< Zefaniya 3 >

1 Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza, owukira ndi odetsedwa!
Běda městu tomuto hltavému a poškvrněnému a utiskujícímu.
2 Sumvera aliyense, sulandira chidzudzulo. Sumadalira Yehova, suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.
Neposlouchá hlasu, aniž přijímá kázně; v Hospodina nedoufá, k Bohu svému nepřibližuje se.
3 Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma, olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo, zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.
Knížata jeho jsou u prostřed něho lvové řvoucí, soudcové jeho vlci večerní, nehryzou kostí až do rána.
4 Aneneri ake ndi odzikuza; anthu achinyengo. Ansembe ake amadetsa malo opatulika ndipo amaphwanya lamulo.
Proroci jeho kvapní, muži velmi nešlechetní; kněží jeho poškvrňují věci svaté, natahují zákona.
5 Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama; Iye salakwa. Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama, ndipo tsiku lililonse salephera, komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.
Hospodin spravedlivý u prostřed něho jest, nelibuje nepravosti, každého dne soud svůj vynáší na světlo bez přestání, a však nešlechetník neumí se styděti.
6 “Ndachotseratu mitundu ya anthu; ndagwetsa malinga awo. Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo, popanda aliyense wodutsa. Mizinda yawo yawonongedwa; palibe aliyense adzatsalemo.
Vyplénil jsem národy, zpustli zámkové jejich, v pustinu obrátil jsem ulice jejich, tak že žádný přes ně nechodí; zpustla města jejich, tak že není člověka, není žádného obyvatele.
7 Ndinati, ‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa ndi kumvera kudzudzula kwanga!’ Ndipo sindidzawononga nyumba zawo, kapena kuwalanganso. Koma iwo anali okonzeka kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.
Řekl jsem: Jistotně báti se mne budeš, přijmeš kázeň, aby nebyl vypléněn příbytek tvůj tím, čím jsem tě navštíviti chtěl. Ale ráno vstanouce, porušují všecky snažnosti své.
8 Choncho mundidikire,” akutero Yehova, “chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni. Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu, kusonkhanitsa maufumu ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo; mkwiyo wanga wonse woopsa. Dziko lonse lidzatenthedwa ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.
Protož očekávejtež na mne, praví Hospodin, do dne toho, v kterémž povstanu k loupeži. Nebo soud můj jest, abych sebral národy, shromáždil království, abych vylil na ně rozhněvání své a všecku prchlivost hněvu svého; ohněm zajisté horlivosti mé sehlcena bude všecka tato země.
9 “Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova ndi kumutumikira Iye pamodzi.
Tehdáž zajisté způsobím národům rty čisté, jimiž by vzývali všickni jméno Hospodinovo, a sloužili jemu jedním ramenem.
10 Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi anthu anga ondipembedza, omwazikana, adzandibweretsera zopereka.
Ti, kteříž jsou za řekami Mouřenínské země, koříce se mi, se dcerou rozptýlených mých dary mi přinesou.
11 Tsiku limenelo simudzachita manyazi chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira, popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo. Simudzakhalanso odzikuza mʼphiri langa lopatulika.
V ten den nebudeš se hanbiti za žádné skutky své, jichž jsi se dopustil proti mně; nebo tehdáž odejmu z prostředku tvého ty, kteříž pléší v důstojnosti tvé, a nebudeš se více vyvyšovati na hoře svatosti mé.
12 Koma ndidzasiya pakati panu anthu ofatsa ndi odzichepetsa, amene amadalira dzina la Yehova.
A pozůstavím u prostřed tebe lid chudý a nuzný, i budou doufati ve jménu Hospodinovu.
13 Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika; sadzayankhulanso zonama, ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo. Adzadya ndi kugona ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”
Ostatkové Izraele neučiní nepravosti, aniž mluviti budou lži, aniž se nalezne v ústech jejich jazyk lstivý, ale pásti se budou a odpočívati, a nebude žádného, kdo by je přestrašil.
14 Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni; fuwula mokweza, iwe Israeli! Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
Prozpěvuj, dcero Sionská, prokřikujte, Izraelští, vesel se a plésej vším srdcem, dcero Jeruzalémská,
15 Yehova wachotsa chilango chako, wabweza mdani wako. Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako; sudzaopanso chilichonse.
Že odjal Hospodin soudy tvé, odklidil nepřítele tvého. Král Izraelský Hospodin jest u prostřed tebe, nebudeš se báti více zlého.
16 Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti, “Usaope, iwe Ziyoni; usafowoke.
V ten den bude řečeno Jeruzalému: Neboj se, a Sionu: Nechť nemdlejí ruce tvé.
17 Yehova Mulungu wako ali pakati pako, ali ndi mphamvu yopulumutsa. Adzakondwera kwambiri mwa iwe, adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake, adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”
Hospodin Bůh tvůj u prostřed tebe mocný zachová tě, radovati se bude z tebe velice, přestane na milování svém tebe, plésati bude nad tebou s prozpěvováním, řka:
18 “Ndidzakuchotserani zowawa za pa zikondwerero zoyikika; nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
Toužící po Jeruzalému zase sberu, z tebeť jsou, bolestící pro břímě pohanění vzložené na tebe.
19 Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi onse amene anakuponderezani; ndidzapulumutsa olumala ndi kusonkhanitsa amene anamwazika. Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
Aj, já konec učiním všechněm, kteříž tě trápiti budou v ten čas, a zachovám kulhavou, a zahnanou shromáždím; nýbrž způsobím jim chválu a jméno po vší zemi, v níž pohanění nesli.
20 Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani; pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu. Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu inu mukuona,” akutero Yehova.
V ten čas přivedu vás, v ten čas, pravím, shromáždím vás; nebo dám vám jméno a chválu mezi všemi národy země, když zase přivedu zajaté vaše před očima vašima, dí Hospodin.

< Zefaniya 3 >