< Zekariya 8 >

1 Awa ndi mawu amene Yehova Wamphamvuzonse ananena.
And the word of Jehovah of hosts came to me, saying,
2 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndikuchitira nsanje yayikulu Ziyoni. Mtima wanga ukupweteka chifukwa cha nsanje pa iyeyo.”
Thus says Jehovah of hosts: I am jealous for Zion with great jealousy, and I am jealous for her with great wrath.
3 Yehova akuti, “Ndidzabwerera ku Ziyoni ndi kukakhala ku Yerusalemu. Pamenepo Yerusalemu adzatchedwa Mzinda wa Choonadi ndipo phiri la Yehova Wamphamvuzonse lidzatchedwa Phiri Lopatulika.”
Thus says Jehovah: I am returned to Zion, and will dwell in the midst of Jerusalem. And Jerusalem shall be called The city of truth, and the mountain of Jehovah of hosts, The holy mountain.
4 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Abambo ndi amayi okalamba adzakhalanso mʼmisewu ya mu Yerusalemu, aliyense ali ndi ndodo mʼmanja mwake chifukwa cha kuchuluka kwa masiku ake.
Thus says Jehovah of hosts: There shall yet old men and old women dwell in the streets of Jerusalem, every man with his staff in his hand for very age.
5 Ndipo misewu ya mu mzindamo idzadzaza ndi anyamata ndi atsikana akusewera.”
And the streets of the city shall be full of boys and girls playing in the streets of it.
6 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ngati zikuoneka kuti nʼzosatheka kwa anthu otsala pa nthawi ino, kodi zidzakhala zosathekanso kwa Ine?” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Thus says Jehovah of hosts: If it is marvelous in the eyes of the remnant of this people in those days, should it also be marvelous in my eyes? says Jehovah of hosts.
7 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani ndidzapulumutsa anthu anga kuchokera ku mayiko a kummawa ndi kumadzulo.
Thus says Jehovah of hosts: Behold, I will save my people from the east country, and from the west country.
8 Ndidzawabweretsa kuti adzakhale mu Yerusalemu; adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, wokhulupirika ndi wolungama pakati pawo.”
And I will bring them, and they shall dwell in the midst of Jerusalem. And they shall be my people, and I will be their God, in truth and in righteousness.
9 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Inu amene tsopano mukumva mawu awa amene akuyankhula aneneri amene analipo pamene ankayika maziko a nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, ‘limbani mtima kuti mumange Nyumba ya Yehova.’
Thus says Jehovah of hosts: Let your hands be strong, ye who hear in these days these words from the mouth of the prophets who were in the day that the foundation of the house of Jehovah of hosts was laid, even the temple, that it might be built.
10 Mpaka nthawi imeneyi panalibe munthu wolandira malipiro pa ntchito kapena ndalama zolipirira nyama zogwira ntchito. Panalibe munthu amene ankadzigwirira ntchito mwamtendere chifukwa choopa adani ake, pakuti Ine ndinkawayambanitsa.
For before those days there was no wage for man, nor any wage for beast, nor was there any peace to him who went out or came in, because of the adversary. For I set all men each one against his neighbor.
11 Koma tsopano sindidzachitira otsala mwa anthu awa zomwe ndinachita kale,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
But now I will not be to the remnant of this people as in the former days, says Jehovah of hosts.
12 “Pakuti mbewu zidzamera bwino, mpesa udzabala zipatso zake, nthaka idzatulutsa zomera zake, ndi thambo lidzagwetsa mame. Ndidzapereka zonse kukhala cholowa cha otsala mwa anthu awa.
For there shall be the seed of peace. The vine shall give its fruit, and the ground shall give its increase, and the heavens shall give their dew. And I will cause the remnant of this people to inherit all these things.
13 Monga mwakhala muli chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu ina ya anthu, inu Yuda ndi Israeli, choncho ndidzakupulumutsani, ndipo mudzakhala dalitso. Musachite mantha, koma limbani mtima.”
And it shall come to pass that, as ye were a curse among the nations, O house of Judah and house of Israel, so I will save you, and ye shall be a blessing. Fear not. Let your hands be strong.
14 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Monga ndinatsimikiza mtima kubweretsa choyipa pa inu, komanso osakuchitirani chisoni pamene makolo anu anandikwiyitsa,” akutero Yehova,
For thus says Jehovah of hosts: As I thought to do evil to you, when your fathers provoked me to wrath, says Jehovah of hosts, and I did not relent,
15 “Choncho tsopano ndatsimikiza mtima kuchitiranso zabwino Yerusalemu ndi Yuda. Musachite mantha.
so again I have thought in these days to do good to Jerusalem and to the house of Judah. Fear ye not.
16 Zinthu zoti muchite ndi izi: Muziwuzana zoona zokhazokha, muziweruza moona ndi mwachilungamo mʼmabwalo anu;
These are the things that ye shall do: Speak ye every man the truth with his neighbor. Execute the judgment of truth and peace in your gates.
17 musamachitire mnzanu chiwembu, musamakonde kulumbira zonama. Zonsezi Ine ndimadana nazo,” akutero Yehova.
And let none of you devise evil in your hearts against his neighbor, and love no false oath. For all these are things that I hate, says Jehovah.
18 Yehova Wamphamvuzonse anayankhulanso nane.
And the word of Jehovah of hosts came to me, saying,
19 Ndipo ananena kuti, “Kusala zakudya kwa pa mwezi wachinayi, chisanu, chisanu ndi chiwiri ndi wakhumi, kudzakhala nthawi yachimwemwe, ya chisangalalo ndi nthawi ya madyerero chikondwerero kwa Yuda. Nʼchifukwa chake muzikonda choonadi ndi mtendere.”
Thus says Jehovah of hosts: The fast of the fourth month, and the fast of the fifth, and the fast of the seventh, and the fast of the tenth, shall be to the house of Judah, joy and gladness, and cheerful feasts. Therefore love truth and peace.
20 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu a mitundu yambiri ndi anthu okhala mʼmizinda yambiri adzabwerabe,
Thus says Jehovah of hosts: Peoples shall yet come, and the inhabitants of many cities.
21 ndipo nzika za mzinda wina zidzapita ku mzinda wina, kukanena kuti, ‘Tiyeni mwamsanga tikapemphe madalitso kwa Yehova ndi kukapembedza Yehova Wamphamvuzonse. Inenso ndikupita kumeneko.’
And the inhabitants of one city shall go to another, saying, Let us go speedily to entreat the favor of Jehovah, and to seek Jehovah of hosts. I will go also.
22 Anthu ambiri ndiponso a ku mayiko amphamvu adzabwera ku Yerusalemu kudzapembedza Yehova Wamphamvuzonse ndi kudzapempha madalitso.”
Yea, many peoples and strong nations shall come to seek Jehovah of hosts in Jerusalem, and to entreat the favor of Jehovah.
23 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Masiku amenewo anthu khumi ochokera ku mitundu ya anthu a ziyankhulo zosiyana adzagwira mkanjo wa Myuda ndi kunena kuti, ‘Tipite nawo, chifukwa tamva kuti Mulungu ali nanu.’”
Thus says Jehovah of hosts: In those days, ten men shall take hold, out of all the languages of the nations, they shall take hold of the skirt of him who is a Jew, saying, We will go with you, for we have heard that God is with you.

< Zekariya 8 >