< Zekariya 6 >

1 Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona magaleta anayi akutuluka pakati pa mapiri awiri, mapiri amkuwa.
And again I lifted up my eyes, and looked. And, behold, there came four chariots out from between two mountains, and the mountains were mountains of brass.
2 Galeta loyamba limakokedwa ndi akavalo ofiira, lachiwiri ndi akavalo akuda,
In the first chariot were red horses, and in the second chariot black horses,
3 lachitatu ndi akavalo oyera, ndipo lachinayi ndi akavalo otuwa a mawanga ofiirira, onsewa anali akavalo amphamvu kwambiri.
and in the third chariot white horses, and in the fourth chariot strong grizzled horses.
4 Ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane uja kuti, “Kodi mbuye wanga chimenechi nʼchiyani?”
Then I answered and said to the agent who talked with me, What are these, my lord?
5 Mngeloyo anandiyankha kuti, “Imeneyi ndi mizimu inayi yakumwamba, imene ikuchokera pamaso pa Ambuye wa dziko lonse.
And the agent answered and said to me, These are the four winds of heaven, which go forth from standing before the Lord of all the earth.
6 Galeta la akavalo akuda likupita ku dziko la kumpoto, galeta la akavalo oyera likutsatira, ndipo galeta la akavalo amawanga ofiirira likupita ku dziko la kummwera.”
The chariot in which are the black horses goes forth toward the north country, and the white went forth after them, and the grizzled went forth toward the south country.
7 Pamene akavalo amphamvuwa ankapita, anali ndi changu chofuna kuyendera dziko lapansi. Ndipo iye anati, “Pitani, kayendereni dziko lapansi!”
And the strong ones went forth, and sought to go that they might walk to and fro through the earth. And he said, Get you from here. Walk to and fro through the earth. So they walked to and fro through the earth.
8 Pamenepo anandiyitana, “Taona, akavalo amene apita ku dziko la kumpoto apumulitsa Mzimu wanga kumeneko.”
Then he cried to me, and spoke to me, saying, Behold, those who go toward the north country have quieted my spirit in the north country.
9 Yehova anayankhula nane kuti,
And the word of Jehovah came to me, saying,
10 “Landira mphatso kuchokera kwa anthu amene abwera ku ukapolo, Helidai, Tobiya ndi Yedaya, amene achokera ku Babuloni. Tsiku lomwelo pita ku nyumba ya Yosiya mwana wa Zefaniya.
Take from those of the captivity, even of Heldai, of Tobijah, and of Jedaiah, and come thou the same day, and go into the house of Josiah the son of Zephaniah, where they have come from Babylon.
11 Tenga siliva ndi golide upange chipewa chaufumu, ndipo uchiyike pamutu pa mkulu wa ansembe, Yoswa mwana wa Yehozadaki.
Yea, take silver and gold, and make crowns, and set them upon the head of Joshua the son of Jehozadak, the high priest.
12 Muwuze kuti zimene akunena Yehova Wamphamvuzonse ndi izi: ‘Taonani, munthu wotchedwa Nthambi ndi ameneyu, ndipo adzaphuka pomwe alipo ndi kumanga Nyumba ya Yehova.
And speak to him, saying, Thus speaks Jehovah of hosts, saying, Behold, the man whose name is the Branch. And he shall grow up out of his place, and he shall build the temple of Jehovah,
13 Ndiye amene adzamange Nyumba ya Yehova, adzalandira ulemerero waufumu ndipo adzalamulira pa mpando wake waufumu. Adzakhalanso wansembe pa mpando wake waufumu. Ndipo padzakhala mtendere.’
even he shall build the temple of Jehovah. And he shall bear the glory, and shall sit and rule upon his throne. And he shall be a priest upon his throne, and the counsel of peace shall be between them both.
14 Chipewa cha ufumucho adzachipereka kwa Helemu, Tobiya, Yedaya, ndi kwa Heni mwana wa Zefaniya, kuti chikhale chikumbutso mʼNyumba ya Yehova.
And the crowns shall be to Helem, and to Tobijah, and to Jedaiah, and to Hen the son of Zephaniah, for a memorial in the temple of Jehovah.
15 Anthu okhala kutali adzabwera kudzathandiza kumanga Nyumba ya Yehova, ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe. Zimenezi zidzachitika ngati mudzamvera mwachangu Yehova Mulungu wanu.”
And those who are far off shall come and build in the temple of Jehovah. And ye shall know that Jehovah of hosts has sent me to you. And this shall come to pass, if ye will diligently obey the voice of Jehovah your God.

< Zekariya 6 >