< Zekariya 9 >

1 Mawu a Yehova odzudzula dziko la Hadiraki ndi mzinda wa Damasiko pakuti maso a anthu ndiponso mafuko onse a Israeli ali pa Yehova—
KA wanana o ka olelo a Iehova i ka aina o Haderaka, A o Damaseko kona wahi o hoomaha ai; No ka mea, ua kau pono ia ka maka o na kanaka, a me ka ohana a pau o ka Iseraela maluna o Iehova:
2 ndiponso mzinda wa Hamati, umene ukuchita malire ndi dzikoli, komanso pa Turo ndi Sidoni, ngakhale kuti iwo ndi anzeru kwambiri.
A o Hamata hoi kona palena; O Turo hoi, a me Zidona, no ka mea, ua naauao loa ia.
3 Ndipo Turo anadzimangira linga; wadziwunjikira siliva ngati fumbi, ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu.
A kukulu iho la o Turo i pakaua nona, A ahu iho la i ke kala e like me ka lepo, A me ke gula e like me ka naele o na alanui.
4 Taonani Ambuye adzamulanda chuma chakecho ndi kuwononga mphamvu zake mʼnyanja, ndipo adzapserera ndi moto.
Aia hoi, na ka Haku ia e hookuke aku, A e hoolei aku i kona waiwai iloko o ke kai; A e hoopauia auanei oia i ke ahi.
5 Mzinda wa Asikeloni udzaona zimenezi, nʼkuchita mantha; Gaza adzanjenjemera ndi ululu, chimodzimodzinso Ekroni, chifukwa chiyembekezo chake chidzatheratu. Mfumu ya ku Gaza idzaphedwa ndipo Asikeloni adzakhala opanda anthu.
E ike auanei o Asekelona me ka makau; O Gaza hoi, a e haalulu nui loa ia; A me Ekerona; no ka mea, e poho auanei kona manaolana; E make ke alii o Gaza, A e kanaka ole auanei o Asekelona.
6 Mu Asidodi mudzakhala mlendo, ndipo ndidzathetsa kunyada kwa Afilisti.
A e noho ka malihini ma Asedoda, A e hooki iho no wau i ke kiekie o ka poe Pilisetia.
7 Ndidzachotsa nyama ya magazi mʼkamwa mwawo, chakudya choletsedwa mʼmano mwawo. Amene atsala adzakhala anthu a Mulungu wathu, adzasanduka atsogoleri mu Yuda, ndipo Ekroni adzakhala ngati Ayebusi.
E lawe aku hoi au i kona koko mailoko mai o kona waha, A me kona mau mea hoopailua mai o kona mau niho. Aka, o ka mea i waihoia, no ko kakou Akua ia, E like auanei ia me ka lunaaina, ma ka Iuda, A o Ekerona hoi me he Iebusi la:
8 Koma Ine ndidzalondera Nyumba yanga ndi kuyiteteza kwa ankhondo osakaza. Palibenso mdani amene adzagonjetse anthu anga, pakuti tsopano ndikuwayangʼanira.
E hoomoana no wau a puni ka hale o'u, no ka poe kaua, I ko lakou hele ae ana a i ka hoi mai ana; Aole hoi e puka hou ae kekahi alii hooluhi iwaena o lakou; No ka mea, ua ike no ka'u mau maka.
9 Sangalala kwambiri, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni! Fuwula, mwana wamkazi wa Yerusalemu! Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe, yolungama ndi yogonjetsa adani, yodzichepetsa ndi yokwera pa bulu, pa mwana wamphongo wa bulu.
E hauoli nui, e ke kaikamahine o Ziona, E hooho olioli, e ke kaikamahine o Ierusalema; Aia hoi, e hele mai ana kou alii iou la: He hoopono, a he hoola no kona; He akahai no, a e noho ana maluna o ka hoki, o ke keiki hoi a ka hoki.
10 Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efereimu ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu, ndipo uta wankhondo udzathyoka. Mfumuyo idzabweretsa mtendere pakati pa mitundu ya anthu. Ulamuliro wake udzayambira ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina, ndipo kuchokera ku Mtsinje (Yufurate) mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
E hoopau auanei hoi au i na halekaa mai ko Eperaima aku, A me ka lio mai Ierusalema aku: E hookiia hoi ke kakaka kaua; A e hai aku auanei oia i ka maluhia i na lahuikanaka; A mai kekahi kai a hiki i kela kai kona aupuni, A mai ka muliwai aku a hiki i na palena o ka honua.
11 Tsono kunena za iwe, chifukwa cha magazi a pangano lako ndi Ine, ndidzamasula amʼndende ako, ndidzawatulutsa mʼdzenje lopanda madzi.
O oe hoi, no ke koko o kau berita, E hookuu aku no au i kou poe paahao, Mailoko ae o ka lua meki, o kahi wai ole.
12 Bwererani ku malo anu otetezedwa, inu amʼndende achiyembekezo; ngakhale tsopano ndikulengeza kuti ndidzakubwezerani zabwino mowirikiza.
E huli ae oukou i ka pakaua, e ka poe pio manaolana; No ka mea, ke hai aku nei au i neia la, E uku palua aku no au nau.
13 Ndidzakoka Yuda monga ndimakokera uta wanga, ndipo Efereimu ndiye muvi wake. Ndidzadzutsa ana ako iwe Ziyoni, kulimbana ndi ana ako iwe Grisi, ndipo ndidzakusandutsa iwe lupanga la munthu wankhondo.
No ka mea, e lena auanei au i ka Iuda no'u, E lena hoi au i ka Eperaima e like me ka kakaka, Alaila e hoeueu ae hoi au i kau mau keiki, e Ziona; E ku e i kau mau keiki, e Iavana, A e hoolilo au ia oe e like me ka pahikaua a ke kanaka koa.
14 Pamenepo Yehova adzaonekera kwa anthu ake; mivi yake idzangʼanima ngati chingʼaningʼani. Ambuye Yehova adzaliza lipenga; ndipo adzayenda mu mkuntho wochokera kummwera,
A e ikea auanei o Iehova maluna o lakou, A e lele aku kona pua e like me ka uila; A e hookani o Iehova ka Haku i ka pu, A e hele aku no ia iloko o na makani ino o ke kukuluhema.
15 ndipo Yehova Wamphamvuzonse adzawateteza. Iwo adzawononga ndipo adzagonjetsa ndi miyala ya legeni. Adzamwa magazi ndi kubangula ngati amwa vinyo; magazi adzayenderera ngati a mʼmbale yowazira magazi pa ngodya za guwa lansembe.
Na Iehova o na kaua lakou e hoomalu mai; E ai iho lakou, a e hehi lakou maluna o na ala o ka maa; a e inu lakou, a e walaau e like me ka poe inu waina: A e hoopihaia lakou e like me na bola, a me na kihi o ke kuahu.
16 Tsiku limenelo Yehova Mulungu wawo adzawapulumutsa pakuti anthu ake ali ngati nkhosa. Adzanyezimira mʼdziko lake ngati miyala yokongola pa chipewa chaufumu.
A e malama mai o Iehova ko lakou Akua ia lakou ia la, E like me ka ohana hipa, i poe kanaka nona; No ka mea, e lilo auanei lakou i mau pohaku maikai o ka papalealii, I hookiekieia maluna o kona aina,
17 Taonani chikoka ndi kukongola kwawo! Tirigu adzasangalatsa anyamata, ndi vinyo watsopano anamwali.
Nani ka nui o kona lokomaikai! Nani hoi ka nui o kona maikai! O ka palaoa ka mea e hooulu ai i na keikikane, A o ka waina hou i na kaikamahine.

< Zekariya 9 >