< Zekariya 4 >

1 Kenaka mngelo amene amayankhula nane anabwerera nandidzutsa, ngati mmene amadzutsira munthu amene ali mʼtulo.
And the agent who talked with me came again, and awoke me, as a man who is awakened out of his sleep.
2 Anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ine ndikuona choyikapo nyale, chonse chagolide ndi mbale pamwamba pake ndi nyale zoyaka zisanu ndi ziwiri, iliyonse ili ndi zibowo zisanu ndi ziwiri zolowetsera zingwe zoyatsira.
And he said to me, What do thou see? And I said, I have seen, and, behold, a lampstand all of gold, with its bowl upon the top of it, and its seven lamps on it. There are seven pipes to each of the lamps, which are upon the top of it,
3 Ndiponso pambali pake pali mitengo ya olivi iwiri, umodzi uli kumanja kwa mbaleyo ndipo winawo kumanzere.”
and two olive trees by it, one upon the right side of the bowl, and the other upon the left side of it.
4 Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi nʼchiyani mbuye wanga?”
And I answered and spoke to the agent who talked with me, saying, What are these, my lord?
5 Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ndinayankha kuti, “Ayi mbuye wanga.”
Then the agent who talked with me answered and said to me, Do thou not know what these are? And I said, No, my lord.
6 Choncho iye anandiwuza kuti, “Mawu a Yehova kwa Zerubabeli ndi awa: ‘Osati mwa nkhondo kapena ndi mphamvu, koma ndi Mzimu wanga,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Then he answered and spoke to me, saying, This is the word of Jehovah to Zerubbabel, saying, Not by might, nor by power, but by my Spirit, says Jehovah of hosts.
7 “Kodi ndiwe yani, iwe phiri lamphamvu? Pamaso pa Zerubabeli udzasanduka dziko losalala. Pamenepo adzabweretsa mwala wotsiriza. Akamadzawuyika pamwamba anthu adzafuwula kuti, ‘Mulungu adalitse Nyumbayi! Mulungu adalitse Nyumbayi!’”
Who are thou, O great mountain? Before Zerubbabel thou shall become a plain, and he shall bring forth the top stone with shoutings of Grace, grace, to it.
8 Ndipo Yehova anayankhulanso nane kuti,
Moreover the word of Jehovah came to me, saying,
9 “Manja a Zerubabeli ndiwo ayika maziko a Nyumbayi; adzatsiriza ndi manja ake omwewo. Pamenepo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse ndiye anakutuma.
The hands of Zerubbabel have laid the foundation of this house. His hands shall also finish it. And thou shall know that Jehovah of hosts has sent me to you.
10 “Ndani wanyoza tsiku la zinthu zazingʼono? Anthu adzasangalala akadzaona chingwe choyezera mʼmanja mwa Zerubabeli. (“Nyale zisanu ndi ziwirizi ndi maso a Yehova, amene amayangʼanayangʼana pa dziko lapansi.”)
For who has despised the day of small things? For these seven shall rejoice, and shall see the plummet in the hand of Zerubbabel, the eyes of Jehovah, which run to and fro through the whole earth.
11 Kenaka ndinafunsa mngelo uja kuti, “Kodi mitengo ya olivi iwiri ili kumanja ndi kumanzere kwa choyikapo nyalechi ikutanthauza chiyani?”
Then I answered, and said to him, What are these two olive trees upon the right side of the lampstand and upon the left side of it?
12 Ndinamufunsanso kuti, “Kodi nthambi ziwiri za mtengo wa olivi zomwe zili pambali pa mipopi yodzera mafuta iwiri yagolide zikutanthauza chiyani?”
And I answered the second time, and said to him, What are these two olive-branches, which are beside the two golden spouts that empty the golden oil out of themselves?
13 Iye anandiyankha kuti, “Kodi iwe sukuzidziwa zimenezi?” Ine ndinati, “Ayi mbuye wanga.”
And he answered me and said, Do thou not know what these are? And I said, No, my lord.
14 Choncho iye anati, “Amenewa ndi anthu awiri amene adzozedwa kuti atumikire Ambuye pa dziko lonse lapansi.”
Then he said, These are the two anointed ones, who stand by the Lord of the whole earth.

< Zekariya 4 >