< Nyimbo ya Solomoni 3 >

1 Usiku wonse ndili pa bedi langa ndinafunafuna amene mtima wanga umamukonda; ndinamufunafuna koma osamupeza.
By night on my bed I sought him whom my soul loves. I sought him, but I did not find him.
2 Ndikudzuka tsopano ndipo ndidzayendayenda mu mzinda, mʼmisewu yake ndi mʼmabwalo ake; ndidzamufunafuna amene mtima wanga umamukonda. Kotero ine ndinamufunafuna iyeyo koma osamupeza.
I said, I will rise now, and go around the city. In the streets and in the broad ways I will seek him whom my soul loves. I sought him, but I did not find him.
3 Alonda anandipeza pamene ankayendera mzinda. “Kodi mwamuonako amene mtima wanga umamukonda?”
The watchmen who go about the city found me. I said, Did ye see him whom my soul loves?
4 Nditawapitirira pangʼono ndinamupeza amene mtima wanga umamukonda. Ndinamugwira ndipo sindinamulole kuti achoke mpaka nditamulowetsa mʼnyumba ya amayi anga, mʼchipinda cha amene anandibereka.
It was but a little that I passed from them when I found him whom my soul loves. I held him, and would not let him go until I had brought him into my mother's house, and into the chamber of her who conceived me.
5 Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo: Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa mpaka pamene chifunire ichocho.
I adjure you, O daughters of Jerusalem, by the roes, or by the hinds of the field, that ye stir not up, nor awake love, until it please.
6 Kodi ndani amene akubwera kuchokera ku chipululu ngati utsi watolotolo, wonunkhira mure ndi lubani, zopangidwa kuchokera ku zonunkhira zonse za anthu amalonda?
Who is this who comes up from the wilderness like pillars of smoke, perfumed with myrrh and frankincense, with all powders of the merchant?
7 Ona! Chimenecho ndi chonyamulira Solomoni, choperekezedwa ndi asilikali 60, anthu amphamvu a ku Israeli,
Behold, it is the litter of Solomon. Sixty mighty men are around it, of the mighty men of Israel.
8 onse atanyamula lupanga, onse odziwa bwino nkhondo, aliyense ali ndi lupanga pambali pake, kukonzekera zoopsa za usiku.
They all handle the sword, and are expert in war. Every man has his sword upon his thigh, because of fear in the night.
9 Mfumu Solomoni anadzipangira chonyamulirachi; anachipanga ndi matabwa ochokera ku Lebanoni.
King Solomon made himself a palanquin of the wood of Lebanon.
10 Milongoti yake anayipanga yasiliva, kumbuyo kwake kwa golide. Mipando yake inakutidwa ndi nsalu yapepo, anakongoletsa mʼkati mwake ndi chikondi cha akazi a ku Yerusalemu.
He made the pillars thereof of silver, the bottom thereof of gold, the seat thereof of purple, the midst thereof being paved with love, from the daughters of Jerusalem.
11 Tukulani inu akazi a ku Ziyoni ndipo mudzaone mfumu Solomoni atavala chipewa chaufumu, chipewa chaufumu chimene amayi ake anamuveka pa tsiku la ukwati wake, tsiku limene mtima wake unasangalala.
Go forth, O ye daughters of Zion, and behold king Solomon with the crown with which his mother has crowned him in the day of his espousals, and in the day of the gladness of his heart.

< Nyimbo ya Solomoni 3 >