< 使徒行傳 2 >

1 五旬節日一到,眾人都聚集一處。
Litafika tsiku la chikondwerero cha Pentekosite, onse anali pamodzi.
2 忽然,從天上來了一陣響聲,好像暴風颳來,充滿了他們所在的全座房屋。
Mwadzidzidzi kunamveka mkokomo kuchokera kumwamba ngati wa mphepo yamphamvu, ndipo inadzaza nyumba yonse imene amakhala.
3 有些散開好像火的舌頭,停留在他們每人頭上,
Iwo anaona zinthu zokhala ngati malilime amoto ogawikana ndipo anakhala pa aliyense wa iwo.
4 眾人都充滿了聖神,照聖神賜給他們的話,說起外方話來。
Ndipo onse anadzazidwa ndi Mzimu Woyera, nayamba kuyankhula mu ziyankhulo zina, monga Mzimu Woyerayo anawayankhulitsa.
5 那時,居住在耶路撒冷的,有從天下各國來的虔誠的猶太人。
Ayuda woopa Mulungu ochokera ku mayiko onse a dziko lapansi ankakhala mu Yerusalemu nthawi imeneyi.
6 這聲音一響,就聚來了許多人,都倉皇失措,因為人人都聽見他們說自己的方言。
Utamveka mkokomo uja, gulu la anthu linasonkhana. Anthuwo anadabwa chifukwa aliyense anawamva atumwiwo akuyankhula ziyankhulo zosiyanasiyana.
7 他們驚訝奇怪地說:「看,這些說話的不都是加里肋亞人嗎﹖
Mothedwa nzeru anafunsana kuti, “Kodi anthu onse amene akuyankhulawa si Agalileya?
8 怎麼我們每人聽見他們說我們出生地的方言呢﹖
Nanga bwanji aliyense wa ife akuwamva iwo mu chinenero cha kwawo?
9 我們中有帕提雅人、瑪待人、厄藍人和居住在美索不達米亞、猶太及卡帕多細雅、本都並亞細亞、
Apanti, Amedi ndi Aelami; okhala ku Mesopotamiya, ku Yudeya ndi ku Kapadokiya, ku Ponto ndi ku Asiya,
10 夫黎基雅和旁非里雅、埃及並靠近基勒乃的利比亞一帶的人,以及僑居的羅馬人、
ku Frugiya ndi Pamfiliya, ku Igupto ndi ku madera a ku Libiya kufupi ndi ku Kurene; alendo ochokera ku Roma,
11 猶太人和歸依猶太教的人、克里特人和阿剌伯人,怎麼我們都聽見他們用我們的話,講論天主的奇事呢﹖」
Ayuda ndi otsatira chipembedzo cha Chiyuda onse pamodzi; Akrete ndi Aarabu, ife tonse tikuwamva akuyankhula za ntchito zodabwitsa za Mulungu mu ziyankhulo zathu.”
12 眾人都驚訝猶豫,彼此說:「這是什麼事﹖」
Modabwa ndi mothedwa nzeru anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Zimenezi zikutanthauzanji?”
13 另有些人卻譏笑說:「他們喝醉了酒!」
Koma ena anawaseka nati, “Aledzera vinyo watsopano.”
14 伯多祿就同十一位宗徒站起來,高聲向他們說:「猶太人和所有居住在耶路撒冷的人!請你們留意,側耳靜聽我的話!
Koma Petro anayimirira pamodzi ndi atumwi khumi ndi mmodziwo ndipo anakweza mawu ake nayankhula kwa gulu la anthu nati: “Ayuda anzanga, ndi nonse amene muli mu Yerusalemu, mvetsetsani izi ndipo tcherani khutu ku zimene ndikunena.
15 這些人並不像你們所設想的喝醉了,因為纔是白天第三時辰;
Kunena zoona, anthu awa sanaledzere ayi, monga momwe mukuganizira, pakuti ino ndi 9 koloko mmawa!
16 反而這是藉岳厄爾先知所預言的:
Koma izi ndi zimene ananena Mneneri Yoweli kuti:
17 『到末日──天主說──我要將我的神傾住在所有有血肉的人身上,你們的兒子和女兒都要說預言,青年人要見異像,老年人要看夢境。
“‘Mulungu akuti, mʼmasiku otsiriza ndidzakhuthulira Mzimu wanga pa anthu onse. Ana anu aamuna ndi aakazi adzanenera, anyamata anu adzaona masomphenya, nkhalamba zanu zidzalota maloto.
18 甚至在那些日子裏,連在我的僕人和我的婢女身上,我也要傾住我的神;他們要講預言。
Ngakhalenso pa antchito anga aamuna ndi aakazi, ndidzakhuthulira Mzimu wanga masiku amenewo, ndipo iwo adzanenera.
19 我要在天上顯示奇蹟,在下地顯示徵兆:血、火和煙氣。
Ndipo ndidzaonetsa zodabwitsa mlengalenga ndi zizindikiro pa dziko lapansi pano, ndizo magazi, moto ndi utsi watolotolo.
20 在上主的偉大和顯赫的日子來臨以前,太陽要變成昏暗,月亮要變成血紅。
Dzuwa lidzadetsedwa ndipo mwezi udzaoneka ngati magazi lisanafike tsiku lalikulu ndi laulemerero la Ambuye.
21 將來,凡呼號上主名字的人,必然獲救。』
Ndipo aliyense amene adzayitana pa dzina la Ambuye adzapulumuka.’
22 諸位以色列人!請聽這些話:納匝肋人耶穌是天主用德能、奇蹟和徵兆──即天主藉他在你們中所行的,一如你們所知道的──給你們證明了的人。
“Inu Aisraeli mverani mawu awa; Yesu wa ku Nazareti anali munthu amene anaperekedwa kwa inu ndi Mulungu. Ndipo Mulungu anakutsimikizirani zimenezi ndi zamphamvu, zodabwitsa ndi zizindikiro zimene anachita mwa Iye pakati panu, monga inu mukudziwa.
23 他照天主已定的計劃和預知,被交付了;你們藉著不法者的手,釘他在十字架上,殺死了他;
Yesu ameneyu anaperekedwa kwa inu mwa kufuna ndi kudziwiratu kwa Mulungu; ndipo inu mothandizidwa ndi anthu oyipa, munamupha Iye pomupachika pa mtanda.
24 天主卻解除了他死亡的苦痛,使他復活了,因為他不能受死亡的控制,
Koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa, kumumasula Iye ku zowawa za imfa, chifukwa kunali kosatheka kuti agwiridwe ndi imfa.
25 因為達味指著他說:『我常將上主置於我眼前;我決不動搖,因他在我右邊。
Pakuti Davide ananena za Iye kuti, “‘Ndinaona Ambuye pamaso panga nthawi zonse. Chifukwa Iye ali kudzanja langa lamanja, Ine sindidzagwedezeka.
26 因此,我心歡樂,我的舌愉快,連我的肉身也要安息於希望中,
Chifukwa chake mtima wanga ndi wokondwa ndipo lilime langa likukondwera; thupi langanso lidzakhala ndi chiyembekezo.
27 因為你決不會將我的靈魂遺棄在陰府,也不會讓你的聖者見到腐朽。 (Hadēs g86)
Chifukwa simudzasiya moyo wanga kumalo a anthu akufa, ku manda, kapena kulekerera Woyerayo kuti awole. (Hadēs g86)
28 你要將生命的道路指示給我,要在你面前用喜樂充滿我。』
Inu munandidziwitsa ine njira zamoyo; Inu mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu.’
29 諸位仁人弟兄!容我坦白對你們講論聖祖達味的事罷!他死了,也埋葬了,他的墳墓直到今天還在我們這裏。
“Abale, ine ndikuwuzani motsimikiza kuti kholo lathu Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda, ndipo manda ake alipo lero lino.
30 他既是先知,也知道天主曾以誓詞對他起了誓,要從他的子嗣中立一位來坐他的御座。
Koma iye anali mneneri ndipo anadziwa kuti Mulungu analonjeza ndi lumbiro kuti adzayika mmodzi wa zidzukulu zake pa mpando waufumu.
31 他既預見了,就論及默西亞的復活說:『他沒有被遺棄在陰府,他的肉身也沒有見到腐朽。』 (Hadēs g86)
Davide ataoneratu zimene zinali mʼtsogolo anayankhula za kuuka kwa Khristu, kuti Iye sanasiyidwe mʼmanda, ndipo thupi lake silinawole. (Hadēs g86)
32 這位耶穌,天主使他復活了,我們都是他的見證人。
Mulungu wamuukitsa Yesu ameneyu, ndipo ife ndife mboni za zimenezi.
33 他被舉揚到天主的右邊,由父領受了所恩許的聖神;你們現今所見所聞的,就是他所傾注的聖神。
Khristu anakwezedwa kukhala kudzanja lamanja la Mulungu, nalandira Mzimu Woyera amene Atate anamulonjeza, ndipo watipatsa ife zimene mukuona ndi kumvazi.
34 達味本來沒有升到天上,但是他卻說:『上主對吾主說:你坐在我右邊,
Pakuti si Davide anakwera kumwamba koma iye akuti, “‘Ambuye anawuza Ambuye anga kuti: Khala kudzanja langa lamanja
35 等我使你的仇敵,變作你腳的踏板。』
mpaka nditasandutsa adani ako kukhala chopondapo mapazi ako.’
36 所以,以色列全家應確切知道:天主已把你們所釘死的這位耶穌,立為主,立為默西亞了。」
“Nʼchifukwa chake, Aisraeli onse adziwe ndithu kuti, Yesu amene inu munamupachika, Mulungu wamuyika kukhala Ambuye ndiponso Mpulumutsi.”
37 他們一聽見這些話,就心中刺痛,遂向伯多祿和其他宗徒說:「諸位仁人弟兄!我們該作什麼﹖」
Anthu atamva zimenezi, anatsutsika kwambiri mu mtima ndipo anati kwa Petro ndi atumwi enawo, “Abale, kodi ife tichite chiyani?”
38 伯多祿便對他們說:「你們悔改罷!你們要以耶穌基督的名字受洗,好赦免你們的罪過,並領受聖神的恩惠。
Petro anawayankha kuti, “Lapani ndipo mubatizidwe aliyense wa inu, mʼdzina la Yesu Khristu kuti machimo anu akhululukidwe. Ndipo mudzalandira mphatso ya Mzimu Woyera.
39 因為這恩許就是為了你們和你們的子女,以及一切遠方的人,因為都是我們的上主天主所召叫的。」
Pakuti lonjezoli ndi lanu ndi ana anu ndiponso la onse amene ali kutali, ndi iwo onse amene Ambuye Mulungu wathu adzawayitane.”
40 他還講了很多別的作證的話,並勸他們說:「你們應救自己脫離這邪惡的世代。」
Petro anawachenjeza ndi mawu ena ambiri, ndipo anawadandaulira iwo kuti, “Mudzipulumutse ku mʼbado owonongeka uno.”
41 於是,凡接受他的話的人,都受了洗;在那一天約增添了三千人。
Iwo amene anawulandira uthenga wake anabatizidwa ndipo tsiku lomwelo miyoyo pafupifupi 3,000 inawonjezedwa ku gulu lawo.
42 他們專心聽取宗徒的訓誨,時常團聚,擘餅,祈禱。
Iwo ankasonkhana pamodzi kuphunzitsidwa ndi atumwi, pachiyanjano, pachakudya ndi popemphera.
43 因為宗徒顯了許多奇蹟異事,每人都懷著敬畏之情。
Aliyense ankachita mantha chifukwa cha zodabwitsa ndi zizindikiro zambiri zimene atumwi ankachita.
44 凡信了的人,常齊集一處,一切所有皆歸公用。
Okhulupirira onse anali pamodzi ndipo aliyense ankapereka zinthu zake kuti zikhale za onse.
45 他們把產業和財物變賣,按照每人的需要分配。
Ankagulitsa minda yawo ndi katundu wawo, ndi kugawira kwa aliyense molingana ndi zosowa zake.
46 每天都成群結隊地前往聖殿,也挨戶擘餅,懷著歡樂和誠實的心一起進食。
Tsiku ndi tsiku ankasonkhana pamodzi pa bwalo la pa Nyumba ya Mulungu. Ankadya pamodzi mʼnyumba zawo mwasangala ndi mtima woona.
47 他們常讚頌天主,也獲得了全民眾的愛戴;上主天天使那些得救的人加入會眾。
Ankayamika Mulungu ndipo anthu onse ankawakomera mtima. Ndipo tsiku ndi tsiku Ambuye ankawonjezera ena pa chiwerengero cha olandira chipulumutso.

< 使徒行傳 2 >