< Nyimbo ya Solomoni 6 >

1 Iwe wokongola kuposa akazi onsewa, kodi wokondedwa wakoyo wapita kuti? Kodi wokondedwa wakoyo wakhotera njira iti kuti timufunefune pamodzi ndi iwe?
Where has thy beloved gone, O thou fairest among women? Where has thy beloved turned, that we may seek him with thee?
2 Wachikondi wanga watsikira ku munda kwake, ku timinda ta zokometsera zakudya, akukadyetsa ziweto zake ku minda, ndiponso akuthyola maluwa okongola.
My beloved has gone down to his garden, to the beds of spices, to feed in the gardens, and to gather lilies.
3 Wokondedwa wangayo ndine wake ndipo iyeyo ndi wangawanga; amadyetsa ziweto zake pakati pa maluwa okongola.
I am my beloved's, and my beloved is mine. He feeds among the lilies.
4 Ndiwe wokongola, bwenzi langa, ngati Tiriza, wokongola kwambiri ngati Yerusalemu, ndiwe woopsa ngati gulu lankhondo lonyamula mbendera.
Thou are fair, O my love, as Tirzah, comely as Jerusalem, sublime as an army with banners.
5 Usandipenyetsetse; pakuti maso ako amanditenga mtima. Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.
Turn away thine eyes from me, for they have overcome me. Thy hair is as a flock of goats that lie along the side of Gilead.
6 Mano ako ali ngati gulu la nkhosa zimene zikubwera kuchokera kokazisambitsa, iliyonse ili ndi ana amapasa, palibe imene ili yokha.
Thy teeth are like a flock of ewes, which have come up from the washing, of which every one has twins, and none is bereaved among them.
7 Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutu, masaya ako ali ngati mabandu a makangadza.
Thy temples are like a piece of a pomegranate behind thy veil.
8 Ngakhale patakhala akazi a mfumu 60, ndi azikazi 80, ndi anamwali osawerengeka;
There are sixty queens, and eighty concubines, and virgins without number.
9 koma nkhunda yanga, wangwiro wanga ndi wosiyana ndi wina aliyense; mwana wamkazi yekhayo wa amayi ake, mwana wapamtima wa amene anamubereka. Anamwali anamuona ndipo anamutcha wodala; akazi a mfumu ndi azikazi anamutamanda.
My dove, my undefiled, is but one. She is the only one of her mother. She is the choice one of her who bore her. The daughters saw her, and called her blessed, yea, the queens and the concubines, and they praised her.
10 Ndani uyu akuoneka ngati mʼbandakucha, wokongola ngati mwezi, wowala ngati dzuwa, wochititsa mantha ngati gulu la ankhondo mbendera zili mʼmanja?
Who is she who looks forth as the morning, fair as the moon, clear as the sun, sublime as an army with banners?
11 Ndinatsikira ku munda wa mitengo ya alimondi kukayangʼana zomera zatsopano ku chigwa, kukaona ngati mpesa waphukira kapena ngati makangadza ali ndi maluwa.
I went down into the garden of nuts, to see the green plants of the valley, to see whether the vine budded, and the pomegranates were in flower.
12 Ndisanazindikire kanthu, ndinakhala ngati ndikulota kuti ndili mʼgaleta pambali pa mfumu yanga.
Before I was aware, my soul set me among the chariots of my princely people.
13 Bwerera, bwerera iwe namwali wa ku Sulami; bwerera, bwerera kuti ife tidzakupenyetsetse iwe! Mwamuna Chifukwa chiyani mukufuna kudzapenyetsetsa ine mwana wamkazi wa ku Sulami, pamene ndikuvina pakati pa magulu awiri?
Return, return, O Shulammite, return, return, that we may look upon thee. Why will ye look upon the Shulammite, as upon the dance of two armies?

< Nyimbo ya Solomoni 6 >