhulo zina, monga Mzimu Woyerayo anawayankhulitsa.
5 Byli pak v Jeruzalémě přebývající Židé, muži nábožní, ze všelikého národu, kterýž pod nebem jest.
Ayuda woopa Mulungu ochokera ku mayiko onse a dziko lapansi ankakhala mu Yerusalemu nthawi imeneyi.
6 A když se stal ten hlas, sešlo se množství, a užasli se, že je slyšel jeden každý, ani mluví přirozeným jazykem jeho.
Utamveka mkokomo uja, gulu la anthu linasonkhana. Anthuwo anadabwa chifukwa aliyense anawamva atumwiwo akuyankhula ziyankhulo zosiyanasiyana.
7 I děsili se všickni, a divili, řkouce jedni k druhým: Aj, zdaliž nejsou tito všickni, kteříž mluví, Galilejští?
Mothedwa nzeru anafunsana kuti, “Kodi anthu onse amene akuyankhulawa si Agalileya?
8 A kterak my slyšíme jeden každý jazyk náš, v kterémž jsme se zrodili?
Nanga bwanji aliyense wa ife akuwamva iwo mu chinenero cha kwawo?
9 Partští, a Médští, a Elamitští, a kteříž přebýváme v Mezopotamii, v Židovstvu a v Kappadocii, v Pontu a v Azii,
Apanti, Amedi ndi Aelami; okhala ku Mesopotamiya, ku Yudeya ndi ku Kapadokiya, ku Ponto ndi ku Asiya,
10 V Frygii a v Pamfylii, v Egyptě a v krajinách Libye, kteráž jest vedlé Cyrénu, a příchozí Římané, Židé, i v nově na víru obrácení,
ku Frugiya ndi Pamfiliya, ku Igupto ndi ku madera a ku Libiya kufupi ndi ku Kurene; alendo ochokera ku Roma,
11 Kretští i Arabští, slyšíme je, ani mluví jazyky našimi veliké věci Boží.
Ayuda ndi otsatira chipembedzo cha Chiyuda onse pamodzi; Akrete ndi Aarabu, ife tonse tikuwamva akuyankhula za ntchito zodabwitsa za Mulungu mu ziyankhulo zathu.”
12 I děsili se všickni a divili, jeden k druhému řkouce: I což toto bude?
Modabwa ndi mothedwa nzeru anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Zimenezi zikutanthauzanji?”
13 Jiní pak posmívajíce se, pravili: Mstem se zpili tito.
Koma ena anawaseka nati, “Aledzera vinyo watsopano.”
14 A stoje Petr s jedenácti, pozdvihl hlasu svého, a promluvil k nim: Muži Židé, a všickni, kteříž bydlíte v Jeruzalémě, toto vám známo buď, a ušima pozorujte slov mých.
Koma Petro anayimirira pamodzi ndi atumwi khumi ndi mmodziwo ndipo anakweza mawu ake nayankhula kwa gulu la anthu nati: “Ayuda anzanga, ndi nonse amene muli mu Yerusalemu, mvetsetsani izi ndipo tcherani khutu ku zimene ndikunena.
15 Jistě nejsou tito, jakž vy se domníváte, zpilí, poněvadž jest teprv třetí hodina na den.
Kunena zoona, anthu awa sanaledzere ayi, monga momwe mukuganizira, pakuti ino ndi 9 koloko mmawa!
16 Ale totoť jest, což jest předpovědíno skrze proroka Joele:
Koma izi ndi zimene ananena Mneneri Yoweli kuti:
17 A budeť v posledních dnech, (dí Bůh, ) vyleji z Ducha svého na všeliké tělo, a prorokovati budou synové vaši, i dcery vaše, a mládenci vaši vidění vídati budou, a starci vaši sny míti budou.
“‘Mulungu akuti, mʼmasiku otsiriza ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi aakazi adzanenera, anyamata anu adzaona masomphenya, nkhalamba zanu zidzalota maloto.
18 A zajisté na služebníky a na služebnice své v těch dnech vyleji z Ducha svého, a budou prorokovati.
Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo, ndipo iwo adzanenera.
19 A ukáži zázraky na nebi svrchu, a znamení na zemi dole, krev a oheň a páru dymovou.
Ndipo ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi zizindikiro pa dziko lapansi pano, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
20 Slunce obrátí se v temnost, a měsíc v krev, prvé než přijde ten den Páně veliký a zjevný.
Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi laulemerero la Ambuye.
21 A staneť se, že každý, kdožkoli vzýval by jméno Páně, spasen bude.
Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.’
22 Muži Izraelští, slyšte slova tato: Ježíše toho Nazaretského, muže od Boha zveličeného mezi vámi mocmi a zázraky a znameními, kteréž činil skrze něho Bůh u prostřed vás, jakož i vy sami víte,
“Inu Aisraeli mverani mawu awa; Yesu wa ku Nazareti anali munthu amene anaperekedwa kwa inu ndi Mulungu. Ndipo Mulungu anakutsimikizirani zimenezi ndi zamphamvu, zodabwitsa ndi zizindikiro zimene anachita mwa Iye pakati panu, monga inu mukudziwa.
23 Toho vydaného z uložené rady a předzvědění Božího vzavše, a skrze ruce nešlechetných ukřižovavše, zamordovali jste.
Yesu ameneyu anaperekedwa kwa inu mwa kufuna ndi kudziwiratu kwa Mulungu; ndipo inu mothandizidwa ndi anthu oyipa, munamupha Iye pomupachika pa mtanda.
24 Jehož Bůh vzkřísil, zprostiv bolestí smrti, jakož nebylo možné jemu držánu býti od ní.
Koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa, kumumasula Iye ku zowawa za imfa, chifukwa kunali kosatheka kuti agwiridwe ndi imfa.
25 Nebo David praví o něm: Spatřoval jsem Pána před sebou vždycky; nebo jest mi po pravici, abych se nepohnul.
Pakuti Davide ananena za Iye kuti, “‘Ndinaona Ambuye pamaso panga nthawi zonse. Chifukwa Iye ali kudzanja langa lamanja, Ine sindidzagwedezeka.
26 Protož rozveselilo se srdce mé, a zplésal jazyk můj, nýbrž i tělo mé odpočine v naději.
Chifukwa chake mtima wanga ndi wokondwa ndipo lilime langa likukondwera; thupi langanso lidzakhala ndi chiyembekezo.
27 Nebo nenecháš duše mé v pekle, aniž dáš viděti svatému svému porušení. (Hadēs g86)
Chifukwa simudzasiya moyo wanga kumalo a anthu akufa, ku manda, kapena kulekerera Woyerayo kuti awole. (Hadēs g86)
28 Známé jsi mi učinil cesty života, a naplníš mne utěšením před oblíčejem svým.
Inu munandidziwitsa ine njira zamoyo; Inu mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu.’
29 Muži bratří, sluší směle mluviti k vám o patriarchovi Davidovi, že i umřel, i pochován jest, i hrob jeho jest u nás až do dnešního dne.
“Abale, ine ndikuwuzani motsimikiza kuti kholo lathu Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda, ndipo manda ake alipo lero lino.
30 Prorok tedy byv, a věděv, že přísahou zavázal se jemu Bůh, že z plodu ledví jeho podlé těla vzbudí Krista, a posadí na stolici jeho,
Koma iye anali mneneri ndipo anadziwa kuti Mulungu analonjeza ndi lumbiro kuti adzayika mmodzi wa zidzukulu zake pa mpando waufumu.
31 To předzvěděv, mluvil o vzkříšení Kristovu, že není opuštěna duše jeho v pekle, ani tělo jeho vidělo porušení. (Hadēs g86)
Davide ataoneratu zimene zinali mʼtsogolo anayankhula za kuuka kwa Khristu, kuti Iye sanasiyidwe mʼmanda, ndipo thupi lake silinawole. (Hadēs g86)
32 Toho Ježíše vzkřísil Bůh, jehož my všickni svědkové jsme.
Mulungu wamuukitsa Yesu ameneyu, ndipo ife ndife mboni za zimenezi.
33 Protož pravicí Boží jsa zvýšen, a vzav zaslíbení Ducha svatého od Otce, vylil to, což vy nyní vidíte a slyšíte.
Khristu anakwezedwa kukhala kudzanja lamanja la Mulungu, nalandira Mzimu Woyera amene Atate anamulonjeza, ndipo watipatsa ife zimene mukuona ndi kumvazi.
34 Neboť David nevstoupil v nebe, ale on praví: Řekl Pán Pánu mému: Seď na pravici mé,
Pakuti si Davide anakwera kumwamba koma iye akuti, “‘Ambuye anawuza Ambuye anga kuti: Khala kudzanja langa lamanja
35 Dokudž nepoložím nepřátel tvých za podnože noh tvých.
mpaka nditasandutsa adani ako kukhala chopondapo mapazi ako.’
36 Věziž tedy jistotně všecken dům Izraelský, žeť Bůh i Pánem ho učinil i Kristem, toho Ježíše, kteréhož jste vy ukřižovali.
“Nʼchifukwa chake, Aisraeli onse adziwe ndithu kuti, Yesu amene inu munamupachika, Mulungu wamuyika kukhala Ambuye ndiponso Mpulumutsi.”
37 To slyševše, zkormouceni jsou v srdci, a řekli Petrovi a jiným apoštolům: Což máme činiti, muži bratří?
Anthu atamva zimenezi, anatsutsika kwambiri mu mtima ndipo anati kwa Petro ndi atumwi enawo, “Abale, kodi ife tichite chiyani?”
38 Tedy Petr řekl jim: Pokání čiňte, a pokřti se jeden každý z vás ve jménu Ježíše Krista na odpuštění hříchů, a přijmete dar Ducha svatého.
Petro anawayankha kuti, “Lapani ndipo mubatizidwe aliyense wa inu, mʼdzina la Yesu Khristu kuti machimo anu akhululukidwe. Ndipo mudzalandira mphatso ya Mzimu Woyera.
39 Vámť zajisté zaslíbení to svědčí a synům vašim, i všechněm, kteříž daleko jsou, kterýchžkoli povolal by Pán Bůh náš.
Pakuti lonjezoli ndi lanu ndi ana anu ndiponso la onse amene ali kutali, ndi iwo onse amene Ambuye Mulungu wathu adzawayitane.”
40 A jinými slovy mnohými osvědčoval a napomínal, řka: Oddělte se od pokolení toho zlého.
Petro anawachenjeza ndi mawu ena ambiri, ndipo anawadandaulira iwo kuti, “Mudzipulumutse ku mʼbado owonongeka uno.”
41 Tedy ti, kteříž ochotně přijali slova jeho, pokřtěni jsou, a připojilo se v ten den duší okolo tří tisíců.
Iwo amene anawulandira uthenga wake anabatizidwa ndipo tsiku lomwelo miyoyo pafupifupi 3,000 inawonjezedwa ku gulu lawo.
42 I zůstávali v učení apoštolském, a v společnosti, a v lámání chleba, a na modlitbách.
Iwo ankasonkhana pamodzi kuphunzitsidwa ndi atumwi, pachiyanjano, pachakudya ndi popemphera.
43 I přišla na všelikou duši bázeň, a mnozí divové a zázrakové dáli se skrze apoštoly.
Aliyense ankachita mantha chifukwa cha zodabwitsa ndi zizindikiro zambiri zimene atumwi ankachita.
44 Všickni pak věřící byli pospolu, a měli všecky věci obecné.
Okhulupirira onse anali pamodzi ndipo aliyense ankapereka zinthu zake kuti zikhale za onse.
45 A prodávali vládařství a statky, a dělili mezi všecky, jakž komu potřebí bylo.
Ankagulitsa minda yawo ndi katundu wawo, ndi kugawira kwa aliyense molingana ndi zosowa zake.
46 A na každý den trvajíce jednomyslně v chrámě, a lámajíce po domích chléb, přijímali pokrm s potěšením a sprostností srdce,
Tsiku ndi tsiku ankasonkhana pamodzi pa bwalo la pa Nyumba ya Mulungu. Ankadya pamodzi mʼnyumba zawo mwasangala ndi mtima woona.
47 Chválíce Boha, a milost majíce u všeho lidu. Pán pak přidával církvi na každý den těch, kteříž by spaseni byli.
Ankayamika Mulungu ndipo anthu onse ankawakomera mtima. Ndipo tsiku ndi tsiku Ambuye ankawonjezera ena pa chiwerengero cha olandira chipulumutso.

< Skutky Apoštolů 2 >