< Zekariya 1 >

1 Mwezi wachisanu ndi chitatu, mʼchaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi mneneri Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido, kuti:
La seconde année du règne de Darius, au huitième mois, la parole de l'Éternel fut adressée au prophète Zacharie, fils de Barachie, fils d'Iddo, en ces mots:
2 “Yehova anakwiya kwambiri ndi makolo anu.
L'Éternel a été fort indigné contre vos pères.
3 Choncho awuze anthuwa kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Bwererani kwa Ine,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
Tu leur diras donc: Ainsi a dit l'Éternel des armées: Revenez à moi, dit l'Éternel des armées, et je reviendrai à vous, dit l'Éternel des armées.
4 Musakhale ngati makolo anu, amene aneneri akale anawalalikira kuti: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Tsopano lekani njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu oyipawo.’ Koma iwo sanamvere kapena kulabadira za Ine, akutero Yehova.
Ne soyez pas comme vos pères, que les premiers prophètes ont appelés, en disant: Ainsi a dit l'Éternel des armées: Détournez-vous de vos voies mauvaises et de vos mauvaises actions; mais ils n'ont pas écouté, ils n'ont point fait attention à ma parole, dit l'Éternel.
5 Kodi makolo anuwo ali kuti tsopano? Nanga aneneri, kodi amakhalapo mpaka muyaya?
Vos pères, où sont-ils? Et ces prophètes devaient-ils toujours vivre?
6 Kodi mawu anga ndi malangizo anga, amene ndinawawuza atumiki anga aneneri, suja anawachitira makolo anu? “Tsono iwo analapa ndi kunena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse watichitira zomwe zikuyenera njira zathu ndi machitidwe athu, monga anatsimikiza kuti adzachita.’”
Cependant mes paroles et mes ordres, que j'avais donnés aux prophètes mes serviteurs, ne se sont-ils pas accomplis sur vos pères? Ils sont revenus, et ils ont dit: Tout ce que l'Éternel des armées avait résolu de nous faire, selon nos voies et selon nos actions, il l'a exécuté sur nous.
7 Tsiku la 24 la mwezi wa 11, mwezi wa Sebati, chaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido.
Le vingt-quatrième jour du onzième mois, qui est le mois de Shébat, la seconde année de Darius, la parole de l'Éternel fut adressée au prophète Zacharie, fils de Barachie, fils d'Iddo, en ces mots:
8 Nthawi ya usiku ndinaona masomphenya. Ndinaona munthu atakwera pa kavalo wofiira. Iye anayima pakati pa mitengo ya mchisu mʼchigwa. Kumbuyo kwake kunali akavalo ofiira, akhofi ndi oyera.
J'eus la nuit une vision; et voici, un homme monté sur un cheval roux; il se tenait parmi les myrtes qui étaient dans le fond; et, après lui, des chevaux roux, bais et blancs.
9 Ine ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, kodi zimenezi ndi chiyani?” Mngelo amene amayankhula nane anayankha kuti, “Ndidzakuonetsa kuti zimenezi ndi chiyani.”
Et je dis: Mon Seigneur, qui sont-ils? Et l'ange qui me parlait me dit: Je vais te faire voir ce que sont ces chevaux.
10 Pamenepo munthu amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu anafotokoza kuti, “Amenewa ndiwo amene Yehova wawatuma kuti ayendere dziko lonse lapansi.”
Et l'homme qui se tenait parmi les myrtes, répondit et dit: Ce sont ceux que l'Éternel a envoyés pour parcourir la terre.
11 Ndipo okwera pa akavalo enawo anafotokoza kwa mngelo wa Yehova, amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu kuti, “Ife tayendera dziko lonse lapansi ndipo tapeza kuti dziko lonselo lili pa bata ndi mtendere.”
Et ils répondirent à l'ange de l'Éternel, qui se tenait parmi les myrtes, et dirent: Nous avons parcouru la terre; et voici, toute la terre est tranquille et en repos.
12 Tsono mngelo wa Yehova anati, “Yehova Wamphamvuzonse, kodi mpaka liti mudzakhala osaonetsa chifundo chanu kwa Yerusalemu ndi mizinda ya Yuda, amene mwawakwiyira kwa zaka izi 70?”
Alors l'ange de l'Éternel répondit et dit: Éternel des armées! jusqu'à quand n'auras-tu pas compassion de Jérusalem et des villes de Juda, contre lesquelles tu es indigné depuis soixante et dix ans?
13 Choncho Yehova anayankhula mawu abwino ndi achitonthozo kwa mngelo amene ankayankhula nane.
Et l'Éternel répondit à l'ange qui me parlait, de bonnes paroles, des paroles de consolation.
14 Pamenepo mngelo amene ankayankhula nane anati, “Lengeza mawu awa: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndikuchitira nsanje Yerusalemu ndi Ziyoni,
Et l'ange qui me parlait me dit: Crie, et dis: Ainsi a dit l'Éternel des armées: Je suis jaloux pour Jérusalem, pour Sion, d'une grande jalousie;
15 koma ndakwiya kwambiri ndi anthu a mitundu ina amene akuganiza kuti ali pa mtendere. Ndinakwiyira anthu anga pangʼono pokha, koma iwo anawonjeza kuzunza anthu angawo.’
Et je suis courroucé d'un grand courroux contre ces nations tranquilles; car, lorsque j'étais un peu courroucé, elles ont aidé au mal.
16 “Choncho, Yehova akuti, ‘Ndidzabwerera ku Yerusalemu ndi mtima wachifundo, nyumba yanga adzayimanganso kumeneko. Ndipo adzatenganso chingwe choyezera kuti amange Yerusalemu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
C'est pourquoi, ainsi a dit l'Éternel: Je reviens vers Jérusalem avec compassion; ma maison y sera rebâtie, dit l'Éternel des armées, et le cordeau sera étendu sur Jérusalem.
17 “Lengezanso kuti, Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Mizinda yanga idzakhalanso ndi zokoma zosefukira ndipo Yehova adzatonthoza Ziyoni ndi kusankhanso Yerusalemu.’”
Crie encore, et dis: Ainsi a dit l'Éternel des armées: Mes villes regorgeront encore de biens, et l'Éternel consolera encore Sion, et il élèvera encore Jérusalem.
18 Kenaka ndinayangʼananso, ndipo patsogolo panga panali nyanga zinayi.
Puis je levai les yeux et regardai; et je vis quatre cornes.
19 Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi ndi chiyani?” Iye anandiyankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda, Israeli ndi Yerusalemu.”
Et je dis à l'ange qui me parlait: Qu'est-ce que ces cornes? Et il me dit: Ce sont les cornes qui ont dispersé Juda, Israël et Jérusalem.
20 Kenaka Yehova anandionetsa amisiri azitsulo anayi.
Puis l'Éternel me fit voir quatre forgerons.
21 Ndinafunsa kuti, “Amisiri a zitsulowa akudzachita chiyani?” Iye anayankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda kotero kuti panalibe wina amene akanalimbana nazo, koma amisiri a zitsulowa abwera kudzaziopseza ndi kugwetsa nyanga zimenezi za mitundu ya anthu amene analimbana ndi dziko la Yuda ndi kubalalitsa anthu ake.”
Et je dis: Qu'est-ce que ceux-ci viennent faire? Et il répondit: Ce sont là les cornes qui ont dispersé Juda, tellement que personne n'osait lever la tête; mais ceux-ci sont venus pour les effrayer, pour abattre les cornes des nations, qui ont levé la corne contre le pays de Juda pour le disperser.

< Zekariya 1 >